< 2 Mbiri 14 >

1 Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.
Forsothe Abia slepte with hise fadris, and thei birieden hym in the citee of Dauid; and Asa, his sone, regnede for hym. In whos daies the lond restide ten yeer.
2 Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
And Asa dide that, that was good and plesaunt in the siyt of his God, and he destriede the auteris of straunge worschipyng, and `he destriede hiy places,
3 Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera.
and brak ymagis, and kittide doun woodis;
4 Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake.
and he comaundide Juda to seke the Lord God of her fadris, and to do the lawe and alle comaundementis.
5 Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake.
And he took awei fro alle the citees of Juda auteris and templis of idols, and he regnede in pees.
6 Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.
And he bildide stronge cytees in Juda; for he was in reste, and no batels risiden in his tymes, for the Lord yaf pees.
7 Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.
Forsothe he seide to Juda, Bilde we these cytees, and cumpasse we with wallis, and strengthe we with touris and yatis and lockis, as longe as alle thingis ben restful fro batel; for we han souyte the Lord God of oure fadris, and he hath youe to vs pees bi cumpas. Therfor thei bildiden, and no lettyng was in bildyng.
8 Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.
Sotheli Asa hadde in his oost thre hundrid thousynde of men of Juda berynge scheldis and speris, sotheli of Beniamyn he hadde two hundrid thousynde and fourscoore thousynde of scheeld beeris and of archeris; alle these weren ful stronge men.
9 Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa.
Forsothe Zara of Ethiop yede out ayens hem with his oost ten `sithis an hundrid thousynde, and with thre hundrid charis, and cam `til to Masera.
10 Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.
Certis Aza yede ayens hem, and araiede scheltrun to batel in the valei Sephata, which is bisidis Masera. And he inwardli clepide the Lord God,
11 Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”
and seide, Lord, no dyuersitee is anentis thee, whether thou helpe in fewe, ethir in manye; oure Lord God, helpe thou vs, for we han trist in thee and in thi name, and camen ayens this multitude; Lord, thou art oure God, a man haue not the maistrye ayens thee.
12 Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa,
Therfor the Lord made aferd Ethiopens bifor Asa and Juda, and Ethiopens fledden; and Asa and his puple,
13 ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo.
that was with hym, pursuede hem `til to Gerare. And Ethiopens felden doun `til to deeth, for thei weren al to-brokun bi the Lord sleynge, and bi his oost fiytynge. Therfor thei token many spuylis,
14 Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko.
and smitiden alle the citees `bi the cumpas of Gerare; for greet drede hadde assailid alle men. And thei rifliden cytees, and baren a weye myche prey;
15 Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.
but also thei destrieden the fooldis of scheep, and token multitude without noumbre of scheep and of camels, and turneden ayen in to Jerusalem.

< 2 Mbiri 14 >