< 2 Mbiri 19 >

1 Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
Kong Josafat af Juda derimod vendte uskadt hjem igen til sit Palads i Jerusalem.
2 mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
Da trådte Seeren Jehu, Hananis Søn, frem for ham, og han sagde til Kong Josafat: "Skal man hjælpe de ugudelige? Elsker du dem, der hader HERREN? For den Sags Skyld er HERRENs Vrede over dig!
3 Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
Noget godt er der dog hos dig, thi du har udryddet Asjererne af Landet, og du har vendt dit Hjerte til at søge Gud."
4 Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Josafat blev nu i Jerusalem, Så drog han atter ud blandt Folket fra Be'ersjeba til Efraims Bjerge og førte dem tilbage til HERREN, deres Fædres Gud.
5 Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
Og han indsatte Dommere i Landet i hver enkelt af de befæsfede Byer i Juda.
6 Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
Og han sagde til Dommerne: "Se til, hvad I gør, thi det er ikke for Mennesker, men for HERREN, I fælder Dom, og han er hos eder, når I afsiger Hendelser.
7 Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
Derfor være HERRENs Frygt over eder! Vær varsomme med, hvad I foretager eder, thi hos HERREN vor Gud er der hverken Uret eller Personsanseelse, ej heller tager han imod Bestikkelse!"
8 Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
Også i Jerusalem indsatte Josafat nogle af Leviterne, Præsterne og Overhovederne for Israels Fædrenehuse til at dømme i HERRENs Sager og i Stridigheder mellem Jerusalems Indbyggere.
9 Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
Og han bød dem: "Således skal I gøre i HERRENs Frygt, i Sanddruhed og med redeligt Hjerte:
10 Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
Hver Gang der forelægges eder en Retssag af eders Brødre, der bor i deres Byer, hvad enten det drejer sig om Blodskyld eller om Love, Anordninger og Lovbud, skal I hjælpe dem til Rette, at de ikke skal pådrage sig Skyld forHERREN, så der kommer Vrede over eder og eders Brødre; gør således for ikke at pådrage eder Skyld.
11 “Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”
I alle HERRENs Sager skal Ypperstepræsten Amarja være eders foresatte, i alle Kongens Sager Zebadja, Jisjmaels Søn, Fyrsten i Judas Hus; og Leviterne står eder til Tjeneste som Retsskrivere. Gå nu frimodigt til Værket, HERREN vil være med enhver, der gør sin Pligt."

< 2 Mbiri 19 >