< 2 Mbiri 2 >
1 Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
Süleyman RAB adına bir tapınak, kendisi için de bir saray yaptırmaya karar verdi.
2 Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
Yük taşımak için yetmiş bin, dağlarda taş kesmek için seksen bin, bunlara gözcülük etmek için de üç bin altı yüz kişi görevlendirdi.
3 Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
Sur Kralı Hiram'a da şu haberi gönderdi: “Babam Davut'un oturması için saray yapılırken kendisine gönderdiğin sedir tomruklarından bana da gönder.
4 Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
Tanrım RAB'be adamak üzere, O'nun adına bir tapınak yapıyorum. Bu tapınakta hoş kokulu buhur yakıp adak ekmeklerini sürekli olarak masaya dizeceğiz. Sabah akşam, her Şabat Günü, her Yeni Ay ve Tanrımız RAB'bin belirlediği bayramlarda orada yakmalık sunular sunacağız. İsrail'e bunları sürekli yapması buyruldu.
5 “Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
“Yapacağım tapınak büyük olacak. Çünkü Tanrımız bütün tanrılardan büyüktür.
6 Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
Ama O'na bir tapınak yapmaya kimin gücü yeter? Çünkü O göklere, göklerin göklerine bile sığmaz. Ben kimim ki O'na bir tapınak yapayım! Ancak önünde buhur yakılabilecek bir yer yapabilirim.
7 “Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
“Bana bir adam gönder; Yahuda ve Yeruşalim'de babam Davut'un yetiştirdiği ustalarımla çalışsın. Altın, gümüş, tunç ve demiri işlemede; mor, kırmızı, lacivert kumaş dokumada, oymacılıkta usta olsun.
8 “Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
“Bana Lübnan'dan sedir, çam, algum tomrukları da gönder. Adamlarının oradaki ağaçları kesmekte usta olduklarını biliyorum. Benim adamlarım da seninkilerle birlikte çalışsın.
9 kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
Öyle ki, bana çok sayıda tomruk sağlayabilsinler. Çünkü yapacağım tapınak büyük ve görkemli olacak.
10 Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
Ağaç kesen adamlarına yirmi bin kor bulgur, yirmi bin kor arpa, yirmi bin bat şarap, yirmi bin bat zeytinyağı vereceğim.”
11 Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
Sur Kralı Hiram Süleyman'a mektupla şu yanıtı gönderdi: “RAB halkını sevdiği için, seni onların kralı yaptı.”
12 Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
Hiram mektubunu şöyle sürdürdü: “Yeri göğü yaratan İsrail'in Tanrısı RAB'be övgüler olsun! Kral Davut'a bilge bir oğul verdi; RAB için bir tapınak, kendisi için de bir saray yapacak akıllı ve anlayışlı bir oğul.
13 “Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
“Sana Huram-Avi adında usta ve akıllı birini gönderiyorum.
14 amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
Annesi Danlı, babası Surlu'dur. Altın, gümüş, tunç, demir, taş ve tahta işlemekte; ince keten, mor, lacivert ve kırmızı kumaş dokumakta ustadır. Her türlü oymacılıkta usta olduğu gibi her tasarımı uygulayabilecek yetenektedir. Ustalarınla ve babanın, efendim Davut'un yetiştirdiği ustalarla çalışacak.
15 “Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
“Efendim, sözünü ettiğin buğday, arpa, zeytinyağı ve şarabı kullarına gönder.
16 ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
Biz de sana gereken bütün tomrukları Lübnan'da keser, deniz yoluyla, sallarla Yafa'ya kadar yüzdürürüz. Sonra sen tomrukları alıp Yeruşalim'e götürürsün.”
17 Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
Babası Davut'un yaptığı sayımdan sonra, Süleyman da İsrail'de yaşayan bütün yabancılar arasında bir sayım yaptı. Yabancıların sayısı 153 600 kişi olarak belirlendi.
18 Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.
Bunlardan 70 000'ine yük taşıma, 80 000'ine dağlarda taş kesme, 3 600'üne de işçileri çalıştırma görevi verildi.