< 2 Mbiri 13 >
1 Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda,
La dix-huitième année du Roi Jéroboam Abija commença à régner sur Juda.
2 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya. Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
Et il régna trois ans à Jérusalem. Sa mère avait nom Micaja, et elle était fille d'Uriël de Guibba. Or il y eut guerre entre Abija et Jéroboam.
3 Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.
Et Abija commença la bataille avec une armée composée de gens vaillants pour la guerre; ils étaient quatre cent mille hommes d'élite. Or Jéroboam avait rangé contre lui la bataille avec huit cent mille hommes d'élite, forts et vaillants.
4 Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani!
Et Abija se tint debout sur la montagne de Tsémarajim, qui est dans les montagnes d'Ephraïm, et dit: Jéroboam et tout Israël écoutez-moi.
5 Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere?
N'est-ce pas à vous de savoir que l'Eternel le Dieu d'Israël a donné le Royaume à David sur Israël pour toujours, à lui, [dis-je], et à ses fils, par une alliance inviolable?
6 Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake.
Mais Jéroboam fils de Nébat, serviteur de Salomon fils de David, s'est élevé, et s'est rebellé contre son Seigneur.
7 Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.
Et des hommes de néant, imitateurs [de la malice] du Démon se sont assemblés vers lui, ils se sont fortifiés contre Roboam, fils de Salomon, parce que Roboam était un enfant, [et] de peu de courage, et qu'il ne tint pas ferme devant eux.
8 “Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu.
Et maintenant vous présumez de tenir ferme contre le Royaume de l'Eternel qui est entre les mains des fils de David, parce que vous êtes une grande multitude de peuple, et que les veaux d'or, que Jéroboam vous a faits pour être vos dieux, sont avec vous.
9 Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.
N'avez-vous pas rejeté les Sacrificateurs de l'Eternel, les fils d'Aaron et les Lévites? et ne vous êtes-vous pas fait des sacrificateurs à la façon des peuples des [autres] pays? Tous ceux qui sont venus avec un jeune veau, et avec sept béliers pour être consacrés, et pour être sacrificateurs de ce qui n'est pas Dieu?
10 “Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi.
Mais quant à nous, l'Eternel est notre Dieu, et nous ne l'avons point abandonné; et les Sacrificateurs qui font le service à l'Eternel, sont enfants d'Aaron, et les Lévites [sont employés] à leurs fonctions.
11 Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya.
Et on fait fumer les holocaustes chaque matin et chaque soir à l'Eternel, et le parfum des choses aromatiques. Les pains de proposition sont arrangés sur la table pure, et on allume le chandelier d'or avec ses lampes, chaque soir; car nous gardons ce que l'Eternel notre Dieu veut qui soit gardé; mais vous l'avez abandonné.
12 Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”
C'est pourquoi, voici, Dieu est avec nous pour être notre Chef, et ses Sacrificateurs, et les trompettes de retentissement bruyant pour les faire sonner contre vous. Enfants d'Israël, ne combattez point contre l'Eternel le Dieu de vos pères; car cela ne vous réussira point.
13 Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo.
Mais Jéroboam fit prendre un détour à une embuscade, afin qu'elle se jetât sur eux par derrière; de sorte que les [Israélites] se présentèrent en front à Juda, et l'embuscade était par derrière.
14 Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo
Et ceux de Juda regardèrent, et voici, ils avaient la bataille en front et par derrière, et ils s'écrièrent à l'Eternel, et les Sacrificateurs sonnaient des trompettes.
15 ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
Chacun de Juda jetait aussi des cris de joie, et il arriva, comme ils jetaient des cris de joie, que Dieu frappa Jéroboam et tout Israël, devant Abija et Juda.
16 Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo.
Et les enfants d'Israël s'enfuirent de devant Juda, parce que Dieu les avait livrés entre leurs mains.
17 Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa.
Abija donc et son peuple en firent un fort grand carnage, de sorte qu'il tomba d'Israël cinq cent mille hommes d'élite, blessés à mort.
18 Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Ainsi les enfants d'Israël furent humiliés en ce temps-là, et les enfants de Juda furent renforcés, parce qu'ils s'étaient appuyés sur l'Eternel le Dieu de leurs pères.
19 Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
Et Abija poursuivit Jéroboam, et prit sur lui ces villes; Béthel, et les villes de son ressort; Jésana, et les villes de son ressort; Héphrajim, et les villes de son ressort.
20 Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.
Et Jéroboam n'eut plus de force durant le temps d'Abija; mais l'Eternel le frappa, et il mourut.
21 Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.
Ainsi Abija se fortifia, et prit quatorze femmes, et il en eut vingt et deux fils, et seize filles.
22 Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.
Le reste des faits d'Abija, ses actions, et ses paroles sont écrites dans les Mémoires de Hiddo le Prophète.