< 2 Mbiri 2 >
1 Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
Then Solomon gave word to build a house for the Name of Yahweh, and a house for his kingdom.
2 Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
And Solomon numbered seventy thousand men to bear burdens, and eighty thousand men to hew in the mountain, —and, to oversee them, three thousand six hundred.
3 Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
And Solomon sent unto Huram king of Tyre, saying, —As thou didst deal with David my father, and didst send him cedars to build him a house to dwell in,
4 Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
lo! I, am about to build a house for the Name of Yahweh my God, to hallow unto him—to burn before him sweet incense, and for a continual setting in array, and to offer ascending-sacrifices morning and evening, on the sabbaths, and on the new moons, and on the appointed feasts of Yahweh our God, -age-abiding, is this [law] for Israel.
5 “Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
And, the house which I am about to build, [must be] great, —for great is our God, above all gods.
6 Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
But who is able to build unto him a house? for, the heavens, even the heaven of heavens, cannot contain him, —who then am, I, that I should build unto him a house, though only to burn incense before him?
7 “Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
Now, therefore, send me a wise man, to work in gold and in silver and in bronze and in iron, and in purple and crimson and blue, and skilful to execute gravings, —with the wise men who are with me, in Judah and in Jerusalem, whom my father David did provide.
8 “Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
And send me—timbers of cedar, cypress and sandal-wood, out of the Lebanon, for, I, know that, thy servants, are skilful, to cut the timbers of Lebanon, —and lo! my servants shall be with thy servants:
9 kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
yea to prepare me timbers in abundance, —for, the house which I am about to build, [must be] great and most wonderful.
10 Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
And lo! for the hewers that cut the timbers, have I given wheat as food for thy servants, twenty thousand measures, and barley, twenty thousand measures, and wine, twenty thousand baths, and oil, twenty thousand baths.
11 Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
Then answered Huram king of Tyre, in writing, which he sent unto Solomon, —Because Yahweh hath loved his people, hath he set thee over them as king.
12 Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
And Huram said, Blessed be Yahweh, God of Israel, who made the heavens and the earth, —who hath given, unto David the king, a wise son, skilled in prudence and understanding, who will build a house for Yahweh, and a house for his kingdom.
13 “Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
Now, therefore, have I sent a wise man, skilled in understanding, pertaining to Huram my father:
14 amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
son of a woman of the daughters of Dan, whose father was a man of Tyre, skilled to work in gold and in silver, in bronze, in iron, in stones and in timber, in purple, in blue and in fine white linen, and in crimson, and to grave any manner of graving, and to devise any manner of device that may be given to him, with thy wise men, and the wise men of my lord David thy father.
15 “Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
Now, therefore, the wheat and the barley, the oil and the wine, whereof my lord hath spoken, let him send unto his servants;
16 ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
and, we, will cut down timbers out of the Lebanon, according to all thy need, and will bring them unto thee in floats, upon the sea to Joppa, —and, thou, shalt fetch them up to Jerusalem.
17 Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
So Solomon numbered all the men that were sojourners, who were in the land of Israel, after the numbering, wherewith David his father had numbered them, —and they were found to be—a hundred and fifty-three thousand and six hundred.
18 Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.
And he made up from among them—seventy thousand, to bear burdens, and eighty thousand to hew in the mountain, —and three thousand and six hundred, as overseers, to keep the people at work.