< 1 Timoteyo 2 >

1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
ועתה קדם כל דבר אבקשה מכם לשאת תפלות ותחנונים ובקשות ותודות בעד כל בני אדם׃
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
בעד המלכים וכל השליטים למען נחיה חיי השקט ובטח בכל חסידות וישר׃
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
כי כן טוב ורצוי בעיני אלהים מושיענו׃
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
אשר חפצו שיושעו כל בני האדם ויגיעו להכרת האמת׃
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
כי אחד הוא האלהים ואחד הוא העמד בין אלהים ובין בני אדם הוא בן אדם המשיח ישוע׃
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
אשר נתן את נפשו כפר בעד כל וזאת העדות הבאה בעתה׃
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
אשר אני הפקדתי לה לכרוז ולשליח אמת אני אמר במשיח ולא אשקר מורה הגוים באמונה ובאמת׃
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
לכן רצוני שיתפללו האנשים בכל מקום וישאו ידיהם קדש בלי כעס ומדון׃
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
וכן גם הנשים תתיפינה בתלבשת נאה עם בשת פנים וצניעות לא במחלפות הראש לא בזהב לא בפנינים ולא במלבושים יקרים׃
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
אלא כמו שהוא הגון לנשים אשר בחרו להן יראת אלהים במעשים טובים׃
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
האשה תלמד דומם בכל הכנעה׃
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
ואינני נתן רשות לאשה ללמד אף לא להתנשא על האיש אלא תדום׃
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
כי אדם נוצר בראשונה ואחריו חוה׃
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
ואדם לא נפתה כי האשה שמעה לקול המשיא ותבא לידי עברה׃
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
אבל תושע בלדתה בנים אם תעמדנה באמונה ובאהבה ובקדשה עם הצניעות׃

< 1 Timoteyo 2 >