< 2 Mbiri 19 >
1 Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
Men Josafat, Judas Konge, kom tilbage til sit Hus med Fred til Jerusalem.
2 mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
Og Jehu, Hananis Søn, Seeren, gik ud imod ham og sagde til Kong Josafat: Skal du hjælpe den ugudelige og elske dem, som hade Herren? derfor er der Vrede over dig fra Herrens Ansigt.
3 Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
Dog er der nogle gode Ting fundne hos dig, at du har borttaget Astartebillederne af Landet og beredet dit Hjerte til at søge Gud.
4 Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Saa blev Josafat i Jerusalem; og han drog ud igen iblandt Folket fra Beersaba indtil Efraims Bjerg og førte dem tilbage til Herren, deres Fædres Gud.
5 Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
Og han beskikkede Dommere i Landet, i alle Judas faste Stæder, i hver Stad.
6 Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
Og han sagde til Dommerne: Ser til, hvad I gøre, thi I holde ikke Dom for et Menneske, men for Herren; og han er med eder i Dommens Handel.
7 Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
Derfor lader nu Herrens Frygt være over eder; tager eder i Agt, i hvad I gøre; thi der er ingen Uret hos Herren vor Gud, ej heller Persons Anseelse, ej heller Gavers Annammelse.
8 Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
Tilmed beskikkede Josafat ogsaa i Jerusalem nogle af Leviterne og Præsterne og af Øversterne for Fædrenehusene iblandt Israel til at dømme i Herrens Sager og i Tvistigheder. Og de vendte tilbage til Jerusalem.
9 Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
Og han bød dem og sagde: Gører saa i Herrens Frygt, trolig og med et retskaffent Hjerte!
10 Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
Og ved alle Tvistigheder, som komme for eder og fra eders Brødre, som bo i deres Stæder, imellem Blod og Blod, imellem Lov og Bud, Skikke og Forskrifter, skulle I paaminde dem, at de ikke blive skyldige for Herren, og der maatte komme en Vrede over eder og over eders Brødre; gører saa, da skulle I ikke blive skyldige.
11 “Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”
Og se, Ypperstepræsten Amaria er over eder i alle Herrens Sager og Sebadja, Ismaels Søn, Fyrsten i Judas Hus, i alle Kongens Sager, saa ere og Leviterne Fogeder for eders Ansigt; værer frimodige og gører dette, og Herren skal være med den gode.