< 2 Mbiri 2 >

1 Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
And Solomon determined to build a house to the name of the Lord, and a palace for himself.
2 Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
And he numbered out seventy thousand men to bear burdens, and eighty thousand to hew stones in the mountains, and three thousand six hundred to oversee them.
3 Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
He sent also to Hiram king of Tyre, saying: As thou didst with David my father, and didst send him cedars, to build him a house, in which he dwelt:
4 Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
So do with me that I may build a house to the name of the Lord my God, to dedicate it to burn incense before him, and to perfume with aromatical spices, and for the continual setting forth of bread, and for the holocausts, morning and evening, and on the sabbaths, and on the new moons, and the solemnities of the Lord our God for ever, which are commanded for Israel.
5 “Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
For the house which I desire to build, is great: for our God is great above all gods.
6 Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
Who then can be able to build him a worthy house? if heaven, and the heavens of heavens cannot contain him: who am I that I should be able to build him a house? but to this end only, that incense may be burnt before him.
7 “Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
Send me therefore a skillful man, that knoweth how to work in gold, and in silver, in brass, and in iron, in purple, in scarlet and in blue, and that hath skill in engraving, with the artificers, which I have with me in Judea and Jerusalem, whom David my father provided.
8 “Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
Send me also cedars, and fir trees, and pine trees from Libanus: for I know that thy servants are skillful in cutting timber in Libanus, and my servants shall be with thy servants,
9 kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
To provide me timber in abundance. For the house which I desire to build, is to be exceeding great, and glorious.
10 Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
And I will give thy servants the workmen that are to cut down the trees, for their food twenty thousand cores of wheat, and as many cores of barley, and twenty thousand measures of wine, and twenty thousand measures of oil.
11 Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
And Hiram king of Tyre sent a letter to Solomon, saying: Because the Lord hath loved his people, therefore he hath made thee king over them.
12 Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
And he added, saying: Blessed be the Lord the God of Israel, who made heaven and earth, who hath given to king David a wise and knowing son, endued with understanding and prudence, to build a house to the Lord, and a palace for himself.
13 “Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
I therefore have sent thee my father Hiram, a wise and most skillful man,
14 amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
The son of a woman of the daughters of Dan, whose father was a Tyrian, who knoweth how to work in gold, and in silver, in brass, and in iron, and in marble, and in timber, in purple also, and violet, and silk and scarlet: and who knoweth to grave all sort of graving, and to devise ingeniously all that there may be need of in the work with thy artificers, and with the artificers of my lord David thy father.
15 “Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
The wheat therefore, and the barley and the oil, and the wine, which thou, my lord, hast promised, send to thy servants.
16 ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
And we will cut down as many trees out of Libanus, as thou shalt want, and will convey them in floats by sea to Joppe: and it will be thy part to bring them thence to Jerusalem.
17 Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
And Solomon numbered all the proselytes in the land of Israel, after the numbering which David his father had made, and they were found a hundred and fifty-three thousand and six hundred.
18 Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.
And he set seventy thousand of them to carry burdens on their shoulders, and eighty thousand to hew stones in the mountains: and three thousand and six hundred to be overseers of the work of the people.

< 2 Mbiri 2 >