< 1 Timoteyo 6 >
1 Onse amene ali mu ukapolo ayenera kuona ambuye awo ngati oyenera kuwachitira ulemu, kuti anthu anganyoze dzina la Mulungu ndi chiphunzitso chathu.
E PONO i na kauwa a pau malalo iho o ka auamo, ke manao i ko lakou mau haku, he pono ke hoomaikai nui ia'ku, i ole ai e hoino wale ia ka inoa o ke Akua a me kana olelo.
2 Amene ambuye awo ndi okhulupirira, asawapeputse chifukwa ambuye ndi abale mʼchikhulupiriro. Mʼmalo mwake akuyenera kuwatumikira bwino chifukwa ambuye wawo ndi okondedwa monga okhulupirira ndiponso ndi odzipereka kusamalira akapolo awo. Zinthu izi ukuyenera kuziphunzitsa ndi kuwalamula anthu.
A o ka poe nona na haku manaoio, mai hoowahawaha aku lakou no ko lakou hoahanau ana; aka, e lawelawe aku no lakou, no ka mea, he poe paulele lakou a he poe alohaia e lawe pu ana i ka pono. Ma ia mau mea e ao aku ai oe me ka hooikaika aku.
3 Ngati wina aphunzitsa zosiyana ndi zimenezi, wosagwirizana ndi malangizo woona a Ambuye athu Yesu Khristu ndi chiphunzitso cholemekeza Mulungu,
A ina he okoa ka kekahi ao ana aku, me ka ae ole mai i na huaolelo pono, i na olelo a ko kakou Haku a Iesn Kristo, a me ke ao ana aku mamuli o ka manao maikai i ke Akua;
4 ameneyo ndi wodzitukumula ndipo sakudziwa chilichonse. Iyeyo ali ndi maganizo oyipa, wokonda kusemphana mawu ndi kutsutsana. Zimenezi zimabweretsa nsanje, mikangano, mʼnyozo, kuganizirana zoyipa,
He hookano ia, he naaupo loa, a e kuko wale ana i na ninau a me na huaolelo hooakamai, kahi e ulu ai ka huwa, ka paio, ka nuku, ka hoohuoi ino,
5 ndi kulimbana kosatha pakati pa anthu amitima yopotoka amene alandidwa choonadi ndipo amaganiza kuti kulemekeza Mulungu ndi njira yopezera chuma.
A me ka hoopaapaa huhu ana a na kanaka naau ino, me ka lako ole i ka olelo oiaio, e manao ana hoi, o ka waiwai ka manao i ke Akua; e hoookoa oe ia oe iho ia lakou.
6 Koma kulemekeza Mulungu kuli ndi phindu lalikulu.
Aka, o ka manao i ke Akua, me ka oluolu io, oia ka waiwai nui.
7 Pakuti sitinabweretse kanthu mʼdziko lapansi, ndipo sitingatengenso kanthu pochoka mʼdziko lapansi.
No ka mea, aohe a kakou mea i lawe mai ai iloko o keia ao, he oiaio hoi aohe a kakou mea e hiki ke lawe pu aku iwaho.
8 Koma ngati tili ndi chakudya ndi zovala, zimenezi zitikwanire.
A ina, ia kakou ka ai a me ke kapa, malaila kakou e oluolu ai.
9 Anthu amene amafuna kulemera amagwa mʼmayesero ndi mu msampha ndi mʼzilakolako zambiri zopusa ndi zoopsa zimene zimagwetsera anthu mʼchitayiko ndi mʼchiwonongeko.
Aka, o ka poe e makemake ana i ka waiwai nui, ua haule lakou iloko o ka hoowalewaleia a me ka pahele, a iloko o kela kuko lapuwale keia kuko lapuwale e pono ole ai, na mea e paholo ai na kanaka i ka poino, a me ka make.
10 Pakuti kukonda ndalama ndiye muzu wa zoyipa za mitundu yonse. Anthu ena ofunitsitsa ndalama, asochera ndipo asiya njira yachikhulupiriro ndipo adzitengera zowawitsa zambiri.
No ka mea, o ka puni kala o ka mole no ia o ka hewa a pau; ua kuko nui ia ia e kekahi poe, a ua haalele lakou i ka manaoio, a ua houhou lakou ia lakou iho i na ehaeha he nui.
11 Koma iwe, munthu wa Mulungu, thawa zinthu zonsezi. Tsatira chilungamo, moyo wolemekeza Mulungu, chikhulupiriro, chikondi, kupirira ndi kufatsa.
Aka, o oe, e ke kanaka o ke Akua, e haalele ia mau mea; a e hahai mamuli o ka pono, o ka manao i ke Akua, o ka manaoio, o ke aloha, o ke ahonui, a me ke akahai.
12 Menya nkhondo yabwino yachikhulupiriro. Gwiritsitsa moyo wosatha umene anakuyitanira pamene unavomereza bwino lomwe pamaso pa mboni zambiri. (aiōnios )
E paio aku i ka paio maikai o ka manaoio, e hoopaa aku i ke ola mau loa, i kou mea i kohoia mai ai, a e hooia aku ai i ka hooiaio maikai imua o ke alo o na hoike he lehulehu. (aiōnios )
13 Ndikukulamula pamaso pa Mulungu amene amapatsa moyo zinthu zonse, ndiponso pamaso pa Khristu Yesu amene pochitira umboni pamaso pa Pontiyo Pilato, ananena zoona zenizeni.
Ke kauoha aku nei au ia oe imua i ke alo o ke Akua, ka mea i hoola i na mea a pau, a o Kristo Iesu hoi, ka mea i hoike imua o Ponetio Pilato i ka hooiaio maikai;
14 Usunge lamuloli mopanda banga ndi cholakwa kufikira Ambuye athu Yesu Khristu ataonekera.
E malama oe i keia kauoha i kina ole, me ka hala ole, a hiki wale aku i ka ikea ana mai o ko kakou Haku o Iesu Kristo;
15 Pa nthawi yake Mulungu adzamubweretsa kwa ife. Mulungu ndi wodalitsika ndipo Iye yekha ndiye Wolamulira, Mfumu ya mafumu, Mbuye wa ambuye.
I ka mea i na manawa ona iho, o hoike mai ai oia, o ka Moi pomaikai hookahi, o ke Alii o na alii, o ka Haku o na haku;
16 Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni. (aiōnios )
Nona wale no ka make ole, e noho mau ana iloko o ka malamalama kahi e hiki ole aku ai ke kanaka; aole ikeia e ke kanaka, aole hoi e hiki ia ia ke nana aku; ia ia mau loa hoi ka mahalo a me ka mana. Amene. (aiōnios )
17 Anthu onse amene ali ndi chuma uwalamule kuti asanyade kapena kuyika mitima yawo pa chuma chimene nʼchosadalirika. Koma chiyembekezo chawo chikhale mwa Mulungu amene amatipatsa mowolowamanja zonse zotisangalatsa. (aiōn )
E kauoha aku oe i ka poe waiwai i keia ao, mai hookiekie ko lakou naau, mai hilinai i ka waiwai oiaio ole, aka, i ke Akua ola, nana na mea a pau i haawi lokomaikai mai ia kakou e oluolu ai. (aiōn )
18 Uwalamule kuti azichita zabwino, kuti azikhala olemera pa ntchito zabwino, owolowamanja ndi okonda kugawana zinthu zawo ndi anzawo.
E hana maikai hoi lakou, i lako hoi lakou i na hana maikai, i makaukau hoi i ka haawi wale aku me ka lokomaikai;
19 Potero adzadziwunjikira chuma chokhalitsa ngati maziko okhazikika a nthawi zakutsogolo, kuti akalandire moyo, umene ndi moyo weniweni.
E hoahu ana i kumu maikai na lakou iho, no ka manawa e hiki mai ana, i paa aku ai lakou i ke ola mau loa.
20 Timoteyo, samalitsa zimene unapatsidwa. Upewe nkhani zopanda pake zosalemekeza Mulungu ndiponso maganizo otsutsana amene amaganizidwa molakwika kuti ndi nzeru.
E Timoteo, e malama oe i ka mea i kauohaia'ku ia oe, e pale ana i ka wawa lapuwale, a me ke ku ee ana o ka mea i kapa hewa ia he naauao:
21 Anthu ena chifukwa chovomereza nzeru zotere, asochera nʼkutaya chikhulupiriro chawo. Chisomo chikhale nawe.
O ka mea a kekahi poe i hooia ai, ua haalele hoi i ka manaoio. Ia oe ke alohaia mai. Amene.