< 2 Mbiri 16 >

1 Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.
اما در سال سی و ششم سلطنت آسا، بعشا پادشاه اسرائیل بر یهودا برآمد، ورامه را بنا کرد تا نگذارد که کسی نزد آساپادشاه یهودا رفت و آمد نماید.۱
2 Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko.
آنگاه آسا نقره وطلا را از خزانه های خداوند و خانه پادشاه گرفته، آن را نزد بنهدد پادشاه ارام که دردمشق ساکن بود فرستاده، گفت:۲
3 Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”
«در میان من وتو و در میان پدر من و پدر تو عهد بوده است. اینک نقره و طلا نزد تو فرستادم پس عهدی را که با بعشا پادشاه اسرائیل داری بشکن تا او از نزد من برود.»۳
4 Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali.
و بنهدد آسا پادشاه را اجابت نموده، سرداران افواج خود را بر شهرهای اسرائیل فرستاد و ایشان عیون و دان و آبل مایم و جمیع شهرهای خزانه نفتالی را تسخیر نمودند.۴
5 Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo.
وچون بعشا این را شنید بنا نمودن رامه را ترک کرده، از کاری که می‌کرد باز ایستاد.۵
6 Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.
و آساپادشاه، تمامی یهودا را جمع نموده، ایشان سنگهای رامه و چوبهای آن را که بعشا بنا می کرد برداشتند و او جبع و مصفه را با آنها بنانمود.۶
7 Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu.
و در آن زمان حنانی رایی نزد آساپادشاه یهودا آمده، وی را گفت: «چونکه تو برپادشاه ارام توکل نمودی و بر یهوه خدای خود توکل ننمودی، از این جهت لشکر پادشاه ارام از دست تو رهایی یافت.۷
8 Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu.
آیا حبشیان ولوبیان لشکر بسیار بزرگ نبودند؟ و ارابه‌ها وسواران از حد زیاده نداشتند؟ اما چونکه برخداوند توکل نمودی آنها را به‌دست توتسلیم نمود.۸
9 Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”
زیرا که چشمان خداوند درتمام جهان تردد می‌کند تا قوت خویش را برآنانی که دل ایشان با او کامل است نمایان سازد. تو در اینکار احمقانه رفتار نمودی، لهذا ازاین ببعد در جنگها گرفتار خواهی شد.»۹
10 Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.
اماآسا بر آن رایی غضب نموده، او را در زندان انداخت زیرا که از این امر خشم او بر وی افروخته شد و در همان وقت آسا بر بعضی از قوم ظلم نمود.۱۰
11 Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
و اینک وقایع اول و آخر آسا در تورایخ پادشاهان یهودا و اسرائیل مکتوب است.۱۱
12 Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga.
ودر سال سی و نهم سلطنت آسا مرضی درپایهای او عارض شد و مرض او بسیار سخت گردید و نیز در بیماری خود از خداوند مددنخواست بلکه از طبیبان.۱۲
13 Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake.
پس آسا با پدران خود خوابید و در سال چهل و یکم از سلطنت خود وفات یافت.۱۳
14 Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.
و او را در مقبره‌ای که برای خود در شهر داود کنده بود دفن کردندو او را در دخمه‌ای که از عطریات و انواع حنوطکه به صنعت عطاران ساخته شده بودگذاشتند و برای وی آتشی بی‌نهایت عظیم برافروختند.۱۴

< 2 Mbiri 16 >