< 2 Mbiri 13 >

1 Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda,
I KA makahiki umi kumamawalu o ke alii o Ieroboama, noho alii iho la o Abiia maluna o ka Iuda.
2 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya. Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
Ekolu makahiki kona noho alii ana ma Ierusalema; a o ka inoa o kona makuwahine o Mikaia ke kaikamahine a Uriela no Gibea. A he kaua no iwaena o Abiia a me Ieroboama.
3 Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.
A hoonohonoho iho la o Abiia i ke kaua me ka poe koa, ka poe ikaika i ke kaua, eha haneri tausani kanaka i waeia: a o Ieroboama hoi, hoonohonoho oia i ke kaua me na kanaka i waeia ewalu haneri tausani, he poe koa ikaika.
4 Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani!
Alaila, ku iluna o Abiia maluna o ka puu o Zemaraima, aia no ia ma ka mauna o Eperaima, a olelo aku la, E hoolohe mai, e Ieroboama a me ka Iseraela a pau;
5 Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere?
Aole anei oukou i ike, ua haawi mai la o Iehova ke Akua o ka Iseraela i ke aupuni maluna o ka Iseraela, ia Davida, i mea mau loa ia ia, a me kana poe mamo, me ka berita paakai?
6 Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake.
Aka, ua ku iluna o Ieroboama ke keiki a Nebata, ke kauwa a Solomona ke keiki a Davida, a kipi iho la i kona haku.
7 Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.
A ua hoakoakoaia io na la na kanaka lapuwale, ka poe hewa, a ua hooikaika ku e mai ia Rehoboama, i ke keiki a Solomona. A he keiki o Rehoboama ia wa, a palupalu kona naau, aole i hiki ia ia ke ku e ia lakou.
8 “Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu.
Ano, ke manao nei oukou e hooikaika ku e mai i ke aupuni o Iehova aia ma ka lima o na keiki a Davida; o oukou ka poe koa nui loa, a me oukou pu na bipi keiki gula a Ieroboama i hana'i, i mau akua no oukou.
9 Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.
Aole anei oukou i kipaku i na kahuna a Iehova i ka poe mamo a Aarona, a me na Levi, a hoonoho iho la no oukou iho i na kahuna e like me na lahuikanaka o na aina e? a o kela mea keia mea e hiki mai me ka bipi keiki, a me na hipakane ehiku ma kona lima i mea haawi aku, ua lilo ia i kahuna no na akua lapuwale.
10 “Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi.
Aka, o makou nei, o Iehova, oia ko makou Akua, aole makou i haalele ia ia; a o na kahuna, ka poe kauwa na Iehova, o ka poe mamo lakou a Aarona, a o na Levi, e hana ana lakou i ka lakou oihana iho.
11 Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya.
Kukuni lakou i kela kakahiaka i keia kakahiaka, i kela ahiahi i keia ahiahi, i na mohaikuni na Iehova, a me na mea poni ala; a hoonoho lakou maluna o ka papaaina maemae i ka berena hoike, a me ka ipukukui gula e aa ana kona mau manamana i kela ahiahi keia ahiahi; no ka mea, e maluna ana makou i ka oihana na Iehova, ko makou Akua, aka, o oukou la, ua haalele ia ia.
12 Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”
Eia hoi me makou ke Akua i luna no makou, a o kona mau kahuna no hoi me na mea kani e hoopuiwa ia oukou. E na mamo a Iseraela, mai kaua aku oukou ia Iehova i ke Akua o ko oukou poe kupuna; no ka mea, aole pono iki oukou pela.
13 Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo.
A hoonoho o Ieroboama i poe moemoe e hoohalua mahope o lakou, nolaila, imua o ka Iuda kekahi poe, a ma ko lakou kua no hoi ka poe hoohalua.
14 Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo
A ike ka Iuda, aia no ke kaua mamua o lakou a mahope kekahi, kahea aku lakou ia Iehova, a hookani ka poe kahuna i na pu.
15 ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
Alaila, hooho ae la ka poe kanaka o Iuda; a i ka hooho ana o ka Iuda poe kanaka, i luku mai la o Iehova ia Ieroboama a me ka Iseraela a pau imua o Abiia, a me ka Iuda.
16 Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo.
A auhee aku la ka poe mamo a Iseraela imua o ka Iuda, a haawi mai ke Akua i ua poe la iloko o ko lakou lima.
17 Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa.
A luku aku la o Abiia a me kona poe kanaka ia lakou me ka luku nui; a o ka poe o ka Iseraela i pepehiia a haule iho la, elima haneri tausani kanaka i waeia.
18 Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Pela i pio ai ka poe mamo a Iseraela ia manawa, a lanakila iho la ka Iuda, no ka mea, ua hilinai aku lakou ia Iehova i ke Akua o ko lakou poe kupuna.
19 Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
Alualu aku la o Abiia mahope o Ieroboama, a lawe pio oia i na kulanakauhale mai ona aku la, ia Betela, a me na kauhale e pili ana ilaila ia Iesana a me na kauhale e pili ana ilaila; ia Eperaima no hoi a me na kauhale e pili ana ilaila.
20 Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.
Aole i loaa hou ia Ieroboama kona ikaika i na la o Abiia; a hahau mai la o Iehova ia ia, a make iho la.
21 Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.
Lanakila iho la o Abiia, a lawe ae la nana i na wahine he umi a me kumamaha, a hanau mai la na keikikane he iwakalua a me kumamalua, a me na kaikamahine he umi a me kumamaono.
22 Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.
A o ke koena o na hana a Abiia a me kona mau aoao, a me kana olelo, ua kakauia ma na kaao a Ido, ke kaula.

< 2 Mbiri 13 >