< 1 Timoteyo 6 >
1 Onse amene ali mu ukapolo ayenera kuona ambuye awo ngati oyenera kuwachitira ulemu, kuti anthu anganyoze dzina la Mulungu ndi chiphunzitso chathu.
Let all who are under the yoke of slavery hold their own masters to be deserving of honour, so that the name of God and the Christian teaching may not be spoken against.
2 Amene ambuye awo ndi okhulupirira, asawapeputse chifukwa ambuye ndi abale mʼchikhulupiriro. Mʼmalo mwake akuyenera kuwatumikira bwino chifukwa ambuye wawo ndi okondedwa monga okhulupirira ndiponso ndi odzipereka kusamalira akapolo awo. Zinthu izi ukuyenera kuziphunzitsa ndi kuwalamula anthu.
And those who have believing masters should not be wanting in respect towards them because they are their brethren, but should serve them all the more willingly because those who profit by the faithful service rendered are believers and are friends.
3 Ngati wina aphunzitsa zosiyana ndi zimenezi, wosagwirizana ndi malangizo woona a Ambuye athu Yesu Khristu ndi chiphunzitso cholemekeza Mulungu,
So teach and exhort. If any one is a teacher of any other kind of doctrine, and refuses assent to wholesome instructions--those of our Lord Jesus Christ--and the teaching that harmonizes with true godliness,
4 ameneyo ndi wodzitukumula ndipo sakudziwa chilichonse. Iyeyo ali ndi maganizo oyipa, wokonda kusemphana mawu ndi kutsutsana. Zimenezi zimabweretsa nsanje, mikangano, mʼnyozo, kuganizirana zoyipa,
he is puffed up with pride and has no true knowledge, but is crazy over discussions and controversies about words which give rise to envy, quarrelling, revilings, ill-natured suspicions,
5 ndi kulimbana kosatha pakati pa anthu amitima yopotoka amene alandidwa choonadi ndipo amaganiza kuti kulemekeza Mulungu ndi njira yopezera chuma.
and persistent wranglings on the part of people whose intellects are disordered and they themselves blinded to all knowledge of the truth; who imagine that godliness means gain.
6 Koma kulemekeza Mulungu kuli ndi phindu lalikulu.
And godliness is gain, when associated with contentment;
7 Pakuti sitinabweretse kanthu mʼdziko lapansi, ndipo sitingatengenso kanthu pochoka mʼdziko lapansi.
for we brought nothing into the world, nor can we carry anything out of it;
8 Koma ngati tili ndi chakudya ndi zovala, zimenezi zitikwanire.
and if we have food and clothing, with these we will be satisfied.
9 Anthu amene amafuna kulemera amagwa mʼmayesero ndi mu msampha ndi mʼzilakolako zambiri zopusa ndi zoopsa zimene zimagwetsera anthu mʼchitayiko ndi mʼchiwonongeko.
But people who are determined to be rich fall into temptation and a snare, and into many unwise and pernicious ways which sink mankind in destruction and ruin.
10 Pakuti kukonda ndalama ndiye muzu wa zoyipa za mitundu yonse. Anthu ena ofunitsitsa ndalama, asochera ndipo asiya njira yachikhulupiriro ndipo adzitengera zowawitsa zambiri.
For from love of money all sorts of evils arise; and some have so hankered after money as to be led astray from the faith and be pierced through with countless sorrows.
11 Koma iwe, munthu wa Mulungu, thawa zinthu zonsezi. Tsatira chilungamo, moyo wolemekeza Mulungu, chikhulupiriro, chikondi, kupirira ndi kufatsa.
But you, O man of God, must flee from these things; and strive for uprightness, godliness, good faith, love, fortitude, and a forgiving temper.
12 Menya nkhondo yabwino yachikhulupiriro. Gwiritsitsa moyo wosatha umene anakuyitanira pamene unavomereza bwino lomwe pamaso pa mboni zambiri. (aiōnios )
Exert all your strength in the honourable struggle for the faith; lay hold of the Life of the Ages, to which you were called, when you made your noble profession of faith before many witnesses. (aiōnios )
13 Ndikukulamula pamaso pa Mulungu amene amapatsa moyo zinthu zonse, ndiponso pamaso pa Khristu Yesu amene pochitira umboni pamaso pa Pontiyo Pilato, ananena zoona zenizeni.
I charge you--as in the presence of God who gives life to all creatures, and of Christ Jesus who at the bar of Pontius Pilate made a noble profession of faith--
14 Usunge lamuloli mopanda banga ndi cholakwa kufikira Ambuye athu Yesu Khristu ataonekera.
that you keep God's commandments stainlessly and without reproach till the Appearing of our Lord Jesus Christ.
15 Pa nthawi yake Mulungu adzamubweretsa kwa ife. Mulungu ndi wodalitsika ndipo Iye yekha ndiye Wolamulira, Mfumu ya mafumu, Mbuye wa ambuye.
For, as its appointed time, this will be brought about by the blessed and only Sovereign, the King of kings and Lord of lords,
16 Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni. (aiōnios )
who alone possesses immortality, dwelling in unapproachable light, and whom no man has seen or can see. To Him be eternal honour and power! Amen. (aiōnios )
17 Anthu onse amene ali ndi chuma uwalamule kuti asanyade kapena kuyika mitima yawo pa chuma chimene nʼchosadalirika. Koma chiyembekezo chawo chikhale mwa Mulungu amene amatipatsa mowolowamanja zonse zotisangalatsa. (aiōn )
Impress on those who are rich in the present age that they must not be haughty nor set their hopes on riches--that unstable foundation--but on God who provides us richly with all things for our enjoyment. (aiōn )
18 Uwalamule kuti azichita zabwino, kuti azikhala olemera pa ntchito zabwino, owolowamanja ndi okonda kugawana zinthu zawo ndi anzawo.
They must be beneficent, rich in noble deeds, open-handed and liberal;
19 Potero adzadziwunjikira chuma chokhalitsa ngati maziko okhazikika a nthawi zakutsogolo, kuti akalandire moyo, umene ndi moyo weniweni.
storing up for themselves that which shall be a solid foundation for the future, that they may lay hold of the Life which is life indeed.
20 Timoteyo, samalitsa zimene unapatsidwa. Upewe nkhani zopanda pake zosalemekeza Mulungu ndiponso maganizo otsutsana amene amaganizidwa molakwika kuti ndi nzeru.
O Timothy, guard the truths entrusted to you, shunning irreligious and frivolous talk, and controversy with what is falsely called 'knowledge';
21 Anthu ena chifukwa chovomereza nzeru zotere, asochera nʼkutaya chikhulupiriro chawo. Chisomo chikhale nawe.
of which some have spoken boastfully in connexion with the true faith, and have erred. Grace be with you all.