< 2 Mbiri 15 >

1 Mzimu wa Mulungu unabwera pa Azariya mwana wa Odedi.
Og Asaria, Odeds Søn — over ham kom Guds Aand.
2 Iye anapita kukakumana ndi Asa ndipo anati kwa iye, “Tandimverani, inu Asa ndi Ayuda onse ndi Benjamini. Yehova ali ndi inu, inunso mukakhala naye. Ngati inu mumufunafuna Iye mudzamupeza, koma ngati mumusiya, Iye adzakusiyani.
Og han gik ud imod Asa og sagde til ham: Hører mig, Asa og al Juda og Benjamin! Herren er med eder, fordi I ere med ham, og dersom I søge ham, skal han lade sig finde af eder, men om I forlade ham, skal han forlade eder.
3 Kwa nthawi yayitali Israeli anali wopanda Mulungu weniweni, wopanda wansembe wophunzitsa ndi wopanda malamulo.
Og der var mange Dage for Israel, da de vare uden sand Gud og uden Præst, som underviste dem, og uden Lov.
4 Koma pamene anali pa mavuto anatembenukira kwa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi kufunafuna Iye, ndipo anamupeza.
Og de omvendte sig i deres Nød til Herren, Israels Gud, og søgte ham, og han lod sig finde af dem.
5 Masiku amenewo sikunali kwabwino kuyenda ulendo, pakuti anthu onse okhala mʼdziko anali pa mavuto aakulu.
Men i hine Tider havde ingen Fred, naar han gik ud, og naar han gik ind; thi et stort Bulder gik over alle Indbyggerne i Landene,
6 Mtundu umodzi umakanthidwa ndi mtundu wina ndipo mzinda wina umakanthidwa ndi mzinda wina, pakuti Mulungu amawasautsa ndi mazunzo a mtundu uliwonse.
og de bleve sønderknuste, Folk imod Folk, og Stad imod Stad; thi Gud forfærdede dem med alle Haande Angest.
7 Koma inu, khalani amphamvu ndipo musataye mtima, pakuti mudzalandira mphotho ya ntchito yanu.”
Men I, værer frimodige og lader ikke eders Hænder synke; thi der er Løn for eders Gerning.
8 Asa atamva mawu awa ndiponso uneneri wa Azariya mwana wa Odedi, analimba mtima. Iye anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi mʼmizinda yonse imene analanda a ku mapiri a Efereimu. Iye anakonzetsa guwa lansembe la Yehova limene linali kutsogolo kwa khonde la Nyumba ya Mulungu.
Der Asa hørte disse Ord og Profeten Odeds Profeti, blev han frimodig og borttog Vederstyggelighederne fra det ganske Judas og Benjamins Land og fra de Stæder, som han havde indtaget af Efraims Bjerg, og fornyede Herrens Alter, som var foran Herrens Forhal.
9 Kenaka anasonkhanitsa anthu onse a ku Yuda ndi Benjamini ndiponso anthu ochokera ku Efereimu, Manase ndi Simeoni amene ankakhala pakati pawo, pakuti gulu lalikulu linabwera kwa iye kuchokera ku Israeli litaona kuti anali ndi Yehova Mulungu wake.
Og han samlede al Juda og Benjamin og de fremmede hos dem af Efraim og af Manasse og af Simeon; thi mangfoldige af Israel gik over til ham, der de saa, at Herren hans Gud var med ham.
10 Iwo anasonkhana mu Yerusalemu mwezi wachitatu wa chaka cha 15 cha ulamuliro wa Asa.
Og de samlede sig til Jerusalem, i den tredje Maaned i Asas Regerings femtende Aar.
11 Pa nthawi imeneyi anapereka nsembe kwa Yehova, ngʼombe 700 ndiponso nkhosa ndi mbuzi 7,000 zochokera pa zolanda ku nkhondo zimene anabweretsa.
Og de ofrede til Herren samme Dag af det Bytte, som de havde ført hjem, syv Hundrede Øksne og syv Tusinde Faar.
12 Iwo anachita pangano loti azifunafuna Yehova, Mulungu wa makolo awo, ndi mtima ndi moyo wawo wonse.
Og de indgik Pagten om at søge Herren, deres Fædres Gud, af deres ganske Hjerte og af deres ganske Sjæl.
13 Aliyense wosafunafuna Yehova Mulungu wa Israeli aziphedwa, kaya ndi wamngʼono kapena wamkulu, mwamuna kapena mkazi.
Og hver, som ikke vilde søge Herren, Israels Gud, skulde dødes, baade liden og stor, baade Mand og Kvinde.
14 Iwo analumbira kwa Yehova, mokweza mawu, akuyimba malipenga ndi mbetete.
Og de tilsvore Herren med høj Røst og med Frydeskrig og med Basuner og med Trompeter.
15 Anthu onse a ku Yuda anakondwera pa kulumbirako chifukwa analumbira ndi mtima wawo wonse. Iwo anafunafuna Mulungu mwachidwi, ndipo anamupeza Iye. Kotero Yehova anawapatsa mpumulo mbali zonse.
Og al Juda var glad over Eden; thi de havde svoret af deres ganske Hjerte og søgte ham med deres ganske Villie, og han lod sig finde af dem; og Herren skaffede dem Rolighed trindt omkring.
16 Mfumu Asa anachotsanso Maaka agogo ake pa udindo wa amayi a mfumu chifukwa anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo, naliswa ndipo kenaka anakaliwotcha ku chigwa cha Kidroni.
Og Kong Asa afsatte ogsaa sin Moder Maaka, at hun ikke skulde være Dronning, fordi hun havde gjort sig et grueligt Billede af Astarte, og Asa udryddede hendes gruelige Billede og stødte det smaat og opbrændte det ved Kedrons Bæk.
17 Ngakhale kuti sanachotse malo opembedzerako mafano mu Israeli, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova, masiku onse a moyo wake.
Men Højene toges ikke bort af Israel, dog var Asas Hjerte retskaffent alle hans Dage.
18 Iye anabweretsanso mʼNyumba ya Mulungu zipangizo zasiliva, golide ndi ziwiya zina zimene iyeyo ndi abambo ake anazipatula.
Og han førte de Ting, som hans Fader havde helliget, og det, som han selv havde helliget, ind i Guds Hus, Sølv og Guld og Kar.
19 Panalibenso nkhondo mpaka chaka cha 35 cha ufumu wa Asa.
Og der var ingen Krig indtil det fem og tredivte Aar af Asas Regering.

< 2 Mbiri 15 >