< 1 Atesalonika 1 >
1 Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu.
Павел, та Сильван, та Тимотей до церков Солунських. у Бозї Отцї і Господї Ісусї Христї: Благодать вам і мир од Бога Отця і Господа Ісуса Христа.
2 Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu.
Дякуємо Богові всякого часу за всїх вас, роблячи спомин про вас у молитвах наших,
3 Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
без перестану згадуючи ваше діло віри, і працю любови, і терпіннє уповання на Господа нашого Ісуса Христа перед Богом і Отцем нашим,
4 Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani,
знаючи, браттє Богові любе, вибраннє ваше.
5 chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni.
Бо благовістє наше не було до вас у слові тілько, а і в силї, і в Дусі сьвятому, і в великій певнотї, яко ж і знаєте, які ми були між вами задля вас.
6 Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera.
І ви стали послїдувателями нашими і Господнїми, прийнявши слово в великому горю з радощами Духа сьвятого,
7 Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya.
так що ви стали ся взором усім віруючим у Македониї і Ахаї.
8 Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu,
Од вас бо промчало ся слово Господнє не тілько в Македониї і Ахаї, та й у всяке місце віра ваша в Бога пройшла, так що не треба нам що й казати.
9 pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona.
Вони бо самі про нас звіщають, який вхід мали ми до вас і як ви обернулись до Бога од ідолів, служити Богу живому і правдивому,
10 Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.
і ждати Сина Його з небес, котрого воскресив з мертвих, Ісуса, збавляючого нас від наступаючого гнїва.