< 2 Mbiri 1 >

1 Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.
USolomoni indodana kaDavida waseqina embusweni wakhe, leNkosi uNkulunkulu wakhe yayilaye, yamenza waba mkhulu kakhulu.
2 Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja.
USolomoni wasekhuluma kuIsrayeli wonke, kubaphathi bezinkulungwane labamakhulu, lakubahluleli, lakuzo zonke induna kuIsrayeli wonke, inhloko zaboyise.
3 Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja.
USolomoni lebandla lonke laye basebesiya endaweni ephakemeyo eyayiseGibeyoni; ngoba kwakukhona lapho ithente lenhlangano kaNkulunkulu uMozisi inceku yeNkosi alenzayo enkangala.
4 Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu.
Kodwa uDavida wayewenyusile umtshokotsho kaNkulunkulu uvela eKiriyathi-Jeyarimi, wawusa lapho uDavida ayewulungisele khona, ngoba wayewumisele ithente eJerusalema.
5 Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko.
Lelathi lethusi, uBhezaleli indodana kaUri indodana kaHuri ayelenzile, walibeka phambi kwethabhanekele leNkosi; uSolomoni lebandla badinga-ke kulo.
6 Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.
USolomoni wasesenyukela lapho elathini lethusi phambi kweNkosi elalisethenteni lenhlangano, wanikela phezu kwalo iminikelo yokutshiswa eyinkulungwane.
7 Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
Ngalobobusuku uNkulunkulu wabonakala kuSolomoni, wathi kuye: Cela engingakupha khona.
8 Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake.
USolomoni wasesithi kuNkulunkulu: Wena wenzele uDavida ubaba umusa omkhulu, wangenza ngaba yinkosi esikhundleni sakhe.
9 Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi.
Khathesi, Nkosi Nkulunkulu, kaliqiniswe ilizwi lakho kuDavida ubaba, ngoba wena ungenze ngaba yinkosi phezu kwabantu abanengi ngangothuli lomhlabathi.
10 Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
Khathesi ngipha inhlakanipho lolwazi ukuze ngiphume ngingene phambi kwalababantu; ngoba ngubani ongehlulela lababantu bakho abakhulu kangaka?
11 Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo,
UNkulunkulu wasesithi kuSolomoni: Ngenxa yokuthi lokhu bekusenhliziyweni yakho, njalo ungacelanga inotho, ingcebo, lodumo, lempilo yezitha zakho, futhi ungacelanga insuku ezinengi, kodwa uzicelele inhlakanipho lolwazi ukuze wahlulele abantu bami engikwenze waba yinkosi phezu kwabo:
12 Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”
Inhlakanipho lolwazi ukuphiwe; ngizakunika futhi inotho lengcebo lodumo, angazange abe lakho okunjalo amakhosi ayengaphambi kwakho, langemva kwakho kakuyikuba khona okunjalo.
13 Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.
Wasebuya uSolomoni evela endaweni ephakemeyo eseGibeyoni waya eJerusalema, evela phambi kwethente lenhlangano; wasebusa phezu kukaIsrayeli.
14 Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu.
USolomoni wasebuthanisa izinqola labagadi bamabhiza; wayelezinqola ezingamakhulu alitshumi lane, labagadi bamabhiza abazinkulungwane ezilitshumi lambili; wasekubeka emizini yezinqola, njalo kanye lenkosi eJerusalema.
15 Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
Inkosi yasisenza isiliva legolide eJerusalema kwaba njengamatshe, njalo wenza imisedari yaba njengemikhiwa yesikhamore esesihotsheni, ngobunengi.
16 Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe.
Wasengenisa ngokuthenga amabhiza avela eGibhithe, ayengekaSolomoni, lelembu elicolekileyo; labathengi benkosi babelithatha ilembu elicolekileyo ngentengo.
17 Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.
Basebesenyusa bekhupha inqola eGibhithe ngamashekeli esiliva angamakhulu ayisithupha, lebhiza ngamashekeli alikhulu lamatshumi amahlanu. Ngokunjalo bakukhuphela wonke amakhosi amaHethi lamakhosi eSiriya ngesandla sabo.

< 2 Mbiri 1 >