< 1 Atesalonika 5 >

1 Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
Sasa, kwa habari ya muda na nyakati, ndugu, hamna haja kwamba kitu chochote kiandikwe kwenu.
2 chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
Kwa kuwa ninyi wenyewe mwajua kwa usahihi ya kuwa siku ya Bwana inakuja kama mwizi ajapo usiku.
3 Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
Pale wasemapo kuna “Amani na usalama”, ndipo uharibifu huwajia ghafla. Ni kama utungu umjiavyo mama mwenye mimba. Hawataepuka kwa njia yeyote.
4 Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
Lakini ninyi, ndugu hampo kwenye giza hata ile siku iwajie kama mwizi.
5 Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
Kwa maana ninyi nyote ni wana wa nuru na wana wa mchana. Sisi siyo wana wa usiku au wa gizani.
6 Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
Hivyo basi, tusilale kama wengine walalavyo. Bali tukeshe na kuwa makini.
7 Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
Kwa kuwa wanaolala hulala usiku na wanao lewa hulewa usiku.
8 Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
Kwa kuwa sisi ni wana wa mchana, tuwe makini. Tuvae ngao ya imani na upendo, na, kofia ya chuma, ambayo ni uhakika wa wokovu wa wakati ujao.
9 Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
Kwa kuwa Mungu hakutuchagua mwanzo kwa ajili ya gadhabu, bali kwa kupata wokovu kwa njia ya Bwana Yesu Kristo.
10 Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
Yeye ndiye aliyetufia ili kwamba, tukiwa macho au tumelala, tutaishi pamoja naye.
11 Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
Kwa hiyo, farijianeni na kujengana ninyi kwa ninyi, kama ambavyo tayari mnafanya.
12 Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
Ndugu, twawaomba muwatambue wale wanaotumika miongoni mwenu na wale walio juu yenu katika Bwana na wale wanao washauri.
13 Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
Tunawaomba pia muwatambue na kuwapa heshima katika upendo kwa sababu ya kazi yao. Muwe na amani miongoni mwenu ninyi wenyewe.
14 Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
Twawasihi, ndugu: muwaonye wasio kwenda kwa utaratibu, watieni moyo walio kata tamaa, Wasaidieni walio wanyonge, na muwe wavumilivu kwa wote.
15 Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
Angalieni asiwepo mtu yeyote anayelipa baya kwa baya kwa mtu yeyote. Badala yake, fanyeni yaliyo mema kwa kila mmoja wenu na kwa watu wote.
16 Kondwerani nthawi zonse.
Furahini siku zote.
17 Pempherani kosalekeza.
Ombeni bila kukoma.
18 Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
Mshukuruni Mungu kwa kila jambo, kwa sababu hayo ndiyo mapenzi ya Mungu kwenu katika Yesu Kristo.
19 Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
Msimzimishe Roho.
20 Musanyoze mawu a uneneri.
Msiudharau unabii.
21 Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
Yajaribuni mambo yote. Mlishike lililo jema.
22 Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
Epukeni kila mwonekano wa uovu.
23 Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
Mungu wa amani awakamilishe katika utakatifu. Roho, nafsi na mwili vitunzwe pasipo mawaa katika kuja kwake Bwana wetu Yesu Kristo.
24 Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
Yeye aliyewaita ni mwaminifu, naye ndiye mwenye kutenda.
25 Abale, mutipempherere.
Ndugu, tuombeeni pia.
26 Perekani moni wachikondi kwa onse.
Wasalimuni ndugu wote kwa busu takatifu.
27 Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
Nawasihi katika Bwana kwamba barua hii isomwe kwa ndugu wote.
28 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.
Neema ya Bwana wetu Yesu Kristo iwe pamoja nanyi.

< 1 Atesalonika 5 >