< 1 Atesalonika 1 >

1 Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu.
پولس و سلوانس و تیموتاوس، به کلیسای تسالونیکیان که در خدای پدر وعیسی مسیح خداوند می‌باشید. فیض و سلامتی از جانب پدر ما خدا و عیسی مسیح خداوند با شما باد.۱
2 Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu.
پیوسته درباره جمیع شما خدا را شکرمی کنیم و دائم در دعاهای خود شما را ذکرمی نماییم،۲
3 Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
چون اعمال ایمان شما و محنت محبت و صبر امید شما را در خداوند ما عیسی مسیح در حضور خدا و پدر خود یاد می‌کنیم.۳
4 Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani,
زیرا که‌ای برادران و‌ای عزیزان خدا، ازبرگزیده شدن شما مطلع هستیم،۴
5 chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni.
زیرا که انجیل ما بر شما محض سخن وارد نشده، بلکه با قوت وروح‌القدس و یقین کامل، چنانکه می‌دانید که درمیان شما بخاطر شما چگونه مردمان شدیم.۵
6 Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera.
وشما به ما و به خداوند اقتدا نمودید و کلام را درزحمت شدید، با خوشی روح‌القدس پذیرفتید،۶
7 Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya.
به حدی که شما جمیع ایمانداران مکادونیه واخائیه را نمونه شدید،۷
8 Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu,
بنوعی که از شما کلام خداوند نه فقط در مکادونیه و اخائیه نواخته شد، بلکه در هرجا ایمان شما به خدا شیوع یافت، بقسمی که احتیاج نیست که ما چیزی بگوییم،۸
9 pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona.
زیرا خود ایشان درباره ما خبر می‌دهند که چه قسم وارد به شما شدیم و به چه نوع شما از بتها به سوی خدا بازگشت کردید تا خدای حی حقیقی را بندگی نمایید،۹
10 Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.
و تا پسر او را از آسمان انتظاربکشید که او را از مردگان برخیزانید، یعنی عیسی که ما را از غضب آینده می‌رهاند.۱۰

< 1 Atesalonika 1 >