< 1 Timoteyo 2 >

1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
Jeg formaner da først af alt til, at der holdes Bønner, Påkaldelser, Forbønner, Taksigelser for alle Mennesker,
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
for Konger og alle dem, som ere i Højhed, at vi må leve et roligt og stille Levned i al Gudsfrygt og Ærbarhed;
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
dette er smukt og velbehageligt for Gud, vor Frelser,
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
som vil, at alle Mennesker skulle frelses og komme til Sandheds Erkendelse.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
Thi der er een Gud, og også een Mellemmand imellem Gud og Mennesker, Mennesket Kristus Jesus,
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
som gav sig selv til en Genløsnings Betaling for alle, hvilket er Vidnesbyrdet i sin Tid,
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
og for dette er jeg bleven sat til Prædiker og Apostel (jeg siger Sandhed, jeg lyver ikke), en Lærer for Hedninger i Tro og Sandhed.
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
Så vil jeg da, at Mændene på ethvert Sted, hvor de bede, skulle opløfte fromme Hænder uden Vrede og Trætte.
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
Ligeså, at Kvinder skulle pryde sig i sømmelig Klædning med Blufærdighed og Ærbarhed, ikke med Fletninger og Guld eller Perler eller kostbar Klædning,
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
men, som det sømmer sig Kvinder, der bekende sig til Gudsfrygt, med gode Gerninger.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
En Kvinde bør i Stilhed lade sig belære, med al Lydighed;
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
men at være Lærer tilsteder jeg ikke en Kvinde, ikke heller at byde over Manden, men at være i Stilhed.
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
Thi Adam blev dannet først, derefter Eva;
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
og Adam blev ikke bedraget, men Kvinden blev bedraget og er falden i Overtrædelse.
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
Men hun skal frelses igennem sin Barnefødsel, dersom de blive i Tro og Kærlighed og Hellighed med Ærbarhed.

< 1 Timoteyo 2 >