< 1 Atesalonika 4 >

1 Potsiriza, abale, tinakulangizani kale momwe mukuyenera kukhalira kuti mukondweretse Mulungu, monga momwe mukukhaliramo. Tsopano tikukupemphani ndi kukulimbikitsani mwa Ambuye Yesu kuti muchite zimenezi koposa kale.
خلاصه‌ای برادران، از شما در عیسی خداوند استدعا و التماس می‌کنیم که چنانکه از ما یافته‌اید که به چه نوع باید رفتار کنیدو خدا را راضی سازید، به همانطور زیادتر ترقی نمایید.۱
2 Inu mukudziwa malangizo amene tinakupatsani mwa ulamuliro wa Ambuye Yesu.
زیرا می‌دانید چه احکام از جانب عیسی خداوند به شما دادیم.۲
3 Ndi chifuniro cha Mulungu kuti muyeretsedwe: kuti mupewe dama;
زیرا که این است اراده خدا یعنی قدوسیت شما تا از زنا بپرهیزید.۳
4 aliyense wa inu aphunzire kulamulira thupi lake mʼnjira yoyera ndi yaulemu,
تاهرکسی از شما بداند چگونه باید ظرف خویشتن را در قدوسیت و عزت دریابد،۴
5 osati yotsata chilakolako chonyansa monga amachitira akunja, amene sadziwa Mulungu.
و نه در هوس شهوت، مثل امت هایی که خدا را نمی شناسند.۵
6 Pa zimenezi munthu asachimwire mʼbale wake kapena kumuonerera. Ambuye adzalanga anthu onse amene amachita machimo amenewa, monga tinakuwuzani kale ndi kukuchenjezani.
و تا کسی در این امر دست تطاول یا طمع بر برادر خود دراز نکند، زیرا خداوند از تمامی چنین کارها انتقام کشنده است.۶
7 Pakuti Mulungu sanatiyitane kuti tizichita zonyansa, koma kuti tikhale oyera mtima.
چنانکه سابق نیز به شما گفته و حکم کرده‌ایم، زیرا خدا ما را به ناپاکی نخوانده است، بلکه به قدوسیت.۷
8 Choncho, aliyense amene akukana malangizo awa sakukana munthu koma Mulungu, Mulungu weniweniyo amene amakupatsani Mzimu Woyera.
لهذا هرکه حقیر شمارد، انسان را حقیر نمی شمارد، بلکه خدا را که روح قدوس خود را به شما عطا کرده است.۸
9 Tsono kunena za kukondana wina ndi mnzake, nʼkosafunikira kuti tikulembereni, popeza ndi Mulungu amene anakuphunzitsani za kukondana wina ndi mnzake.
اما در خصوص محبت برادرانه، لازم نیست که به شما بنویسم، زیرا خود شما از خدا آموخته شده‌اید که یکدیگر را محبت نمایید؛۹
10 Ndipo kunena zoona, mumakonda abale onse a mʼbanja la Mulungu a ku Makedoniya. Komabe, abale tikukulimbikitsani kuti muzichita zimenezi koposa kale.
و چنین هم می‌کنید با همه برادرانی که در تمام مکادونیه می‌باشند. لیکن‌ای برادران از شما التماس داریم که زیادتر ترقی کنید.۱۰
11 Yesetsani kuti mukhale moyo wofatsa. Aliyense asamale ntchito yakeyake ndi kugwira ntchito ndi manja ake.
و حریص باشید در اینکه آرام شوید و به‌کارهای خود مشغول شده، به‌دستهای خویش کسب نمایید، چنانکه شما راحکم کردیم،۱۱
12 Mukatero akunja adzalemekeza makhalidwe anu a tsiku ndi tsiku, ndi kuti inuyo mukhale osadalira wina aliyense.
تا نزد آنانی که خارج‌اند بطورشایسته رفتار کنید و به هیچ‌چیز محتاج نباشید.۱۲
13 Abale, ife sitikufuna mukhale osadziwa za amene akugona, kapena kumva chisoni ngati anthu ena opanda chiyembekezo.
اما‌ای برادران نمی خواهیم شما از حالت خوابیدگان بی‌خبر باشید که مبادا مثل دیگران که امید ندارند، محزون شوید.۱۳
14 Ife timakhulupirira kuti Yesu anamwalira naukanso. Moteronso timakhulupirira kuti amene anamwalira ali mwa Yesu, Mulungu adzawaukitsa nʼkubwera nawo pamodzi ndi Yesuyo.
زیرا اگر باورمی کنیم که عیسی مرد و برخاست، به همینطورنیز خدا آنانی را که در عیسی خوابیده‌اند با وی خواهد آورد.۱۴
15 Molingana ndi mawu a Ambuye mwini, tikukuwuzani kuti, ife amene tikanali ndi moyo, otsala mpaka kubwera kwa Ambuye, sitidzawasiya kumbuyo amene anagona kale.
زیرا این را به شما از کلام خدامی گوییم که ما که زنده و تا آمدن خداوند باقی باشیم برخوابیدگان سبقت نخواهیم جست.۱۵
16 Pakuti Ambuye mwini adzatsika kuchokera kumwamba, ndi mfuwu waulamuliro, ndi liwu la mngelo wamkulu, ndi kulira kwa lipenga la Mulungu, ndipo akufa amene ali mwa Yesu adzauka poyamba.
زیرا خود خداوند با صدا و با آواز رئیس فرشتگان و با صور خدا از آسمان نازل خواهدشد و مردگان در مسیح اول خواهند برخاست.۱۶
17 Kenaka, ife amene tili ndi moyo, otsalafe, tidzakwatulidwa pamodzi ndi iwo mʼmitambo kukakumana ndi Ambuye mlengalenga. Tsono ife tidzakhala ndi Ambuye mpaka muyaya.
آنگاه ما که زنده و باقی باشیم، با ایشان در ابرهاربوده خواهیم شد تا خداوند را در هوا استقبال کنیم و همچنین همیشه با خداوند خواهیم بود.۱۷
18 Nʼchifukwa chake tsono muzilimbikitsana ndi mawu amenewa.
پس بدین سخنان همدیگر را تسلی دهید.۱۸

< 1 Atesalonika 4 >