< 2 Mbiri 17 >

1 Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
Then Jehoshaphat, his son, reigned in his place. And he grew strong against Israel.
2 Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
And he appointed numbers of soldiers in all the cities of Judah that had been fortified with walls. And he placed garrisons in the land of Judah, and in the cities of Ephraim that his father Asa had seized.
3 Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
And the Lord was with Jehoshaphat, because he walked in the first ways of his father, David. And he did not trust in the Baals,
4 Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
but in the God of his father. And he advanced in his precepts, and not according to the sins of Israel.
5 Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
And the Lord confirmed the kingdom in his hand. And all of Judah gave gifts to Jehoshaphat. And innumerable riches were brought to him, and much glory.
6 Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
And when his heart had taken courage because of the ways of the Lord, he now also took away the high places and the sacred groves from Judah.
7 Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
Then, in the third year of his reign, he sent Benhail, and Obadiah, and Zechariah, and Nethanel, and Micaiah, from among his leaders, so that they might teach in the cites of Judah.
8 Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
And with them were the Levites Shemaiah and Nethaniah and Zebadiah, and also Asahel and Shemiramoth and Jehonathan, and the Levites Adonijah and Tobijah and Tobadonijah. And with them were the priests Elishama and Jehoram.
9 Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
And they were teaching the people in Judah, having with them the book of the law of the Lord. And they were traveling through all the cities of Judah, and were instructing the people.
10 Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
And so, the fear of the Lord fell upon all the kingdoms of the lands which were around Judah. And they did not dare to make war against Jehoshaphat.
11 Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
Moreover, the Philistines carried gifts to Jehoshaphat, and a tribute in silver. Also, the Arabians brought cattle: seven thousand seven hundred rams, and the same number of he-goats.
12 Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
Therefore, Jehoshaphat increased and was magnified, even on high. And in Judah, he built houses in the likeness of towers, and walled cities.
13 ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
And he prepared many works in the cities of Judah. Also, there were men experienced in warfare in Jerusalem,
14 Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
and this is the number of them, by each of the houses and families. In Judah, the leader of the army was Adnah, the commander; and with him were three hundred thousand very experienced men.
15 otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
After him, Jehohanan was the leader; and with him were two hundred eighty thousand.
16 otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
Also after him, there was Amasiah, the son of Zichri, who was consecrated to the Lord; and with him were two hundred thousand strong men.
17 Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
Following him, there was Eliada, who was experienced in battle; and with him were two hundred thousand, holding bow and shield.
18 otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
Then too, after him, there was Jehozabad; and with him were one hundred eighty thousand lightly-armed soldiers.
19 Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.
All these were at the hand of the king, aside from the others, whom he had positioned in the walled cities, in all of Judah.

< 2 Mbiri 17 >