< 1 Timoteyo 5 >
1 Usadzudzule munthu wachikulire mokalipa, koma umuchenjeze ngati abambo ako. Achinyamata uwatenge ngati abale ako.
Nnaakalipile bhakongopa, ikabhe mwaaleye mbuti ainabhenu. Na bhashanda mwaatendelanje mbuti ashaapwenu,
2 Amayi achikulire uwatenge ngati amayi ako ndipo amayi achitsikana uwatenge ngati alongo ako, nʼkuyera mtima konse.
bhanabhakongwe bhakongopa, mbuti anyinabhenu, na bhali mbuti ashaalumbu bhenu, nkuikonjeleya mowe.
3 Uziwachitira ulemu akazi amasiye amene ali okhaokha.
Mwaalelanje bhanabhakongwe bhalinginji bhashitenga bha kweli.
4 Koma ngati mkazi wamasiye ali ndi ana ndi zidzukulu, anawo ayambe aphunzira kukwaniritsa udindo wawo pa banja lawo moopa Mulungu, potero akubweza zabwino kwa makolo awo ndi agogo awo. Pakuti zimenezi ndiye zimakondweretsa Mulungu.
Ikabheje bhashitenga bhakwete bhana eu bhaukulu, bhana eu bhaukulubho, bhaijiganyanje kutenda ipinjikwa na dini kwa ashaalongo ajabhonji nkwaalelanga bhaakwetenje, pabha genego ni ga pingwa na a Nnungu.
5 Mkazi wamasiye amene ali yekha ndi wopanda womuthandiza, ameneyo wayika chiyembekezo chake pa Mulungu, ndipo amapemphera kosalekeza usana ndi usiku kuti Mulungu azimuthandiza.
Bhai bhakongwe bhali bhashitenga kweli, bhangali mundu jwa kwaajangutila, bhenebho bhashibhika ngulupai yabho kwa a Nnungu, na bhanalonjeya nkwaatindibhalila na nkwaajuga shilo na mui.
6 Koma mkazi wamasiye amene amangokhalira kuchita zosangalatsa moyo wake, wafa kale ngakhale akanali ndi moyo.
Ikabheje nshitenga akagulila ilokoli yangali ya mmbone jwenejo awile, nkali alonjeye.
7 Pereka malangizo amenewa kwa anthu kuti akhale opanda zolakwa.
Mwaalajilanje genego, nkupinga bhanagambwanje.
8 Ngati wina sasamalira abale ake, makamaka a mʼbanja mwake mwenimweni, ameneyo wakana chikhulupiriro ndipo ndi woyipa kuposa wosakhulupirira.
Ikabheje mundu jojowe alepela kulela ashaalongo ajakwe, yani bhandu bha nnikaja lyakwe, jwenejo ajikanile ngulupai, numbe jwangali jwa mmbone kupunda mundu jwangali ngulupai.
9 Mayi wamasiye aliyense amene sanakwanitse zaka 60 zakubadwa, asakhale mʼgulu la akazi amasiye. Akhale woti anakwatiwapo ndi mwamuna wake mmodzi yekha.
Bhakongwe bhashitenga bhanajandikwe munkumbi gwa bhashitenga bhakaishile yaka makumi shita, numbe bhabhe bhakongwe bhalombilwe na kamope,
10 Akhale mayi woti amadziwika bwino pa ntchito zake zabwino monga kulera ana, kusamalira alendo, kusambitsa mapazi a anthu a Mulungu, kuthandiza amene ali pa mavuto ndi kudzipereka pa ntchito zonse zabwino.
na bhalumbililwe itendi ya mmbone, nkulela bhana bhabho ukoto na nkuposhela bhajeninji, na nkwaatendelanga ya mituka bhandunji bha ukonjelo na nkujangutila bhandunji bhalaga, na nkutumbilila kutenda ya mmbone.
11 Akazi amasiye achitsikana, usawayike mʼgulu limeneli. Pakuti zilakolako zawo zikayamba kuwavutitsa nʼkuwalekanitsa ndi Khristu, amafuna kukwatiwanso.
Ikabheje bhashitenga bhalinginji bhali, nnaajandikanje, pabha shilokoli sha nshiilu shipundaga, shibhalekanje kwaapinga a Kilishitu, nilombwa kabhili,
12 Zikatero amadziweruza okha chifukwa aphwanya lonjezo lawo loyamba.
penepo shibhaukumulwanje kuti bhashilekanga ngulupai jabhonji ja ntai.
13 Komanso amakhala ndi chizolowezi cha ulesi ndi kumangoyenda khomo ndi khomo. Ndipo sikungokhala aulesi kokha komanso kuchita miseche, kududukira za eni ake, kumangokamba zinthu zosayenera kukamba.
Numbe pamo na genego, bhashitenga bha nneyo paatandubha ukata, na kukonangona mmajumba ga bhandunji, na nngabha ukatape, ikabheje na lungw'enyi, na kwiijinjiya mmalobhe ga bhananji, akuno bhalibheleketanga ikapinjikwa bheleketa.
14 Kotero, ndikulangiza akazi amasiye achitsikana kuti akwatiwe, akhale ndi ana, asamalire makomo awo ndipo asamupatse mdani mpata wonyoza
Bhai nne punguganishiya, bhashitenga bhakanabhe kongopalanga, bhalombwanje na bhakolanje bhana na bhagoyanje nyumba yabhonji, nkupinga ashaamagongo ajetu bhanakolanje sha kutugamba.
15 Akazi amasiye ena apatuka kale nʼkumatsatira Satana.
Pabha, bhashitenga bhananji bhaobhilenje nikunkagula Lishetani.
16 Ngati mayi aliyense wokhulupirira ali ndi akazi amasiye amene akuwasamalira, apitirizebe kuwasamalira ndipo asalemetse mpingo, kuti mpingo uthandize akazi amasiye amene ali okhaokha.
Ikabheje bhakongwe Bhakilishitu, bhakolaga alongo ajabho bhashitenga, bhanapinjikwa kwaajangutila, nngabha kulileshela likanisha lyene liengolyo, nkupinga likanisha likole liengo lya kwaalelanga bhashitenga bhapundilenje kulaga.
17 Akulu ampingo amene amayangʼanira bwino zochitika za mu mpingo, ndi oyenera ulemu wowirikiza, makamaka amene ntchito yawo ndi kulalikira ndi kuphunzitsa.
Bhanangulungwa bhatendanga liengo ukoto nnikanisha, inapinjikwa bhalipwanje pabhili, na kaje bhene bhatendanga liengo lya lunguya na jiganya bhala.
18 Pakuti Mawu a Mulungu amati, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu,” ndi “Wantchito ngoyenera kulandira malipiro ake.”
Pabha Majandiko ga Ukonjelo ganalugula, “Nnantabhe kangw'a ng'ombe alilibhata yalya nkukubhata.” Kabhili, “Nkamula liengo anapinjikwa kupata nshaala gwakwe.”
19 Usamamvere mawu oneneza akulu ampingo pokhapokha patakhala mboni ziwiri kapena zitatu.
Nnakunde malobhe ga kwaashitakiya bhanangulungwa bha likanisha, gwangali bhaakong'ondela bhabhili eu bhatatu.
20 Akulu ampingo amene akuchimwa, uwadzudzule poyera kuti ena aphunzirepo.
Bhene bhatendanga ilebho, mwaaleyanje palugwinjili, nkupinga bhananji bhajogopanje.
21 Ndikukulamulira pamaso pa Mulungu, pamaso pa Yesu Khristu ndi pamaso pa angelo osankhika, kuti usunge malangizowa mosachotsera ndipo usachite kalikonse mokondera.
Ngunakunnajila pa meyo ga a Nnungu na a Yeshu Kilishitu na ashimalaika bha ukonjelo, nkamule gene malajilogo gwangali luagu wala kummika mundu pa ligaa.
22 Usafulumire kusanjika manja munthu, ndipo usavomerezane ndi anthu ena pa machimo. Usunge bwino kuyera mtima kwako.
Nnatende shangu kummishila mundu makono. Wala nnaijinjiye muilebho ya bhananji, mwiiteije nnainyatiye.
23 Uleke kumangomwa madzi okha, koma uzimwako vinyo pangʼono chifukwa cha vuto lako la mʼmimba ndi kudwala kwako kwa pafupipafupi.
Tandubhila nnaino nnangw'e mashipe, ikabheje na divai kashoko, kwa ligongo lya matumbo genu gakumpoteka na ilwele inkulwala lwala.
24 Anthu ena machimo awo amaonekeratu poyera, amakafika pa mpando wachiweruzo eni akewo asanakafike. Machimo a anthu ena amabwera mʼmbuyo mwawo.
Yambi ya bhandunji bhana inabhoneka gwangali nng'iyo na inalongolela kuukumu, ikabheje yambi ya bhananji pabhoneka kungai.
25 Momwemonso, ntchito zabwino zimaonekera poyera, ndipo ngakhale zipande kutero, sizingatheke kubisika.
Nneyo peyo na itendi ya mmbone, inabhoneka gwangali nng'iyo na nkali gakamanyikago gakaishika.