< 2 Mbiri 2 >

1 Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
Och Salomo satte sig före att bygga Herrans namne ett hus, och ett sins rikes hus;
2 Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
Och afräknade sjutiotusend män till bördor, och åttatiotusend timbermän uppå berget, och tretusend och sexhundrad befallningsmän öfver dem.
3 Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
Och Salomo sände till Hyram, Konungen i Tyro, och lät säga honom: Såsom du med minom fader David gjorde, och sände honom cedreträ, att han skulle bygga sig ett hus, der han uti bo skulle;
4 Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
Si, jag vill bygga Herrans mins Guds Namne ett hus, att honom må helgadt varda, till att röka god rökverk för honom, och till alltid bereda skådobröd, och bränneoffer om morgon och afton, på Sabbather och nymånader, och på Herrans vår Guds högtider; till evig tid för Israel.
5 “Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
Och det hus, som jag bygga vill, skall vara stort; förty vår Gud är större än alle gudar.
6 Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
Men ho är dess mägtig, att han bygger honom hus? Ty himmelen och alla himlars himlar kunna icke begripa honom. Ho skulle då jag vara, att jag skulle bygga honom hus? Utan att man må röka för honom.
7 “Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
Så sänd mig nu en vis man, till att arbeta på guld, silfver, koppar, jern, skarlakan, rosenrödt, gult silke, och den som kan utgrafva med de visa, som när mig äro i Juda och Jerusalem, hvilka min fader David beställt hafver.
8 “Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
Och sänd mig cedreträ, furoträ och hebenträ af Libanon; förty jag vet, att dine tjenare kunna hugga trä på Libanon; och si, mine tjenare skola vara med dina tjenare;
9 kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
Att man tillreder mig mycket trä; ty huset, som jag bygga vill, skall vara stort och härligit.
10 Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
Och si, jag vill gifva dina tjenare timbermannomen, som trä hugga, tjugutusend corar stött hvete, och tjugutusend corar bjugg, och tjugutusend bath vin, och tjugutusend bath oljo.
11 Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
Då sade Hyram, Konungen i Tyro, genom skrifvelse, och sände till Salomo: Derföre, att Herren hafver sitt folk kärt, hafver han gjort dig till Konung öfver dem.
12 Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
Och Hyram sade ytterligare: Lofvad vare Herren Israels Gud, som himmel och jord gjort hafver, att han gifvit hafver Konung David en visan, klokan och förståndigan son, som Herranom ett hus, och ett sins rikes hus bygga må.
13 “Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
Så sänder jag nu en visan man, som förstånd hafver, nämliga Hyram Abiv;
14 amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
Ene qvinnos son utaf Dans döttrar, och hans fader hade varit en Tyrer; han kan arbeta på guld, silfver, koppar, jern, sten, trä, skarlakan, gult silke, linnet, rosenrödt: och allahanda utgrafva, och göra allahanda konsteliga, det man honom föregifver, med dina visa, och med mins herras Konung Davids dins faders visa.
15 “Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
Så sände nu min herre hvete, bjugg, oljo och vin, till sina tjenare, såsom han sagt hafver;
16 ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
Så vilje vi hugga trä på Libanon, så mycket som behöfves, och vilje låta det lägga i flottar i hafvet, in åt Japho; dädan må du låta föra det upp till Jerusalem.
17 Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
Och räknade Salomo alla främlingar i Israels land, efter det tal då David hans fader dem räknade; och vordo funne hundrade och femtio tusend, tretusend och sexhundrad.
18 Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.
Och han gjorde af dem sjutiotusend dragare, och åttatiotusend huggare på bergena, och tretusend och sexhundrad befallningsmän, som folket vid arbetet höllo.

< 2 Mbiri 2 >