< 2 Mbiri 15 >

1 Mzimu wa Mulungu unabwera pa Azariya mwana wa Odedi.
Or Azarias, fils d’Oded, l’esprit de Dieu étant venu en lui,
2 Iye anapita kukakumana ndi Asa ndipo anati kwa iye, “Tandimverani, inu Asa ndi Ayuda onse ndi Benjamini. Yehova ali ndi inu, inunso mukakhala naye. Ngati inu mumufunafuna Iye mudzamupeza, koma ngati mumusiya, Iye adzakusiyani.
Sortit à la rencontre d’Asa, et lui dit: Ecoutez-moi, Asa, et vous, Juda et Benjamin. Le Seigneur a été avec vous, parce que vous avez été avec lui. Si vous le cherchez, vous le trouverez, mais si vous l’abandonnez, il vous abandonnera.
3 Kwa nthawi yayitali Israeli anali wopanda Mulungu weniweni, wopanda wansembe wophunzitsa ndi wopanda malamulo.
Il se passera un grand nombre de jours en Israël, sans vrai Dieu, sans prêtre enseignant et sans loi.
4 Koma pamene anali pa mavuto anatembenukira kwa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi kufunafuna Iye, ndipo anamupeza.
Et lorsque dans leur angoisse ils reviendront au Seigneur Dieu d’Israël, et qu’ils le chercheront, ils le trouveront.
5 Masiku amenewo sikunali kwabwino kuyenda ulendo, pakuti anthu onse okhala mʼdziko anali pa mavuto aakulu.
En ce temps-là, il n’y aura point de paix pour l’entrant et le sortant, mais des terreurs de toutes parts sur tous les habitants de la terre;
6 Mtundu umodzi umakanthidwa ndi mtundu wina ndipo mzinda wina umakanthidwa ndi mzinda wina, pakuti Mulungu amawasautsa ndi mazunzo a mtundu uliwonse.
Car une nation combattra contre une nation, et une ville contre une ville, parce que le Seigneur les troublera de toutes sortes d’angoisses.
7 Koma inu, khalani amphamvu ndipo musataye mtima, pakuti mudzalandira mphotho ya ntchito yanu.”
Vous donc, fortifiez-vous, et que vos mains ne s’affaiblissent point; car il y aura une récompense pour votre œuvre.
8 Asa atamva mawu awa ndiponso uneneri wa Azariya mwana wa Odedi, analimba mtima. Iye anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi mʼmizinda yonse imene analanda a ku mapiri a Efereimu. Iye anakonzetsa guwa lansembe la Yehova limene linali kutsogolo kwa khonde la Nyumba ya Mulungu.
Lorsqu’Asa eut entendu cela, c’est-à-dire les paroles et la prophétie d’Azarias, fils d’Oded, le prophète, il se fortifia, et enleva les idoles de toute la terre de Juda et de Benjamin, et des villes qu’il avait prises, du mont Ephraïm, et il dédia l’autel du Seigneur qui était devant le portique du Seigneur.
9 Kenaka anasonkhanitsa anthu onse a ku Yuda ndi Benjamini ndiponso anthu ochokera ku Efereimu, Manase ndi Simeoni amene ankakhala pakati pawo, pakuti gulu lalikulu linabwera kwa iye kuchokera ku Israeli litaona kuti anali ndi Yehova Mulungu wake.
Et il assembla tout Juda et Benjamin, et avec eux les étrangers venus d’Ephraïm, de Manassé, et de Siméon; car plusieurs s’étaient réfugiés d’Israël vers lui, voyant que le Seigneur son Dieu était avec lui.
10 Iwo anasonkhana mu Yerusalemu mwezi wachitatu wa chaka cha 15 cha ulamuliro wa Asa.
Et lorsqu’ils furent venus à Jérusalem le troisième mois, l’an quinzième du règne d’Asa,
11 Pa nthawi imeneyi anapereka nsembe kwa Yehova, ngʼombe 700 ndiponso nkhosa ndi mbuzi 7,000 zochokera pa zolanda ku nkhondo zimene anabweretsa.
Ils immolèrent au Seigneur en ce jour-là, parmi les dépouilles et le butin qu’ils avaient emmené, sept cents bœufs et sept mille béliers.
12 Iwo anachita pangano loti azifunafuna Yehova, Mulungu wa makolo awo, ndi mtima ndi moyo wawo wonse.
Et le roi entra selon la coutume pour confirmer l’alliance, afin qu’ils cherchassent le Seigneur Dieu de leurs pères de tout leur cœur et de toute leur âme.
13 Aliyense wosafunafuna Yehova Mulungu wa Israeli aziphedwa, kaya ndi wamngʼono kapena wamkulu, mwamuna kapena mkazi.
Or, si quelqu’un, dit-il, ne cherche pas le Seigneur Dieu d’Israël, qu’il meure, depuis le plus petit jusqu’au plus grand, depuis l’homme jusqu’à la femme.
14 Iwo analumbira kwa Yehova, mokweza mawu, akuyimba malipenga ndi mbetete.
Et ils le jurèrent au Seigneur avec une voix forte au milieu des cris de joie, au bruit de la trompette et au son des clairons,
15 Anthu onse a ku Yuda anakondwera pa kulumbirako chifukwa analumbira ndi mtima wawo wonse. Iwo anafunafuna Mulungu mwachidwi, ndipo anamupeza Iye. Kotero Yehova anawapatsa mpumulo mbali zonse.
Tous ceux qui étaient dans la Judée, avec exécration; car c’est en tout leur cœur qu’ils jurèrent, et avec leur entière volonté qu’ils cherchèrent le Seigneur; et ils le trouvèrent, et le Seigneur leur donna le repos à l’entour.
16 Mfumu Asa anachotsanso Maaka agogo ake pa udindo wa amayi a mfumu chifukwa anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo, naliswa ndipo kenaka anakaliwotcha ku chigwa cha Kidroni.
Asa déposa Maacha, mère du roi, de l’autorité souveraine, parce qu’elle avait élevé dans un bois sacré un simulacre de Priape, qu’il brisa entièrement; et l’ayant mis en pièces, il le brûla dans le torrent de Cédron.
17 Ngakhale kuti sanachotse malo opembedzerako mafano mu Israeli, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova, masiku onse a moyo wake.
Mais les hauts lieux restèrent en Israël; cependant le cœur d’Asa fut parfait durant tous ses jours.
18 Iye anabweretsanso mʼNyumba ya Mulungu zipangizo zasiliva, golide ndi ziwiya zina zimene iyeyo ndi abambo ake anazipatula.
Et les choses que son père avait vouées ainsi que lui-même, il les porta dans la maison du Seigneur: de l’argent, de l’or et différentes espèces de vases.
19 Panalibenso nkhondo mpaka chaka cha 35 cha ufumu wa Asa.
Or il n’y eut point de guerre jusqu’à la trente-cinquième année du règne d’Asa.

< 2 Mbiri 15 >