< 2 Mbiri 11 >
1 Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
Y vino Roboam a Jerusalén y reunió a los hombres de Judá y Benjamín, ciento ochenta mil de sus mejores combatientes, para hacer la guerra contra Israel y recuperar el reino para Roboam.
2 Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
Pero la palabra del Señor vino a Semaías, el hombre de Dios, diciendo:
3 “Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
Di a Roboam, hijo de Salomón, rey de Judá, y a todo Israel en Judá y Benjamín.
4 ‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
El Señor ha dicho: No debes ir a la guerra contra tus hermanos; que cada uno regrese a su casa, porque esto es mi propósito. Así que escucharon las palabras del Señor y no lucharon contra Jeroboam.
5 Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
Ahora se guardó Roboam en Jerusalén, construyendo ciudades amuralladas en Judá.
6 Betelehemu, Etamu, Tekowa,
Fue el constructor de Belén y Etam y Tecoa.
7 Beti Zuri, Soko, Adulamu,
Y Bet-sur, Soco, Adulam.
9 Adoraimu, Lakisi, Azeka,
Y Adoraim, Laquis, Azeca,
10 Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
Y Zora, Ajalón, Hebrón, ciudades amuralladas de Judá y Benjamín.
11 Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
E hizo fuertes las ciudades amuralladas, y puso capitanes en ellas y almacenes de comida, aceite y vino.
12 Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
Y en cada ciudad puso provisiones de escudos y lanzas, y las hizo muy fuertes. Y Judá y Benjamín los mantuvo a su lado.
13 Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
Y los sacerdotes y levitas que estaban en todo Israel se reunieron con él desde todas partes de su país.
14 Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
Porque los levitas abandonaron sus lugares de vida y sus bienes, y vinieron a Judá y Jerusalén; porque Jeroboam y sus hijos los habían enviado lejos, no dejando que fueran sacerdotes para el Señor;
15 Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
Y él mismo hizo sacerdotes para los lugares altos, y para las imágenes de las cabras y los bueyes que había hecho.
16 Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Y después de ellos, de todas las tribus de Israel, todos aquellos cuyos corazones estaban fijos y fieles al Señor, el Dios de Israel, llegaron a Jerusalén para hacer ofrendas al Señor, el Dios de sus antepasados.
17 Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
Continuaron aumentando el poder del reino de Judá, e hicieron a Roboam, hijo de Salomón, fuerte por tres años. y por tres años anduvieron en los caminos de David y Salomón.
18 Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
Y tomó Roboam como a su mujer Mahalat, hija de Jerimot, hijo de David y de Abihail, hija de Eliab, hijo de Isaí;
19 Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
Y tuvo hijos junto a él, Jehus, Semarias y Zaham.
20 Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
Y después de ella tomó a Maaca, hija de Absalón; y tuvo a Abiam, Atai, Ziza y Selomit.
21 Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
Maaca, la hija de Absalón, era más querida por Roboam que todas sus esposas y sus concubinas; porque tenía dieciocho esposas y sesenta concubinas, y era padre de veintiocho hijos y sesenta hijas.
22 Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
Y Roboam hizo a Abías, hijo de Maaca, jefe y gobernante entre sus hermanos, porque su propósito era hacerlo rey.
23 Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.
Y en su sabiduría tenía a sus hijos estacionados en cada pueblo amurallado por todas las tierras de Judá y Benjamín; y les dio una gran cantidad de comida, y tomó esposas para ellos.