< 2 Mbiri 12 >

1 Rehobowamu atakhazikika monga mfumu nakhaladi wamphamvu, iyeyo pamodzi ndi Aisraeli onse anasiya malamulo a Yehova.
I stalo se, když utvrdil království Roboám a zmocnil je, opustil zákon Hospodinův, i všecken Izrael s ním.
2 Chifukwa anakhala osakhulupirika pamaso pa Yehova, Sisaki mfumu ya dziko la Igupto inathira nkhondo Yerusalemu mʼchaka chachisanu cha mfumu Rehobowamu.
Stalo se, pravím, léta pátého království Roboámova, že vytáhl Sesák král Egyptský proti Jeruzalému, (nebo byli zhřešili proti Hospodinu),
3 Sisakiyo anabwera ndi magaleta 1,200 ndi anthu okwera akavalo 60,000 ndiponso asilikali osawerengeka ochokera ku Libiya, Suki ndi Kusi amene anabwera naye kuchokera ku Igupto.
S tisícem a dvěma sty vozů, a s šedesáti tisíci jízdných, a nebylo počtu lidu, kterýž přitáhl s ním z Egypta, Lubimských, Sukkimských a Chussimských.
4 Iye analanda mizinda yotetezedwa ya Yuda ndipo anafika mpaka ku Yerusalemu.
A pobral města hrazená, kteráž byla v Judstvu, a přitáhl až k Jeruzalému.
5 Ndipo mneneri Semaya anabwera kwa Rehobowamu ndi kwa atsogoleri a Yuda amene anasonkhana mu Yerusalemu chifukwa cha Sisaki ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova akuti, ‘Inu mwandisiya, choncho Inenso ndakusiyani ndi kukuperekani kwa Sisaki.’”
Tedy Semaiáš prorok přišel k Roboámovi a k knížatům Judským, kteříž se byli sebrali do Jeruzaléma, bojíce se Sesáka, a řekl jim: Toto praví Hospodin: Vy jste mne opustili, i já také opouštím vás v rukou Sesákových.
6 Atsogoleri a Israeli pamodzi ndi mfumu anadzichepetsa nati, “Yehova ndi wolungama.”
I ponížili se knížata Izraelská i král, a řekli: Spravedlivýť jest Hospodin.
7 Yehova ataona kuti adzichepetsa, anayankhula ndi Semaya kuti, “Pakuti adzichepetsa, Ine sindiwawononga koma posachedwapa ndiwapulumutsa. Sinditsanulira ukali wanga pa Yerusalemu kudzera mwa Sisaki.
A když viděl Hospodin, že se ponížili, stalo se slovo Hospodinovo k Semaiášovi, řkoucí: Ponížiliť jsou se, neshladím jich, ale dám jim tudíž vysvobození, aniž se vyleje prchlivost má na Jeruzalém skrze Sesáka.
8 Komabe iwo adzakhala pansi pa ulamuliro wake, kuti aphunzire kudziwa kusiyanitsa pakati pa kutumikira Ine ndi kutumikira mafumu a mayiko ena.”
A však sloužiti jemu budou, aby zkusili, co jest to mně sloužiti, a sloužiti králům zemským.
9 Sisaki mfumu ya dziko la Igupto atathira nkhondo Yerusalemu, iye anatenga chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu. Iye anatenga zinthu zonse kuphatikizapo zishango zagolide zimene Solomoni anapanga.
A tak vstoupiv Sesák král Egytský do Jeruzaléma, pobral poklady domu Hospodinova, i poklady domu královského, všecko to pobral. Vzal i pavézy zlaté, kterýchž byl nadělal Šalomoun.
10 Ndipo mfumu inapereka zishango zamkuwa kwa oyangʼanira mʼmalo mwake ndipo iwo anazipereka kwa oyangʼanira alonda amene amayangʼanira pa chipata cha nyumba yaufumu.
I nadělal král Roboám místo nich pavéz měděných, a poručil je úředníkům nad drabanty, kteříž ostříhali brány domu královského.
11 Nthawi ina iliyonse imene mfumu ikupita ku Nyumba ya Yehova, alonda amapita nayo atanyamula zishango, ndipo kenaka amakazibwezera ku chipinda cha alonda.
A když král chodíval do domu Hospodinova, přicházívali drabanti a nosili je; potom též zase přinášeli je do pokoje drabantů.
12 Pakuti mfumu Rehobowamu inadzichepetsa, mkwiyo wa Yehova unamuchokera, sanawonongedweretu. Kunena zoona, munali zinthu zina zabwino mu Yuda.
Když se pak ponížil, odvrátila se od něho prchlivost Hospodinova, a neshladil ho do cela, tak jakož se k Judovi v dobrých věcech ohlašoval.
13 Mfumu Rehobowamu anayika maziko a ufumu wake mwamphamvu mu Yerusalemu ndipo anapitirira kukhala mfumu. Iye anali ndi zaka 41 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka 17 mu Yerusalemu, mzinda wa Yehova umene anasankha pakati pa mafuko a Aisraeli mmene Yehova anakhazikikamo. Dzina la amayi ake linali Naama, amene anali Mwamoni.
Tedy zmocnil se král Roboám v Jeruzalémě a kraloval; nebo ve čtyřidcíti a v jednom létě byl Roboám, když počal kralovati, a sedmnácte let kraloval v Jeruzalémě, městě, kteréž vyvolil Hospodin ze všech pokolení Izraelských, aby tam přebývalo jméno jeho. Jméno matky jeho bylo Naama Ammonitská.
14 Rehobowamu anachita zoyipa chifuwa mtima wake sunafunefune Yehova.
Kterýž činil zlé věci; nebo neustavil srdce svého, aby hledal Hospodina.
15 Ntchito za Rehobowamu, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri la mneneri Semaya ndi mlosi Ido amene amalemba mbiri? Panali nkhondo yosatha pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
Věci pak Roboámovy, první i poslední, zdaž zapsány nejsou v knihách Semaiáše proroka, a Iddo proroka, kdež se vyčítá pořádek rodů, ano i války mezi Roboámem a Jeroboámem, po všecky dny?
16 Rehobowamu anamwalira, ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Ndipo mwana wake Abiya analowa ufumu mʼmalo wake.
I usnul Roboám s otci svými, a pochován jest v městě Davidově, a kraloval Abiáš syn jeho místo něho.

< 2 Mbiri 12 >