< 1 Timoteyo 6 >

1 Onse amene ali mu ukapolo ayenera kuona ambuye awo ngati oyenera kuwachitira ulemu, kuti anthu anganyoze dzina la Mulungu ndi chiphunzitso chathu.
همۀ غلامان مسیحی باید با اربابان خود در کمال احترام رفتار کنند تا مردم نام خدا و تعلیم او را بد نگویند.
2 Amene ambuye awo ndi okhulupirira, asawapeputse chifukwa ambuye ndi abale mʼchikhulupiriro. Mʼmalo mwake akuyenera kuwatumikira bwino chifukwa ambuye wawo ndi okondedwa monga okhulupirira ndiponso ndi odzipereka kusamalira akapolo awo. Zinthu izi ukuyenera kuziphunzitsa ndi kuwalamula anthu.
اگر ارباب هم مسیحی باشد، نباید از او سوءاستفاده نمایند و از زیر کار شانه خالی کنند، بلکه برعکس باید بهتر کار کنند، چون به یک برادر مسیحی خدمت می‌کنند. این نکات را به ایمانداران تعلیم بده و ایشان را تشویق نما تا آنها را اجرا کنند.
3 Ngati wina aphunzitsa zosiyana ndi zimenezi, wosagwirizana ndi malangizo woona a Ambuye athu Yesu Khristu ndi chiphunzitso cholemekeza Mulungu,
اگر کسی تعلیم دیگری بدهد و با آموزشهای درست خداوند ما، عیسی مسیح، و با تعالیم دیندارانه موافق نباشد،
4 ameneyo ndi wodzitukumula ndipo sakudziwa chilichonse. Iyeyo ali ndi maganizo oyipa, wokonda kusemphana mawu ndi kutsutsana. Zimenezi zimabweretsa nsanje, mikangano, mʼnyozo, kuganizirana zoyipa,
چنین شخصی پر از تکبر شده و فاقد درک و فهم است، و علاقه‌ای ناسالم به مجادلات و نزاعها دربارۀ مفهوم کلمات دارد، چیزی که منجر می‌گردد به حسادت، مشاجرات، گفتگوهای بدخواهانه، بدگمانی‌های شرارت‌بار،
5 ndi kulimbana kosatha pakati pa anthu amitima yopotoka amene alandidwa choonadi ndipo amaganiza kuti kulemekeza Mulungu ndi njira yopezera chuma.
و اصطکاک‌های دائمی میان افرادی که ذهنی فاسد دارند، و به حقیقت پشت کرده‌اند، و گمان می‌برند که دینداری وسیله‌ای است برای کسب منافع مالی!
6 Koma kulemekeza Mulungu kuli ndi phindu lalikulu.
اما دینداری به‌همراه قانع بودن، ثروت عظیمی است.
7 Pakuti sitinabweretse kanthu mʼdziko lapansi, ndipo sitingatengenso kanthu pochoka mʼdziko lapansi.
ما چیزی با خود به این دنیا نیاورده‌ایم و چیزی نیز نخواهیم برد.
8 Koma ngati tili ndi chakudya ndi zovala, zimenezi zitikwanire.
پس اگر خوراک و پوشاک کافی داریم، باید قانع و راضی باشیم.
9 Anthu amene amafuna kulemera amagwa mʼmayesero ndi mu msampha ndi mʼzilakolako zambiri zopusa ndi zoopsa zimene zimagwetsera anthu mʼchitayiko ndi mʼchiwonongeko.
زیرا آنانی که به دنبال ثروت‌اندوزی می‌دوند، دیر یا زود دست به کارهای نادرست می‌زنند؛ این کارها به خود ایشان صدمه زده، فکرشان را فاسد می‌کند و آنها را به تباهی و نابودی می‌کشد.
10 Pakuti kukonda ndalama ndiye muzu wa zoyipa za mitundu yonse. Anthu ena ofunitsitsa ndalama, asochera ndipo asiya njira yachikhulupiriro ndipo adzitengera zowawitsa zambiri.
زیرا عشق به ثروت، ریشۀ انواع شرارت‌هاست. بعضی‌ها که در آرزوی ثروت بوده‌اند، از ایمان رویگردان شده، خود را گرفتار انواع دردها کرده‌اند.
11 Koma iwe, munthu wa Mulungu, thawa zinthu zonsezi. Tsatira chilungamo, moyo wolemekeza Mulungu, chikhulupiriro, chikondi, kupirira ndi kufatsa.
ای تیموتائوس، تو مرد خدایی! از این کارهای زشت بگریز، و راستی و تقوا را پیشهٔ خود ساز؛ به خدا اعتماد کن؛ انسان‌ها را محبت نما؛ صبور و مهربان باش.
12 Menya nkhondo yabwino yachikhulupiriro. Gwiritsitsa moyo wosatha umene anakuyitanira pamene unavomereza bwino lomwe pamaso pa mboni zambiri. (aiōnios g166)
در جنگ نیکوی ایمان به‌خوبی بجنگ و به دست آور آن زندگی جاوید را که خدا تو را به آن فراخواند، آن هنگام که در حضور گواهان بسیار، اعتراف نیکو کردی. (aiōnios g166)
13 Ndikukulamula pamaso pa Mulungu amene amapatsa moyo zinthu zonse, ndiponso pamaso pa Khristu Yesu amene pochitira umboni pamaso pa Pontiyo Pilato, ananena zoona zenizeni.
در حضور خدایی که به همه زندگی می‌بخشد، و در حضور مسیح عیسی که با دلیری در برابر پُنتیوس پیلاتُس شهادت داد، به تو سفارش می‌کنم
14 Usunge lamuloli mopanda banga ndi cholakwa kufikira Ambuye athu Yesu Khristu ataonekera.
که تمامی اوامر خدا را انجام دهی، تا کسی نتواند از حال تا بازگشت خداوند ما عیسی مسیح، عیبی در تو بیابد؛
15 Pa nthawi yake Mulungu adzamubweretsa kwa ife. Mulungu ndi wodalitsika ndipo Iye yekha ndiye Wolamulira, Mfumu ya mafumu, Mbuye wa ambuye.
زیرا خدای متبارک که تنها قادر متعال و شاه شاهان و سَرور سَروران است، در زمان معین مسیح را خواهد فرستاد.
16 Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni. (aiōnios g166)
تنها اوست که فناناپذیر است، و در نوری سکونت دارد که کسی را یارای نزدیک شدن به آن نیست، و هیچ بشری او را ندیده و نخواهد دید. عزت و قدرت تا به ابد بر او باد. آمین. (aiōnios g166)
17 Anthu onse amene ali ndi chuma uwalamule kuti asanyade kapena kuyika mitima yawo pa chuma chimene nʼchosadalirika. Koma chiyembekezo chawo chikhale mwa Mulungu amene amatipatsa mowolowamanja zonse zotisangalatsa. (aiōn g165)
به کسانی که در این دنیا ثروتی دارند بگو که مغرور نشوند و به آن امید نبندند چون دیر یا زود از بین خواهد رفت، بلکه امیدشان به خدا باشد که هر چه لازم داریم سخاوتمندانه برای ما فراهم می‌سازد تا از آنها لذّت ببریم. (aiōn g165)
18 Uwalamule kuti azichita zabwino, kuti azikhala olemera pa ntchito zabwino, owolowamanja ndi okonda kugawana zinthu zawo ndi anzawo.
به ایشان بگو دارایی خود را در راه خیر صرف کنند و در نیکوکاری ثروتمند باشند؛ با شادی به محتاجان کمک نمایند، و همیشه آماده باشند تا از ثروتی که خدا به ایشان عطا کرده است، به دیگران نفعی برسانند.
19 Potero adzadziwunjikira chuma chokhalitsa ngati maziko okhazikika a nthawi zakutsogolo, kuti akalandire moyo, umene ndi moyo weniweni.
با این کارهای نیک، ایشان گنجی واقعی برای خود ذخیره می‌کنند که بنیان خوبی برای آینده است، تا آن حیاتی را به دست آورند که زندگی واقعی است.
20 Timoteyo, samalitsa zimene unapatsidwa. Upewe nkhani zopanda pake zosalemekeza Mulungu ndiponso maganizo otsutsana amene amaganizidwa molakwika kuti ndi nzeru.
ای تیموتائوس، آنچه را که خدا به تو به امانت سپرده است، حفظ کن. خود را درگیر بحث‌های بیهوده نکن، به‌خصوص با کسانی که دم از علم و دانش می‌زنند.
21 Anthu ena chifukwa chovomereza nzeru zotere, asochera nʼkutaya chikhulupiriro chawo. Chisomo chikhale nawe.
بعضی از این دسته افراد، در اثر همین بحث‌ها، ایمانشان را از دست داده‌اند. فیض خداوند با تو باد.

< 1 Timoteyo 6 >