< 2 Mbiri 17 >

1 Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
NOHO alii iho la o Iehosapata kana keiki mahope ona, A hooikaika ka e aku la oia i ka Iseraela.
2 Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
Hoonoho oia i ka poe koa iloko o na kulanakauhale a pau o Iuda i paa i ka pa, a hoonoho hoi i na puali koa ma ka aina o Iuda, a me na kulanakauhale o Eperaima, a Asa kona makuakane i hoopio ai.
3 Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
Aia pu o Iehova me Iehosapata, no ka mea, hele oia ma na aoao mua o Davida o kona kupuna, aole hoi i imi oia ia Baala.
4 Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
Aka, imi aku la oia i ke Akua o kona makuakane; a hele ma kona kanawai, aole e like me ka ka Iseraela hana ana.
5 Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
Nolaila hookupaa iho la o Iehova i ke aupuni ma kona lima; a haawi ka luda a pau i na makana na Iehosapata; a ua nui kona waiwai, a me ka hanohano.
6 Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
A ua ikaika kona naau ma na aoao o Iehova; a wawahi iho la ia i na wahi kiekie, a me na kii no Asetarota ma Iuda.
7 Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
A i ka makahiki ekolu o kona aupuni, hoouna aku la oia i na luna ona, ia Benehaila, a me Obadia, a me Zekaria, a me Nataneela, a me Mikaia, e ao aku iloko o na kulanakauhale o luda.
8 Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
A me lakou pu kekahi poe Levi, o Semaia, a me Netanaia, a me Zebadaia, a me Asahela, a me Semiramota, a me Iehonatana, a me Adonia, a me Tobia, a me Tobaadonia, o na Levi ia; a me lakou pu o Elisama a me Iehorama, na kahuna.
9 Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
A ao aku lakou ma Iuda, a lawe pu me lakou i ka buke o ke kanawai o Iehova, a hele lakou a puni na kulanakauhale a pau o luda, a ao aku i na kanaka.
10 Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
Aia maluna o na aupuni a pau o na aina a puni o Iuda ka eehia ia Iehova, aole hoi i kaua mai lakou me Iehosapata.
11 Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
A o kekahi poe o Pilisetia, lawe mai la lakou io Iehosapata la i na makana, a me ke kala hookupu; a o ko Arabia no hoi kekahi, lawe mai la lakou ia ia i poe holoholona, i na hipa kane ehiku tausani, a me na haneri ehiku, a i na kao kane ehiku tausani a me na haneri ehiku.
12 Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
A lilo iho la o Iehosapata i mea nui loa, a kukulu iho la ia i mau papu ma Iuda, a i mau kulanakauhale waiho ukana.
13 ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
A nui kana hana ma na kulanakauhale o Iuda, a nui hoi na kanaka kaua, ka poe ikaika ma Ierusalema.
14 Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
Eia ka helu ana o lakou ma ka hale o ko lakou poe kupuna. No ka hale o Inda, o na luna tausani; o Adena ka luna, a o ka poe koa ikaika me ia, ekolu haneri tausani
15 otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
A mahope ona, o Iehohanana, ka luna, a o ka poe me ia, elua haneri a me kanawalu tausani.
16 otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
A mahope ona, o Amazia, ke keiki a Zikeri, ka mea hookauwa oluolu na Iehova; a o ka poe kanaka ikaika me ia, elua haneri tausani.
17 Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
No Beniamina, o Eliada he kanaka ikaika, a o ka poe me ia e lawe ana i ke kakaka, a me ka palekaua, elua haneri tausani.
18 otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
A mahope ona o lehozabada, a o ka poe me ia ka poe makaukau ma ke kaua, hookahi haneri me kanawalu tausani.
19 Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.
Oia ka poe lawelawe na ke alii, okoa ka poe a ke alii i waiho ai ma na kulanakauhale paa i ka pa ma Iuda a pau loa.

< 2 Mbiri 17 >