< 1 Timoteyo 2 >
1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
The first (OR, most important) thing that I urge [you to tell your congregation] is that [Christians] should continually ask [God] for [what they need]. They should also pray to God [for all other people], and they should be thanking [God].
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
Specifically, they should pray for rulers and for all [other people] who (are in important government positions/have authority), in order that [God will help them to rule]. [As God enables the rulers to rule well], we can live very peaceably as we conduct ours lives doing all that God and others consider to be right and proper.
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
It is good [to pray like that, and] it pleases God, who saves us, when we pray like that.
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
He desires to save everyone. He wants everyone to fully know [and accept] his true [message].
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
He is the [only] one [true] God! And there is [only] one person who talks to God on behalf of people. That person is Christ Jesus, who [himself] is a man!
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
He gave (his [life/himself]) [as a sacrifice] in order to ransom/redeem all [people], which showed at the proper time [that God desires that all people be saved] {[to save all people]}.
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
As for me, he appointed me to declare [this message] and to be an apostle. I am telling the truth [about God appointing me]. I am not lying! He appointed me to teach the non-Jews that they should believe God’s true message.
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
I desire that in every place [where believers worship], the men who pray publicly [MTY] should be men who are not practicing sin. When they pray, they should not be angry [with anyone] and they should not doubt [that God will answer] their prayers (OR, should not quarrel with anyone).
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
[I would like that] the clothing that women wear be (modest and sensible/proper and appropriate) [DOU]. I want them to not fix their hair in fancy/elaborate ways, nor wear gold [jewelry], nor pearls, nor expensive clothing [in order that they may make themselves attractive].
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
Instead, they should be doing things that women who (claim to/say that they) worship God should do; that is, they should be doing good deeds.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
Women must learn to [listen] quietly [during the worship services] and to fully subject themselves [to the leaders of the congregation].
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
I do not permit women to teach [men spiritual truth publicly], and I do not permit them to have authority over men. Instead, [I desire] that women [listen] quietly [during the worship services].
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
Keep in mind that God made Adam first, and afterwards he made Eve,
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
and that it was not Adam whom [Satan] deceived. As a result of the woman being deceived, she sinned. She did what God had told her not to do.
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
But even though she did that, now women will be saved {God will accept women} as they bear children if they continue to trust [God] and if they continue to love others, and if they continue to live in a way that is [more and more] (acceptable to God/like God wants them to), and if they continue to be modest.