< 2 Mbiri 16 >

1 Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.
In the thirty-sixth year of the rule of Asa, Baasha, king of Israel, went up against Judah, building Ramah so that no one was able to go out or in to Asa, king of Judah.
2 Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko.
Then Asa took silver and gold out of the stores of the Lord's house and of the king's store-house, and sent to Ben-hadad, king of Aram, at Damascus, saying,
3 Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”
Let there be an agreement between me and you as there was between my father and your father: see, I have sent you silver and gold; go and put an end to your agreement with Baasha, king of Israel, so that he may give up attacking me.
4 Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali.
And Ben-hadad did as King Asa said, and sent the captains of his armies against the towns of Israel, attacking Ijon and Dan and Abel-maim, and all the store-towns of Naphtali.
5 Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo.
Then Baasha, hearing of it, put a stop to the building of Ramah, and let his work come to an end.
6 Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.
Then King Asa, with all Judah, took away the stones and wood with which Baasha was building Ramah, and he made use of them for building Geba and Mizpah.
7 Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu.
At that time Hanani the seer came to Asa, king of Judah, and said to him, Because you have put your faith in the king of Aram and not in the Lord your God, the army of the king of Aram has got away out of your hands.
8 Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu.
Were not the Ethiopians and the Lubim a very great army, with war-carriages and horsemen more than might be numbered? but because your faith was in the Lord, he gave them up into your hands.
9 Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”
For the eyes of the Lord go this way and that, through all the earth, letting it be seen that he is the strong support of those whose hearts are true to him. In this you have done foolishly, for from now you will have wars.
10 Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.
Then Asa was angry with the seer, and put him in prison, burning with wrath against him because of this thing. And at the same time Asa was cruel to some of the people.
11 Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Now the acts of Asa, first and last, are recorded in the book of the kings of Judah and Israel.
12 Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga.
In the thirty-ninth year of his rule, Asa had a very bad disease of the feet; but he did not go to the Lord for help in his disease, but to medical men.
13 Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake.
So Asa went to rest with his fathers, and death came to him in the forty-first year of his rule.
14 Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.
And they put him into the resting-place which he had made for himself in the town of David, in a bed full of sweet perfumes of all sorts of spices, made by the perfumer's art, and they made a great burning for him.

< 2 Mbiri 16 >