< 1 Timoteyo 2 >
1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
Henu awali jha ghoha, nilonda maombi, ni dua, ni maombesi, ni shukrani fibhombekayi kwa ndabha jha bhanu bhoha,
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
kwandabha jha bhafalme ni bhoha ambabho bhajhele mu mamlaka, ili kwamba tubhwesiajhi kuishi maisha gha amani ni bhololo mu utauwa bhuoha ni litengo.
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
E'le linofu na lyalijhedekelibhwa palongolo pa K'yara mwokozi ghwitu.
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
Muene inoghele kujha bhanu bhoha bhaokolibhwayi na bhabhwesiajhi kujhimanya kweli.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
Kwa kujha ajhe K'yara mmonga, na ajhe mpatanisi mmonga kati jha K'yara ni mwanadamu ambajhe ndo Kristu Yesu.
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
Akihomisi muene kama fidia kwa bhoha, kama bhushuhuda kwa bhwakati muafaka.
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
Kwa ndabha ejhe, nene nemwene, nabhombiki kujha mjumbe ghwa injili ni mitume. Nijobha bhukweli. Nijobhalepi udesi. Nene ne mwalimu bhanu bha mataifa mu imani ni bhukweli.
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
Henu, nilonda bhagosi khila mahali bhas'okayi ni kujhinula mabhoko matakatifu bila ghadhabu ni mashaka.
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
Fefuefu, nilonda bhadala bhakifwekajhi maguanda ghaghilondeka, gha litengo ni kwifigha. Bhasijhi ni njuili syasipotibhu, au dhahabu, au lulu, au maguanda gha gharama mbaha.
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
Kabhele nilonda bhafwalayi maguanda ambagho ghakabhalondeka bhadala bhabhikiri uchaji kwa kup'et'ela matendo manofu.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
N'dala na akimanyisiajhi mu hali jha bhololo ni kwa bhutii bhuoha.
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
Nikanduhurusu lepi n'dala kumanyisya, au kujha ni mamlaka panani pa n'gosi bali atamajhi mu hali jha kugudama.
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
Kwa kujha Adamu abhombiki hoti, kisha Eva.
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
Adamu akofibhu lepi, lakini n'dala akofibhu nesu mu bhuasi.
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
Hata naha, ibetakuokolibhwa kup'el'ela kuhogola bhana, kama bhibetakujhendelela mu imani ni luganu ni mu bhutakasu ni luhala lunofu.