< 2 Mbiri 1 >

1 Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.
Salomon, fils de David, fut donc affermi dans la royauté, et le Seigneur son Dieu était avec lui; et le Seigneur l’éleva très haut.
2 Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja.
Et Salomon donna des ordres à tout Israël, aux tribuns, aux centurions, aux autres chefs, aux magistrats et aux princes des familles;
3 Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja.
Et il s’en alla avec toute la multitude au haut lieu de Gabaon, où était le tabernacle de l’alliance de Dieu, que fit Moïse, serviteur de Dieu, dans le désert.
4 Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu.
Quant à l’arche de Dieu, David l’avait amenée de Cariathiarim au lieu qu’il lui avait préparé, et où il lui avait dressé un tabernacle, c’est-à-dire à Jérusalem.
5 Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko.
Mais l’autel d’airain qu’avait fait Béséléel fils d’Uri, fils de Hur, était resté là devant le tabernacle du Seigneur; et Salomon alla le chercher, lui et toute l’assemblée.
6 Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.
Et Salomon monta sur l’autel d’airain devant le tabernacle de l’alliance du Seigneur, et il y offrit mille hosties.
7 Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
Or voilà qu’en cette nuit même Dieu lui apparut, disant: Demande ce que tu veux que je te donne.
8 Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Alors Salomon dit à Dieu: C’est vous qui avez fait une grande miséricorde à David, mon père, et qui m’avez établi roi à sa place.
9 Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi.
Maintenant donc, Seigneur Dieu, qu’elle s’accomplisse, la promesse que vous avez faite à David, mon père: car c’est vous qui m’avez établi roi sur votre peuple, qui est aussi innombrable que la poussière de la terre.
10 Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
Donnez-moi de la sagesse et de l’intelligence, enfin que j’entre et sorte devant votre peuple; car qui peut juger dignement ce peuple qui est vôtre, et qui est si grand?
11 Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo,
Alors Dieu répondit à Salomon: Parce que cela a plu de préférence à ton cœur, et que tu ne m’as point demandé des richesses, ni des biens, ni de la gloire, ni les âmes de ceux qui te haïssent, ni des jours de vie très nombreux; mais que tu as demandé de la sagesse et de la science, afin que tu puisses juger mon peuple sur lequel je t’ai établi roi:
12 Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”
La sagesse et la science te sont données; et quant à des richesses, à des biens, à de la gloire, je t’en donnerai de telle sorte, que nul parmi les rois, ni avant toi, ni après toi, n’aura été semblable à toi.
13 Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.
Salomon vint donc du haut lieu de Gabaon à Jérusalem, devant le tabernacle d’alliance, et il régna sur Israël.
14 Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu.
Et il rassembla des chars et des cavaliers; on lui disposa mille quatre cents chariots et douze mille cavaliers, et il les fit mettre dans les villes des quadriges, et près du roi à Jérusalem.
15 Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
Et le roi rendit l’or et l’argent communs comme les pierres dans Jérusalem, et les cèdres comme les sycomores qui croissent dans les plaines en grande quantité.
16 Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe.
Mais les chevaux lui étaient amenés d’Égypte et de Coa par les marchands du roi, qui y allaient et les achetaient,
17 Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.
Un attelage de quatre chevaux, six cents sicles d’argent, et un cheval, cent cinquante; et c’est ainsi que dans tous les royaumes des Héthéens, et par tous les rois de Syrie, la vente se pratiquait.

< 2 Mbiri 1 >