< 2 Mbiri 11 >

1 Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
When Rehoboam arrived in Jerusalem, he gathered 180,000 of the best soldiers from the tribes of Judah and Benjamin. He wanted them to fight against [the northern tribes of] Israel [and defeat them], in order that he could rule [all the tribes of] the kingdom again.
2 Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
But Yahweh spoke to the prophet Shemaiah and said this to him:
3 “Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
“Go and tell this to [Solomon’s son] Rehoboam, the king of Judah, and to all the Israeli people of the tribes of Judah and Benjamin:
4 ‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
‘Yahweh says that you must not go to fight against [the people of Israel; they are] your distant relatives. All of you must go home. What has happened is what Yahweh wanted to happen.’” [So Shemaiah went and told that to them, ] and they all heeded what Yahweh had commanded them to do, and they did not attack Jeroboam [and his soldiers].
5 Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
Rehoboam lived in Jerusalem, and his workers built walls around several of the cities and towns in Judah to protect them [against enemy attacks].
6 Betelehemu, Etamu, Tekowa,
In [the area that belonged to] the tribes of Judah and Benjamin they built walls around Bethlehem, Etam, Tekoa,
7 Beti Zuri, Soko, Adulamu,
Beth-Zur, Soco, Adullam,
8 Gati, Maresa, Zifi,
Gath, Mareshah,
9 Adoraimu, Lakisi, Azeka,
Adoraim, Lachish, Azekah,
10 Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
Zorah, Aijalon, and Hebron.
11 Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
He also appointed an army commander in each of those cities and towns, and gave them supplies of food, olive oil, and wine [to keep in storage].
12 Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
He put shields and spears in all the cities and made them well-protected. So he continued to rule the tribes of Judah and Benjamin.
13 Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
The priests and other descendants of Levi throughout Israel supported Rehoboam.
14 Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
The descendants of Levi [who lived outside the territory of Judah and Benjamin] abandoned their property and their pastureland, and they came to Jerusalem and [to other places in] Judah, because Jeroboam and his sons would not allow them to do the work of priests of Yahweh.
15 Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
Instead, Jeroboam appointed the priests that he wanted to work [at the altars he commanded to be built] on the hilltops, [to offer sacrifices to] the idols that he commanded to be made [that resembled] goats and calves.
16 Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
And people from every tribe in Israel who wanted to worship Yahweh, the God to whom the Israelis belonged, went with the descendants of Levi to Jerusalem to live there and to offer sacrifices to Yahweh, the God whom their ancestors [worshiped].
17 Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
They caused the kingdom of Judah to be strong, and for three years they were happy that Solomon’s son Rehoboam was the king. During that time they conducted their lives [righteously] as David and Solomon had done previously.
18 Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
Rehoboam married Mahalath. She was the daughter of David’s son Jerimoth, and her mother was Abihail, the daughter of Eliab and granddaughter of Jesse.
19 Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
Rehoboam and Mahalath had three sons: Jeush, Shemariah, and Zaham.
20 Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
Later Rehoboam married Maacah, the daughter of Absalom, and they had four sons: Abijah, Attai, Ziza, and Shelomith.
21 Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
Rehoboam loved Maacah more than he loved any other of his wives and slave wives. Altogether he had 18 wives and 60 slave wives, and 28 sons and 60 daughters.
22 Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
Rehoboam appointed his son Abijah to be the leader of his [older and younger] brothers, because he wanted to appoint Abijah to be the next king.
23 Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.
He very wisely sent some of his other sons to other cities in the areas of the tribes of Judah and Benjamin, and to all the other cities that had walls around them. He gave them plenty of supplies and many wives.

< 2 Mbiri 11 >