< 2 Mbiri 18 >

1 Tsono Yehosafati anali ndi chuma chambiri ndi ulemu, ndipo iye anachita mgwirizano wa ukwati ndi Ahabu.
And Jehoshaphat had riches and honor in abundance, and he intermarried with Achab.
2 Patapita zaka zina, iye anapita kukacheza kwa Ahabu mu Samariya. Ahabu anaphera iye pamodzi ndi anthu amene anali naye, nkhosa zambiri ndi ngʼombe ndipo anamuwumiriza kuti akathire nawo nkhondo Ramoti Giliyadi
And he went down after [some] years to Achab to Samaria. And Achab killed for him sheep and oxen in abundance, and for the people that were with him, and persuaded him to go up to Ramoth-gil'ad.
3 Ahabu mfumu ya Israeli anafunsa Yehosafati mfumu ya Yuda kuti, “Kodi mudzapita nane kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha kuti, “Ine ndili ngati inu nomwe, ndi anthu anga ngati anthu anu. Ife tikhala nanu limodzi pa nkhondoyi.”
Then said Achab the king of Israel unto Jehoshaphat the king of Judah, Wilt thou go with me against Ramoth-gil'ad! And he said to him, I [will be] like thee, and my people [shall be] as thy people; and we will be with thee in the battle.
4 Koma Yehosafati anatinso kwa mfumu ya Israeli, “Choyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
And Jehoshaphat said unto the king of Israel, Inquire, I pray thee, today [first] of the word of the Lord.
5 Tsono mfumu ya Israeli inasonkhanitsa aneneri 400 ndipo inawafunsa kuti, “Kodi tipite kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Mulungu adzawupereka mʼdzanja la mfumu.”
Then did the king of Israel assemble the prophets, four hundred men, and said unto them, Shall we go to Ramoth-gil'ad to battle, or shall I forbear? And they said, Go up, and God will deliver [it] into the hand of the king.
6 Koma Yehosafati anafunsanso kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wina wa Yehova amene ife tingafunsireko?”
And Jehoshaphat said, Is there not here a prophet of the Eternal besides, that we might inquire of him?
7 Mfumu ya Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife kudzera mwa iye titha kufunsira kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa sandilosera zabwino koma zoyipa nthawi zonse. Iyeyu ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu isanene motero.”
And the king of Israel said unto Jehoshaphat, There is yet one man, by whom we may inquire of the Lord; but I hate him; for he never prophesieth any good concerning me, but at all times evil: it is Michayhu the son of Yimla. And Jehoshaphat said, Let not the king say so.
8 Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa akuluakulu ake ndipo inati, “Kamutengeni Mikaya mwana wa Imula, abwere msanga.”
Then called the king of Israel a certain court-officer, and said, “Hasten hither Michayhu the son of Yimla.”
9 Mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda, atavala mikanjo yawo yaufumu anali atakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopunthira tirigu pa khomo la chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
And the king of Israel and Jehoshaphat the king of Judah were sitting each on his throne, dressed in their royal garments, and they were sitting in a threshing-floor at the entrance of the gate of Samaria: and all the prophets prophesied before them.
10 Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana anapanga nyanga zachitsulo ndipo analengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi udzagunda Aaramu mpaka atawonongedwa!’”
And Zedekiah the son of Kena'anah had made himself horns of iron; and he said, Thus hath said the Lord, With these shalt thou push the Syrians until thou have made an end of them.
11 Aneneri ena onse amanenera chimodzimodzi kuti, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo kapambaneni, pakuti Mulungu adzamupereka mʼdzanja la mfumu.”
And all the prophets prophesied so, saying, Go up against Ramoth-gil'ad, and prosper, and the Lord will deliver it into the king's hand.
12 Wauthenga amene anapita kukayitana Mikaya anati kwa iye, “Taonani aneneri ena onse ngati munthu mmodzi akulosera za chipambano cha mfumu. Mawu anunso agwirizane ndi awo ndipo muyankhule zabwino.”
And the messenger that went to call Michayhu spoke to him, saying, Behold, the words of the prophets are with one voice good for the king: so do let thy word, I pray thee, be like [that of] any one of them, and speak something good.
13 Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndidzanena zimene Mulungu wanga andiwuze.”
And Michayhu said, As the Lord liveth, truly what my God may say, that will I speak.
14 Iye atafika mfumu inamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite ku nkhondo kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Kathireni nkhondo ndipo kapambaneni, pakuti mzindawo udzaperekedwa mʼdzanja lanu.”
And when he was come to the king, the king said unto him, Michah, shall we go to Ramoth-gil'ad to battle, or shall I forbear? And he said, Go ye up, and prosper, and may they be delivered into your hand.
15 Mfumu inati kwa iye, “Kodi ndikuwuze kangati kuti ulumbire kuti usandiwuze chilichonse koma zoonadi mʼdzina la Yehova?”
And the king said to him, How many times yet must I adjure thee that thou shalt not speak to me any thing but the truth in the name of the Lord?
16 Ndipo Mikaya anayankha kuti, “Ine ndinaona Aisraeli atabalalika mʼmapiri monga nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mu mtendere!’”
Then said he, I saw all Israel scattered over the mountains, as flocks that have not a shepherd: and the Lord said, These have no master; let them return every man to his house in peace.
17 Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti sandinenera zabwino koma zoyipa zokhazokha?”
And the king of Israel said to Jehoshaphat, Did I not say unto thee that he would not prophesy concerning me any good, but [only] for evil?
18 Mikaya anapitiriza ndi kunena kuti, “Imvani tsono mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu ndi gulu lonse lakumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi lamanzere.
And he said, Therefore hear ye the word of the Lord: I saw the Lord sitting on his throne, and all the host of heaven standing on his right and his left.
19 Ndipo Yehova anati, ‘Ndani amene adzamunyengerere Ahabu mfumu ya Israeli kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi ndi kukafera komweko?’ “Wina ananena zina, winanso ananena zina.”
And the Lord said, Who will persuade Achab the king of Israel, that he may go up and fall at Ramoth-gil'ad? And one said—one saying after this manner, and another saying after that manner.
20 Pomaliza mzimu wina unatuluka ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, “Ine ndikamunyengerera!” Yehova anafunsa kuti, “Ukagwiritsa ntchito njira yanji?”
Then came there forth a spirit, and placed himself before the Lord, and said, I will persuade him. And the Lord said unto him, Wherewith?
21 Mzimuwo unati, “Ine ndidzapita ndi kukhala mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri ake onse!” Yehova anati, “‘Iwe ukamunyengadi iyeyo. Pita kachite zimenezo.’
And he said, I will go forth, and I will become a lying spirit in the mouth of all his prophets. And he said, Thou wilt persuade him, and also prevail: go forth, and do so.
22 “Choncho Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anuwa. Yehova waneneratu kuti inu mukaona tsoka.”
And now, behold, the Lord hath put a lying spirit in the mouth of these thy prophets: but the Lord hath spoken evil concerning thee.
23 Ndipo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi ndi kumenya khofi Mikaya. Zedekiya anafunsa kuti, “Kodi mzimu wochokera kwa Yehova unadzera njira iti pamene unachoka kwa ine kupita kwa iwe?”
And Zedekiah the son of Kena'anah went near, and struck Michayhu on the cheek, and said, Which is the way the Spirit of the Lord passed away from me to speak with thee?
24 Mikaya anayankha kuti, “Udzadziwa pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
And Michayhu said, Behold, thou shalt see it on that day when thou shalt go into the innermost chamber to hide thyself.
25 Pamenepo mfumu ya Israeli inalamula kuti, “Tengani Mikaya ndipo mupite naye kwa Amoni, wolamulira mzindawo ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu,
And the king of Israel said, Take ye Michayhu, and carry him back unto Amon the governor of the city, and to Joash the king's son;
26 ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyike munthu uyu mʼndende ndipo musamupatse kanthu kalikonse koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwera mwamtendere.’”
And say ye, Thus hath said the king, Put this man in the prison, and feed him with sparing bread and with sparing water, until I return in peace.
27 Mikaya anayankhula kuti, “Ngati inu mukabwera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo anawonjeza kuti, “Anthu nonsenu, mumve zimene ndanenazi.”
And Michayhu said, If thou return at all in peace, then hath the Lord not spoken through me. And he said, Hear it, O all ye nations!
28 Choncho mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
And the king of Israel went up with Jehoshaphat the king of Judah to Ramoth-gil'ad.
29 Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Ine ndipita ku nkhondo modzibisa koma iwe uvale mikanjo yaufumu.” Kotero mfumu ya Israeli inadzibisa ndipo inapita ku nkhondoko.
And the king of Israel said unto Jehoshaphat, I will disguise myself, and enter into the battle; but do thou put on thy royal garments. And the king of Israel disguised himself, and they went into the battle.
30 Tsono mfumu ya Aramu inalamulira olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu koma mfumu ya Israeli yokha.”
And the king of Syria had commanded the captains of the chariots that he had, saying, Fight ye not with the small or with the great, save only with the king of Israel alone.
31 Olamulira magaleta ataona Yehosafati, iwo anaganiza kuti, “Mfumu ya Israeli ndi iyi.” Kotero anatembenuka kukamenyana naye koma Yehosafati anafuwula, ndipo Yehova anamuthandiza. Mulungu anawabweza mʼmbuyo,
And it came to pass, when the captains of the chariots saw Jehoshaphat, that they said, This is the king of Israel. And they encompassed him to fight; and Jehoshaphat cried out, and the Lord helped him; and God induced them to go away from him.
32 pakuti olamulira magaleta ataona kuti sanali mfumu ya Israeli, anasiya kumuthamangitsa.
And it came to pass, when the captains of the chariots perceived that it was not the king of Israel, that they turned back from following him.
33 Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndipo analasa mfumu ya Israeli pakati polumikizira malaya achitsulo. Mfumu inawuza oyendetsa galeta kuti, “Bwerera, undichotse pa nkhondo pano. Ndavulazidwa.”
But a certain man drew his bow at a venture, and struck the king of Israel between the joints and the armor: wherefore he said to the chariot-driver, Turn about, and carry me out of the camp; for I am wounded.
34 Nkhondo inakula kwambiri tsiku lonse, ndipo mfumu ya Israeli inakhala tsonga mʼgaleta lake kuyangʼanana ndi Aaramu mpaka madzulo. Ndipo pamene dzuwa linkalowa inamwalira.
And the battle increased on that day: and the king of Israel stayed [himself] up in the chariot against the Syrians until the evening, and he died at the time of the sun's going down.

< 2 Mbiri 18 >