< 2 Mbiri 12 >

1 Rehobowamu atakhazikika monga mfumu nakhaladi wamphamvu, iyeyo pamodzi ndi Aisraeli onse anasiya malamulo a Yehova.
Og det skete, der Roboams Rige var befæstet, og der han var bleven mægtig, da forlod han og hele Israel med ham Herrens Lov.
2 Chifukwa anakhala osakhulupirika pamaso pa Yehova, Sisaki mfumu ya dziko la Igupto inathira nkhondo Yerusalemu mʼchaka chachisanu cha mfumu Rehobowamu.
Og det skete i Kong Roboams femte Aar, da drog Sisak, Kongen af Ægypten, op imod Jerusalem (thi de havde forsyndet sig imod Herren)
3 Sisakiyo anabwera ndi magaleta 1,200 ndi anthu okwera akavalo 60,000 ndiponso asilikali osawerengeka ochokera ku Libiya, Suki ndi Kusi amene anabwera naye kuchokera ku Igupto.
med tusinde og to Hundrede Vogne og med tresindstyve Tusinde Ryttere, og der var ikke Tal paa det Folk, som kom med ham af Ægypten: Libyer, Sukiter og Morianer.
4 Iye analanda mizinda yotetezedwa ya Yuda ndipo anafika mpaka ku Yerusalemu.
Og han indtog de faste Stæder, som hørte til Juda, og kom til Jerusalem.
5 Ndipo mneneri Semaya anabwera kwa Rehobowamu ndi kwa atsogoleri a Yuda amene anasonkhana mu Yerusalemu chifukwa cha Sisaki ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova akuti, ‘Inu mwandisiya, choncho Inenso ndakusiyani ndi kukuperekani kwa Sisaki.’”
Da kom Semaja, Profeten, til Roboam og til de Øverste i Juda, som havde samlet sig til Jerusalem for Sisaks Skyld, og sagde til dem: Saa sagde Herren: I have forladt mig, og jeg har derfor overladt eder i Sisaks Haand.
6 Atsogoleri a Israeli pamodzi ndi mfumu anadzichepetsa nati, “Yehova ndi wolungama.”
Da ydmygede de Øverste udi Israel sig tillige med Kongen, og de sagde: Herren er retfærdig.
7 Yehova ataona kuti adzichepetsa, anayankhula ndi Semaya kuti, “Pakuti adzichepetsa, Ine sindiwawononga koma posachedwapa ndiwapulumutsa. Sinditsanulira ukali wanga pa Yerusalemu kudzera mwa Sisaki.
Og der Herren saa, at de ydmygede sig, da skete Herrens Ord til Semaja og sagde: De have ydmyget sig, jeg vil ikke ødelægge dem; men om en kort Tid vil jeg lade dem undkomme, og min Fortørnelse skal ikke udøses over Jerusalem ved Sisak.
8 Komabe iwo adzakhala pansi pa ulamuliro wake, kuti aphunzire kudziwa kusiyanitsa pakati pa kutumikira Ine ndi kutumikira mafumu a mayiko ena.”
Dog skulle de vorde hans Tjenere, at de kunne fornemme, hvad det er at tjene mig og at tjene Landenes Riger.
9 Sisaki mfumu ya dziko la Igupto atathira nkhondo Yerusalemu, iye anatenga chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu. Iye anatenga zinthu zonse kuphatikizapo zishango zagolide zimene Solomoni anapanga.
Saa drog Sisak, Kongen af Ægypten, op imod Jerusalem, og han tog Liggendefæet i Herrens Hus og Liggendefæet i Kongens Hus, han tog alting bort; og han tog de Skjolde af Guld, som Salomo havde ladet gøre.
10 Ndipo mfumu inapereka zishango zamkuwa kwa oyangʼanira mʼmalo mwake ndipo iwo anazipereka kwa oyangʼanira alonda amene amayangʼanira pa chipata cha nyumba yaufumu.
Og Kong Roboam lod gøre Kobberskjolde i deres Sted og betroede dem i de øverste Drabanters Haand, som toge Vare paa Døren for Kongens Hus.
11 Nthawi ina iliyonse imene mfumu ikupita ku Nyumba ya Yehova, alonda amapita nayo atanyamula zishango, ndipo kenaka amakazibwezera ku chipinda cha alonda.
Og det skete, saa tidt Kongen gik ind i Herrens Hus, da kom Drabanterne og bare dem ud, og de bare dem tilbage i Drabanternes Kammer.
12 Pakuti mfumu Rehobowamu inadzichepetsa, mkwiyo wa Yehova unamuchokera, sanawonongedweretu. Kunena zoona, munali zinthu zina zabwino mu Yuda.
Og da han ydmygede sig, blev Herrens Vrede vendt af fra ham, thi han vilde ikke ødelægge ham aldeles; thi der var ogsaa nogle gode Ting i Juda.
13 Mfumu Rehobowamu anayika maziko a ufumu wake mwamphamvu mu Yerusalemu ndipo anapitirira kukhala mfumu. Iye anali ndi zaka 41 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka 17 mu Yerusalemu, mzinda wa Yehova umene anasankha pakati pa mafuko a Aisraeli mmene Yehova anakhazikikamo. Dzina la amayi ake linali Naama, amene anali Mwamoni.
Og Kong Roboam befæstede sig i Jerusalem og regerede; thi Roboam var et og fyrretyve Aar gammel, der han blev Konge, og regerede sytten Aar i Jerusalem, i den Stad, som Herren af alle Israels Stammer havde udvalgt for der at sætte sit Navn; og hans Moders Navn var Naema, den ammonitiske.
14 Rehobowamu anachita zoyipa chifuwa mtima wake sunafunefune Yehova.
Og han gjorde det, som var ondt; thi han beredte ikke sit Hjerte til at søge Herren.
15 Ntchito za Rehobowamu, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri la mneneri Semaya ndi mlosi Ido amene amalemba mbiri? Panali nkhondo yosatha pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
Men Roboams Handeler, de første og de sidste, ere de ikke skrevne i Profeten Semajas Krønikers Bog og hos Seeren Iddo, hvor han opregner Slægtregistrene? og der var Krige imellem Roboam og Jeroboam alle Dage.
16 Rehobowamu anamwalira, ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Ndipo mwana wake Abiya analowa ufumu mʼmalo wake.
Og Roboam laa med sine Fædre, og blev begraven i Davids Stad; og Abia, hans Søn, blev Konge i hans Sted.

< 2 Mbiri 12 >