< 2 Mbiri 2 >
1 Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
撒羅滿決定為上主的名建造聖殿,為自己修築王宮。
2 Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
撒羅滿點派了七萬人作運夫,八萬人在山上鑿石,三千六百人作監工。
3 Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
撒羅滿遣使向提洛王希蘭說:「有如你怎樣對待了我父達味,給他運來了香柏木,建造他居住的宮殿,也請你如此對待我。
4 Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
我現今要為上主我的天主的名,建造一座聖殿,奉獻給他,在他面前焚燒芬芳的香料,永遠獻上供餅,每日早晚、安息日、月朔,以及上主我們天主的節日,奉獻全燔祭:這為以色列人是永久的事。
5 “Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
我建造的殿宇必須廣大,因為我們的天父大於諸神。
6 Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
然而,誰有能力為他建造一座殿宇﹖天與諸天之天,尚容不下他。我是誰,竟能為他建造殿宇﹖不過只是為在他面前焚香罷了!
7 “Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
現在,請你給我派一位技師來,他要精於金、銀、銅、鐵,以及紫紅、朱紅、藍線等工作;並且還應會各種雕刻,好與我父親達味在猶大和耶路撒冷所準備的技術人員一同工作。
8 “Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
請你由黎巴嫩給我運香柏、松柏和檀香木來,因為我知道你的僕人善於砍伐黎巴嫩的木材;我的僕人將與你的僕人一同工作。
9 kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
他們要為我大量預備木材,因為我要建造的殿宇極其廣大。
10 Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
至於你那些伐木砍樹的僕人,我必供給他們食糧,小麥二萬「苛爾,」大麥二萬「苛爾,」酒兩萬「巴特,」油兩萬「巴特。」[提洛王應允合作]
11 Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
提洛王希蘭回信給撒羅滿說:「上主由於愛慕自己的百姓,所以立你作了他們的君王。」
12 Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
希蘭又說:「創造天地的上主以色列的天主應受讚美! 因為他賜給了達味王一個智慧的兒子,聰明機敏,可為上主建造殿宇,為自己修築無宮。
13 “Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
我現在打發一個具有智慧和才學的人去,他名叫胡蘭阿彼,
14 amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
是一丹支派女人的兒子,他父親是提洛人,他精於金、銀、銅、鐵、石、木紫色、紅色、藍色、細麻,以及朱紅線各種工作,善於各種雕刻,又能設計各種托於他的技工。這人可與你的技師和你父親我主達味的技師,一同工作。
15 “Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
我主談及的小麥、大麥、油和酒,請即運來分配給僕人。
16 ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
我們必照你所需要的,在黎巴嫩砍伐樹木,編成木筏,由海上運到約培;以後你運到耶路撒冷。選派工匠
17 Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
撒羅滿按照他父親達味所統計過的數目,又統計了住在以色列境內的一切外方人,共計十五萬三千六百人,
18 Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.
委派其中的七萬人作運夫,八萬人在山上鑿石,安千六百人作監工,督促人民工作。