< 2 Mbiri 11 >
1 Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
Idi nakasangpet ni Rehoboam idiay Jerusalem, inummongna ti balay ni Juda ken Benjamin, 180, 000 a napili a lallaki a soldado, a makigubat iti Israel, tapno maisubli manen ti pagarian kenni Rehoboam.
2 Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
Ngem immay ti sao ni Yahweh kenni Semaias, a tao ti Dios, a kunana,
3 “Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
“Agsaoka kenni Rehoboam, a putot a lalaki ni Solomon, nga ari ti Juda, ken kadagiti amin a tattao ti Israel idiay Juda ken Benjamin; a kunam,
4 ‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
'Kastoy ti kuna ni Yahweh: Rumbeng a saanyo a rauten wenno gubaten dagiti kakabsatyo. Rumbeng nga agsubli ti tunggal lalaki iti balayna, ta pagayatak ti napasamak.”' Impangagda ngarud dagiti sasao ni Yahweh ket imbabawida ti panangrautda kenni Jeroboam.
5 Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
Nagnaed ni Rehoboam idiay Jerusalem ket nangibangon kadagiti siudad idiay Juda a pangsalaknib.
6 Betelehemu, Etamu, Tekowa,
Binangonna ti Betlehem, Etam, Tekoa,
7 Beti Zuri, Soko, Adulamu,
Bet-zur, Soco, Adullam,
9 Adoraimu, Lakisi, Azeka,
Adoraim, Lakis, Azeka,
10 Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
Zora, Aijalon ken Hebron. Dagitoy dagiti nasarikedkedan a siudad idiay Juda ken Benjamin.
11 Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
Pinalagdana dagiti sarikedked ket nangisaad isuna kadagiti mangidaulo kadagitoy, nga addaan kadagiti abasto a taraon, lana, ken arak.
12 Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
Nangikabil isuna kadagiti kalasag ken gayang iti tunggal siudad ken pinatibkerna dagiti siudad. Kukuana ti Juda ken Benjamin.
13 Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
Napan kenkuana dagiti padi ken Levita nga adda iti entero nga Israel manipud kadagiti beddengda.
14 Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
Ta pinanawan dagiti Levita dagiti pagpastoranda ken sanikuada tapno mapanda idiay Juda ken Jerusalem; ta pinagtalaw ida ni Jeroboam ken dagiti putotna a lallaki, tapno saandan a maaramid dagiti pagrebbenganda a kas padi ni Yahweh.
15 Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
Nangdutok ni Jeroboam kadagiti bukodna a padi nga agserbi kadagiti disso a pagdaydayawan ken kadagiti didiosen a sinan-urbon a baka ken sinan-kalding nga inaramidna.
16 Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Simmurot kadakuada dagiti tattao a nagtaud iti amin a tribu ti Israel, dagiti nangipapuso a mangsapul kenni Yahweh a Dios ti Israel; napanda idiay Jerusalem tapno mangidatagda kenni Yahweh a Dios dagiti kapuonanda.
17 Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
Isu a pinatibkerda ti pagarian ti Juda, ken pinabilegda ni Rehoboam a putot ni Solomon, bayat iti tallo a tawen—ta nagbiagda iti wagas da David ken Solomon iti tallo a tawen.
18 Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
Inasawa ni Rehoboam ni Mahalat nga anak a babai da Abigail ken Jerimot a putot a lalaki ni David, ni Abigail ti putot a babai ni Eliab, a putot a lalaki ni Jesse.
19 Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
Nangipasngay ni Mahalat iti annak a lallaki: Da Jeus, Semarias ken Zaham.
20 Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
Kalpasan ni Mahalat, inasawa ni Rehoboam ni Maaca a putot a babai ni Absalom; impasngayna da Abias, Attai, Ziza ken Selomit.
21 Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
Ad-adda nga inayat ni Rehoboam ni Maaca a putot a babai ni Absalom ngem kadagiti dadduma nga assawana ken kadagiti kamalalana (nangasawa isuna iti sangapulo ket walo ken innem a pulo ti kamalalana, ken duapulo ket walo ti putotna a lallaki ken innem a pulo a babbai).
22 Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
Dinutokan ni Rehoboam ni Abias nga anak ni Maaca a kas panguloen, a mangidaulo kadagiti kakabsatna; gandatna nga isuna ti isaadna nga ari.
23 Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.
Nagturay a sisisirib ni Rehoboam; inwarasna dagiti amin a putotna a lallaki iti entero a daga ti Juda ken Benjamin iti tunggal nasarikedkedan a siudad. Inikkanna pay ida iti nabuslon a taraon ken imbirokanna ida iti adu nga assawa.