< 1 Timoteyo 3 >

1 Mawu woona ndi awa: Ngati munthu akufunitsitsa atakhala woyangʼanira, ndiye kuti akufuna ntchito yabwino.
Voici une vérité certaine: Si quelqu’un désire l’épiscopat, il désire une œuvre bonne.
2 Tsono woyangʼanira ayenera kukhala munthu wopanda chotsutsika nacho, mwamuna wa mkazi mmodzi yekha, woganiza bwino, wodziretsa, waulemu, wosamala bwino alendo, wodziwa kuphunzitsa.
L’évêque doit donc être irréprochable, n’avoir épousé qu’une seule femme, être sobre, prudent, grave, chaste, hospitalier, capable d’enseigner;
3 Asakhale chidakwa, asakhale wandewu, koma wofatsa, asakhale wokonda mikangano, kapena wokonda ndalama.
Non porté à boire et à frapper; mais modéré, ennemi des contestations, désintéressé, mais surtout
4 Akhale wodziwa kusamala bwino banja lake ndi kulera ana ake bwino, kuti akhale omvera ndi aulemu weniweni.
Gouvernant bien sa maison, tenant ses enfants soumis, en toute chasteté
5 (Ngati munthu sadziwa kusamala banja lake lomwe, angathe bwanji kusamala mpingo wa Mulungu?)
(Car si quelqu’un ne sait pas gouverner sa propre maison, comment gouvernera-t-il l’Eglise de Dieu?)
6 Asakhale wongotembenuka mtima kumene kuopa kuti angadzitukumule napezeka pa chilango monga Satana.
Non néophyte, de peur qu’enflé d’orgueil, il ne tombe dans la condamnation du diable.
7 Ayeneranso kukhala munthu wambiri yabwino ndi akunja, kuti anthu asamutonze nagwa mu msampha wa Satana.
Il faut aussi qu’il ait un bon témoignage de ceux qui sont dehors, afin qu’il ne tombe pas dans l’opprobre et dans les filets du diable.
8 Momwemonso atumiki, akhale anthu oyenera ulemu, woona mtima, osakhala okonda zoledzeretsa, osakonda kupeza zinthu mwachinyengo.
Que les diacres, de même, soient pudiques, qu’ils n’aient pas deux langues; qu’ils ne soient pas adonnés au vin, qu’ils ne courent pas après un gain sordide;
9 Ayenera kugwiritsa mozama choonadi cha chikhulupiriro ndi kukhala ndi chikumbumtima chabwino.
Qu’ils conservent le mystère de la foi dans une conscience pure.
10 Ayambe ayesedwa kaye, ndipo ngati palibe kanthu kowatsutsa, aloleni akhale atumiki.
Et qu’eux aussi soient d’abord éprouvés; et qu’ensuite ils exercent le ministère s’ils sont sans reproche.
11 Momwemonso, akazi akhale olemekezeka, osasinjirira koma oganiza bwino ndi odalirika pa chilichonse.
Que pareillement les femmes soient pudiques, non médisantes, mais sobres, fidèles en toutes choses.
12 Mtumiki akhale wokhulupirika kwa mkazi wake ndipo ayenera kukhala wosamalira bwino ana ake ndi onse a pa khomo pake.
Que les diacres n’aient épousé qu’une seule femme; qu’ils gouvernent bien leurs enfants et leurs propres maisons.
13 Iwo amene atumikira bwino amakhala ndi mbiri yabwino ndipo amakhala chitsimikizo chachikulu cha chikhulupiriro chawo mwa Khristu Yesu.
Car ceux qui auront bien rempli leur ministère, acquerront un rang honorable et une grande confiance dans la foi qui est dans le Christ Jésus.
14 Ngakhale ndili ndi chiyembekezo choti ndifika komweko posachedwapa, ndikukulemberani malangizo awa.
Je t’écris ces choses, quoique j’espère aller bientôt te voir;
15 Ine zina zikandichedwetsa kubwera, mudziwe za mmene anthu ayenera kukhalira mʼNyumba ya Mulungu, imene ndi mpingo wa Mulungu wamoyo, mzati ndi maziko achoonadi.
Afin que, si je tarde, tu saches comment te conduire dans la maison de Dieu, qui est l’Eglise du Dieu vivant, la colonne et le fondement de la vérité.
16 Mosakayikira, chinsinsi cha chikhulupiriro chathu chachikulu: Khristu anaonekera ali ndi thupi la munthu, Mzimu anamuchitira umboni, angelo anamuona, analalikidwa pakati pa mitundu yonse, dziko lapansi linamukhulupirira, anatengedwa kupita kumwamba mwa ulemerero.
Et il est manifestement grand ce mystère de piété, qui s’est révélé dans la chair, qui a été justifié par l’Esprit, dévoilé aux anges, annoncé aux nations, cru dans le monde, reçu dans la gloire.

< 1 Timoteyo 3 >