< 2 Mbiri 13 >

1 Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda,
En el año dieciocho del rey Jeroboam, Abías se convirtió en rey de Judá.
2 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya. Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
Fue rey en Jerusalén durante tres años; El nombre de su madre era Maaca, la hija de Uriel de Guibea. Y hubo guerra entre Abías y Jeroboam.
3 Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.
Y Abías salió a pelear con un ejército de hombres de guerra, cuatrocientos mil de sus mejores hombres; y Jeroboam alineó sus fuerzas contra él, ochocientos mil de sus mejores hombres de guerra.
4 Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani!
Y Abías tomó posición en el monte Zemaraim, en la región montañosa de Efraín, y dijo: Escúchenme, Jeroboam y todo Israel:
5 Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere?
¿No te queda claro que el Señor, el Dios de Israel, le dio el gobierno de Israel a David y sus hijos para siempre, por un acuerdo hecho con sal?
6 Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake.
Más Jeroboam, hijo de Nabat, siervo de Salomón, hijo de David, tomó las armas contra su señor.
7 Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.
Y ciertos hombres insensatos y perversos se unieron a él y se impusieron contra Roboam, el hijo de Salomón, pues era joven y débil de carácter, y no podía retenerlos.
8 “Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu.
Ahora es su propósito ponerse en contra de la autoridad que el Señor ha puesto en manos de los hijos de David, y ustedes, son una gran multitud y tienen con ustedes los bueyes de oro que hizo Jeroboam para ser sus dioses.
9 Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.
Y después de expulsar a los sacerdotes del Señor, los hijos de Aarón y los levitas, ¿no han hecho sacerdotes de entre ustedes mismos como lo hacen los pueblos de otras tierras? para que cualquiera que venga a hacerse sacerdote ofreciendo un buey o siete ovejas, pueda ser un sacerdote de aquellos que no son dioses.
10 “Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi.
Pero en cuanto a nosotros, el Señor es nuestro Dios, y no nos hemos apartado de él; tenemos sacerdotes que hacen la obra del Señor, incluso los hijos de Aarón y los levitas en sus lugares;
11 Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya.
Por quienes las ofrendas quemadas y los inciensos son enviados en humo delante del Señor cada mañana y cada tarde; y pusieron el pan sagrado sobre su mesa y los candelabros de oro con sus luces encendidas cada noche; porque guardamos las órdenes que nos dio el Señor nuestro Dios, pero ustedes se han alejado de él.
12 Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”
Y ahora Dios está con nosotros a la cabeza, y sus sacerdotes con sus fuertes cuernos sonando contra ti. Oh hijos de Israel, no hagan guerra contra el Señor, el Dios de sus antepasados, porque no les irá bien.
13 Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo.
Pero Jeroboam había puesto a algunos de sus hombres para que los atacaran por la espalda, por lo que algunos se enfrentaban a Judá y otros estaban apostados en secreto a sus espaldas.
14 Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo
Y Judá, volviendo sus rostros, vio que estaban siendo atacados por delante y por detrás; y clamaron al Señor para pedir ayuda, mientras los sacerdotes hacían sonar sus cuernos.
15 ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
Y los hombres de Judá dieron un fuerte clamor; y ante su clamor, Dios derrotó a Jeroboam y a todo Israel delante de Abías y de Judá.
16 Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo.
Y huyeron los hijos de Israel delante de Judá, y Dios los entregó en sus manos.
17 Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa.
Y Abías y su pueblo los mataron con gran destrucción; quinientos mil de los mejores de Israel fueron puestos a filo de espada.
18 Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Entonces en ese tiempo los hijos de Israel fueron humillados, y los hijos de Judá prevalecieron, porque confiaron en el Señor, el Dios de sus padres.
19 Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
Y Abías fue tras Jeroboam y tomó algunas de sus ciudades, Bethel con sus pueblos pequeños y Jesana con sus pueblos pequeños y Efron con sus pueblos pequeños.
20 Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.
Y Jeroboam no volvió a recuperar su poder en la vida de Abías; y el SEÑOR envió muerte sobre él.
21 Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.
Pero Abías se engrandeció, y tuvo catorce esposas, y fue padre de veintidós hijos y dieciséis hijas.
22 Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.
Y el resto de los hechos de Abías, y sus caminos y sus dichos, están registrados en el relato del profeta Iddo.

< 2 Mbiri 13 >