< 1 Timoteyo 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.
Od Pavla, apostola Isusa Hrista, po zapovijesti Boga spasa našega i Gospoda Isusa Hrista, nada našega,
2 Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro. Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.
Timotiju, pravome sinu u vjeri, blagodat, milost, mir od Boga oca našega i Hrista Isusa Gospoda našega.
3 Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga,
Kao što te molih da ostaneš u Efesu, kad iðah u Maæedoniju, da zapovjediš nekima da ne uèe drukèije,
4 kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro.
Niti da gledaju na laži i na teftere od plemena kojima nema kraja, i koji prije èine prepiranja negoli Božij napredak u vjeri.
5 Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona.
A namjera je zapovijesti ljubav od èista srca i dobre savjesti i vjere nelicemjerne;
6 Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo.
U kojima neki pogriješivši svrnuše u prazne govore,
7 Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.
I htjeli bi da budu zakonici, a ne razumiju ni šta govore, ni šta utvrðuju.
8 Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino.
A znamo da je zakon dobar ako ga ko drži kao što treba.
9 Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena.
Znajuæi ovo da pravedniku zakon nije postavljen, nego bezakonicima i nepokornima i bezbožnicima i grješnicima, nepravednima i poganima, krvnicima oca i matere, krvnicima ljudskima,
10 Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona.
Kurvarima, muželožnicima, ljudokradicama, lažljivcima, kletvoprestupnicima, i ako što drugo ima protivno zdravoj nauci,
11 Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.
Po jevanðelju slave blaženoga Boga, koje je meni povjereno.
12 Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake.
I zahvaljujem Hristu Isusu Gospodu našemu koji mi daje moæ, što me za vjerna primi i postavi me u službu,
13 Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro.
Koji sam prije bio hulnik i gonitelj i siledžija; ali bih pomilovan, jer ne znajuæi uèinih u nevjerstvu.
14 Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.
Ali se još veæma umnoži blagodat Gospoda našega Isusa Hrista s vjerom i ljubavi u Hristu Isusu.
15 Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa.
Istinita je rijeè i svakoga primanja dostojna da Hristos Isus doðe na svijet da spase grješnike, od kojijeh sam prvi ja.
16 Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. (aiōnios g166)
Ali toga radi ja bih pomilovan da na meni prvome pokaže sve trpljenje Isus Hristos za ugled onima koji mu hoæe vjerovati za život vjeèni. (aiōnios g166)
17 Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
A caru vjeènome, neraspadljivome, koji se ne vidi, jedinome premudrome Bogu èast i slava vavijek vijeka. Amin. (aiōn g165)
18 Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo
Ovu pak zapovijest predajem ti, sine Timotije, po preðašnjijem proroštvima za tebe: da ratuješ u njima dobar rat,
19 utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka.
Imajuæi vjeru i dobru savjest, koju neki odbacivši otpadoše od vjere;
20 Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.
Meðu kojima su Imenej i Aleksandar koje predadoh sotoni da se nauèe ne huliti.

< 1 Timoteyo 1 >