< 2 Mbiri 15 >

1 Mzimu wa Mulungu unabwera pa Azariya mwana wa Odedi.
و روح خدا به عزریا ابن عودید نازل شد.۱
2 Iye anapita kukakumana ndi Asa ndipo anati kwa iye, “Tandimverani, inu Asa ndi Ayuda onse ndi Benjamini. Yehova ali ndi inu, inunso mukakhala naye. Ngati inu mumufunafuna Iye mudzamupeza, koma ngati mumusiya, Iye adzakusiyani.
و او برای ملاقات آسا بیرون آمده، وی را گفت: «ای آسا و تمامی یهودا وبنیامین از من بشنوید! خداوند با شما خواهد بودهر گاه شما با او باشید و اگر او را بطلبید او راخواهید یافت، اما اگر او را ترک کنید او شما راترک خواهد نمود.۲
3 Kwa nthawi yayitali Israeli anali wopanda Mulungu weniweni, wopanda wansembe wophunzitsa ndi wopanda malamulo.
و اسرائیل مدت مدیدی بی‌خدای حق و بی‌کاهن معلم و بی‌شریعت بودند.۳
4 Koma pamene anali pa mavuto anatembenukira kwa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi kufunafuna Iye, ndipo anamupeza.
اما چون در تنگیهای خود به سوی یهوه خدای اسرائیل بازگشت نموده، او را طلبیدند او رایافتند.۴
5 Masiku amenewo sikunali kwabwino kuyenda ulendo, pakuti anthu onse okhala mʼdziko anali pa mavuto aakulu.
و در آن زمان به جهت هر‌که خروج ودخول می‌کرد هیچ امنیت نبود بلکه اضطراب سخت بر جمیع سکنه کشورها می‌بود.۵
6 Mtundu umodzi umakanthidwa ndi mtundu wina ndipo mzinda wina umakanthidwa ndi mzinda wina, pakuti Mulungu amawasautsa ndi mazunzo a mtundu uliwonse.
و قومی از قومی و شهری از شهری هلاک می‌شدند، چونکه خدا آنها را به هر قسم بلا مضطرب می‌ساخت.۶
7 Koma inu, khalani amphamvu ndipo musataye mtima, pakuti mudzalandira mphotho ya ntchito yanu.”
اما شما قوی باشید و دستهای شماسست نشود زیرا که اجرت اعمال خود راخواهید یافت.»۷
8 Asa atamva mawu awa ndiponso uneneri wa Azariya mwana wa Odedi, analimba mtima. Iye anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi mʼmizinda yonse imene analanda a ku mapiri a Efereimu. Iye anakonzetsa guwa lansembe la Yehova limene linali kutsogolo kwa khonde la Nyumba ya Mulungu.
پس چون آسا این سخنان و نبوت (پسر)عودید نبی را شنید، خویشتن را تقویت نموده، رجاسات را از تمامی زمین یهودا و بنیامین و ازشهرهایی که در کوهستان افرایم گرفته بود دورکرد، و مذبح خداوند را که پیش روی رواق خداوند بود تعمیر نمود.۸
9 Kenaka anasonkhanitsa anthu onse a ku Yuda ndi Benjamini ndiponso anthu ochokera ku Efereimu, Manase ndi Simeoni amene ankakhala pakati pawo, pakuti gulu lalikulu linabwera kwa iye kuchokera ku Israeli litaona kuti anali ndi Yehova Mulungu wake.
و تمامی یهودا وبنیامین و غریبان را که از افرایم و منسی و شمعون در میان ایشان ساکن بودند جمع کرد زیرا گروه عظیمی از اسرائیل چون دیدند که یهوه خدای ایشان با او می‌بود به او پیوستند.۹
10 Iwo anasonkhana mu Yerusalemu mwezi wachitatu wa chaka cha 15 cha ulamuliro wa Asa.
پس در ماه سوم از سال پانزدهم سلطنت آسا در اورشلیم جمع شدند.۱۰
11 Pa nthawi imeneyi anapereka nsembe kwa Yehova, ngʼombe 700 ndiponso nkhosa ndi mbuzi 7,000 zochokera pa zolanda ku nkhondo zimene anabweretsa.
و در آن روز هفتصد گاو و هفت هزار گوسفند از غنیمتی که آورده بودند برای خداوند ذبح نمودند.۱۱
12 Iwo anachita pangano loti azifunafuna Yehova, Mulungu wa makolo awo, ndi mtima ndi moyo wawo wonse.
و به تمامی دل و تمامی جان خود عهد بستند که یهوه خدای پدران خودرا طلب نمایند.۱۲
13 Aliyense wosafunafuna Yehova Mulungu wa Israeli aziphedwa, kaya ndi wamngʼono kapena wamkulu, mwamuna kapena mkazi.
و هر کسی‌که یهوه خدای اسرائیل را طلب ننماید، خواه کوچک و خواه بزرگ، خواه مرد و خواه زن، کشته شود.۱۳
14 Iwo analumbira kwa Yehova, mokweza mawu, akuyimba malipenga ndi mbetete.
و به صدای بلند و آواز شادمانی و کرناها و بوقها برای خداوند قسم خوردند.۱۴
15 Anthu onse a ku Yuda anakondwera pa kulumbirako chifukwa analumbira ndi mtima wawo wonse. Iwo anafunafuna Mulungu mwachidwi, ndipo anamupeza Iye. Kotero Yehova anawapatsa mpumulo mbali zonse.
و تمامی یهودا به‌سبب این قسم شادمان شدند زیرا که به تمامی دل خودقسم خورده بودند، و چونکه او را به رضامندی تمام طلبیدند وی را یافتند و خداوند ایشان را ازهر طرف امنیت داد.۱۵
16 Mfumu Asa anachotsanso Maaka agogo ake pa udindo wa amayi a mfumu chifukwa anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo, naliswa ndipo kenaka anakaliwotcha ku chigwa cha Kidroni.
و نیز آسا پادشاه مادر خود معکه را از ملکه بودن معزول کرد زیرا که او تمثالی به جهت اشیره ساخته بود و آسا تمثال او را قطع نمود و آن راخرد کرده، در وادی قدرون سوزانید.۱۶
17 Ngakhale kuti sanachotse malo opembedzerako mafano mu Israeli, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova, masiku onse a moyo wake.
امامکانهای بلند از میان اسرائیل برداشته نشد. لیکن دل آسا در تمامی ایامش کامل می‌بود.۱۷
18 Iye anabweretsanso mʼNyumba ya Mulungu zipangizo zasiliva, golide ndi ziwiya zina zimene iyeyo ndi abambo ake anazipatula.
وچیزهایی را که پدرش وقف کرده، و آنچه را که خودش وقف نموده بود از نقره و طلا و ظروف به خانه خداوند درآورده۱۸
19 Panalibenso nkhondo mpaka chaka cha 35 cha ufumu wa Asa.
و تا سال سی و پنجم سلطنت آسا جنگ نبود.۱۹

< 2 Mbiri 15 >