< 2 Mbiri 16 >

1 Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.
In year thirty and six of [the] reign of Asa he came up Baasha [the] king of Israel on Judah and he built Ramah to not [surely] permitting one going out or one coming in to Asa [the] king of Judah.
2 Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko.
And he brought out Asa silver and gold from [the] treasuries of [the] house of Yahweh and [the] house of the king and he sent [it] to Ben Hadad [the] king of Aram who dwelt in Damascus saying.
3 Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”
A covenant [be] between me and between you and between father my and between father your here! I have sent to you silver and gold go break covenant your with Baasha [the] king of Israel so he may go up from on me.
4 Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali.
And he listened Ben Hadad to the king Asa and he sent [the] commanders of the armies which [belonged] to him against [the] cities of Israel and they struck down Ijon and Dan and Abel Maim and all [the] stores of [the] cities of Naphtali.
5 Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo.
And it was when heard Baasha and he ceased from building Ramah and he caused to cease work his.
6 Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.
And Asa the king he took all Judah and they carried off [the] stones of Ramah and wood its which he had built Baasha and he built with them Geba and Mizpah.
7 Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu.
And at the time that he came Hanani the seer to Asa [the] king of Judah and he said to him because depending you on [the] king of Aram and not you depended on Yahweh God your there-fore it has escaped [the] army of [the] king of Aram from hand your.
8 Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu.
¿ Not the Cushites and the Libyans were they an army - for multitude chariotry and horsemen to abundance exceedingly and because depending you on Yahweh he gave them in hand your.
9 Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”
For Yahweh eyes his [are] roving about in all the earth to show himself strong with [those who] heart their [is] complete to him you have acted foolishly on this for from now there with you [will be] wars.
10 Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.
And he was angry Asa against the seer and he put him [the] house of the stock[s] for in a rage with him on this and he crushed Asa some of the people at the time that.
11 Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
And there! [the] matters of Asa former and latter there they [are] written on [the] scroll of the kings of Judah and Israel.
12 Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga.
And he became sick Asa in year thirty and nine of reign his in feet his [was] to upwards sickness his and also in sickness his not he sought Yahweh for the physicians.
13 Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake.
And he lay down Asa with ancestors his and he died in year forty and one of reigning his.
14 Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.
And people buried him in own grave his which he had dug for himself in [the] city of David and they made lie him in the lying place which he had filled spices and kinds mixed as ointment of work and they burned for him a burning great up to muchness.

< 2 Mbiri 16 >