< 2 Mbiri 17 >
1 Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
UJehoshafathi indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe; waziqinisa ukumelana loIsrayeli.
2 Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
Wasebeka amabutho kuyo yonke imizi ebiyelweyo yakoJuda; wabeka lamabutho enqaba elizweni lakoJuda, lemizini yakoEfrayimi uyise uAsa ayeyithumbile.
3 Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
INkosi yasisiba loJehoshafathi, ngoba wahamba ngendlela zakuqala zikaDavida uyise, kabadinganga oBhali;
4 Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
kodwa wadinga kuNkulunkulu kayise, wahamba ngemilayo yakhe, njalo kungenjengokwenza kukaIsrayeli.
5 Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
Ngakho iNkosi yawuqinisa umbuso esandleni sakhe, loJuda wonke waletha izipho kuJehoshafathi; wasesiba lenotho lodumo ngobunengi.
6 Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
Inhliziyo yakhe yasiphakama ezindleleni zeNkosi; futhi-ke wasusa indawo eziphakemeyo lezixuku koJuda.
7 Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
Langomnyaka wesithathu wokubusa kwakhe wathuma kuziphathamandla zakhe, kuBeni-Hayili lakuObhadiya lakuZekhariya lakuNethaneli lakuMikhaya, ukufundisa emizini yakoJuda.
8 Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
Kanye lazo-ke amaLevi, oShemaya loNethaniya loZebhadiya loAsaheli loShemiramothi loJehonathani loAdonija loTobija loTobi-Adonija, amaLevi; kanye labo-ke oElishama loJehoramu, abapristi.
9 Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
Basebefundisa koJuda, belogwalo lomlayo weNkosi; babhoda kuyo yonke imizi yakoJuda, bafundisa abantu.
10 Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
Kwasekusiba lokuyesaba iNkosi phezu kwayo yonke imibuso yamazwe ayehanqe uJuda, okokuthi kayilwanga loJehoshafathi.
11 Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
Labanye bamaFilisti bamlethela uJehoshafathi izipho, lesiliva lokuthela; amaArabhiya lawo amlethela imihlambi, inqama eziyizinkulungwane eziyisikhombisa lamakhulu ayisikhombisa, lezimpongo eziyizinkulungwane eziyisikhombisa lamakhulu ayisikhombisa.
12 Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
UJehoshafathi wayelokhu ekhula njalo, waze waba sengqongeni. Wasesakha koJuda izinqaba lemizi yeziphala.
13 ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
Wayelomsebenzi omnengi emizini yakoJuda, lamadoda empi, amaqhawe alamandla, eJerusalema.
14 Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
Lala ngamanani awo ngezindlu zaboyise: KoJuda, induna zezinkulungwane, uAdina engumphathi, njalo kanye laye amaqhawe alamandla azinkulungwane ezingamakhulu amathathu;
15 otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
leceleni kwakhe uJohanani umphathi, njalo kanye laye izinkulungwane ezingamakhulu amabili lamatshumi ayisificaminwembili;
16 otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
leceleni kwakhe uAmasiya indodana kaZikiri, owazinikela ngesihle eNkosini, njalo kanye laye amaqhawe alamandla azinkulungwane ezingamakhulu amabili.
17 Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
LakoBhenjamini: UEliyada iqhawe elilamandla, njalo kanye laye izinkulungwane ezingamakhulu amabili, ezihlome ngedandili langesihlangu;
18 otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
leceleni kwakhe uJehozabadi, njalo kanye laye izinkulungwane ezilikhulu lamatshumi ayisificaminwembili, abahlomele impi.
19 Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.
Laba babesebenzela inkosi ngaphandle kwalabo inkosi eyayibabeke emizini ebiyelweyo kuye wonke uJuda.