< 1 Samueli 1 >

1 Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
Ie henane zay, teo t’indaty e Ramataime-zofime, am-bohibohi’i Efraime ao atao Elkanà, ana’ Ierohame, ana’ i Elihò, ana’ i Tohò ana’ i Tsofe, nte-Efraime.
2 Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
Roe ty vali’e, ty añara’ ty raike, Khanà, ty añara’ty raike, Peninà; nanañ’ anake t’i Peninà, fe mbetsiterake t’i Khanà.
3 Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
Ie amy zay niavotse i rova’ey boa-taoñe indatiy nitalaho naho nisoroñe am’ Iehovà’ i Màroy e Silò añe. Mpisoroñe amy Iehovà henane zay t’i Kofený naho i Pinekase.
4 Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
Ie tsatoke ty andro hanoen- tsoroñe le songa nanjotsoa’e t’i Peninà tañanjomba’e naho o ana-dahi’e naho anak’ ampela’e iabio;
5 Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
tinolo’e anjara mañeva t’i Khanà, fa i Khanà ty nikokoa’e, fe kinape’ Iehovà ty hovi’e.
6 Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
Le nanolo-tsotry aze nainai’e i rafe’ey, nembere’e amy te nampikitihe’ Iehovà i hovi’ey.
7 Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
Aa le nitolom-panao izay an-taoñ’an-taon-dre, ie nionjomb’ amy anjomba’ Iehovày mb’eo, le nampisoañe’e avao; ie nirovetse, tsy nete nikama.
8 Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
Aa le hoe t’i Elkanà vali’e ama’e, O Khanà, ino o iroveta’oo? akore te tsy mihinañe? ino ty mampalorè ty tro’o? tsy lombolombo’ ty ana-dahy folo ama’o v’irahoo?
9 Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
Aa ie fa nikama naho ninoñe e Silò ao iereo le niongake t’i Khanà, —ie amy zao niambesatse amy fiambesa’e an-tokonan-dalambein’ anjomba’ Iehovày t’i Elý mpisoroñe;
10 Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
le nitalaho amy Iehovà an-kafairan’ arofo i rakembay vaho nangololoike ty rovetse.
11 Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
Le nifanta an-titike ty hoe: O ry Iehovà’ i Màroy, naho toe ho vazoho’o ty fisotrian’ anak’ ampata’o toy, naho hahatiahy ahy, naho tsy handikofa’o o fetrek’oro’oo naho ho tolora’o ana-dahy ty mpitoro’o ampela, le hatoloko am’Iehovà ho amo hene andro hiveloma’eo vaho tsy hozaem-piharatse ty añambone’e.
12 Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
Aa ie nitolon-kalaly añatrefa’ Iehovà, le nioni’ i Elý i falie’ey.
13 Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
Nisaontsy añ’ arofo’e ao t’i Khanà, o fivimbi’eo avao ty nihetseke, le tsy nirey i fiarañanaña’ey; aa le natao’ i Elý t’ie nijike.
14 Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
Le hoe t’i Elý tama’e, Ampara’ te ombia t’ihe ho màmo avao? adono añe o divai’oo.
15 Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
Nanoiñe aze ty Khanà, amy ty hoe: Aiy! ry talèko, ampela mioremèñe ‘no-ahoo; tsy mpinon-divay ndra tòake, fe nadoako añatrefa’ Iehovà ty troko.
16 Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
Ko atao’o ho anam-Beliale ty anak’ ampata’o, fa ami’ty hamaro-toreoko naho amy fanaheloakoy ty nivolañeko.
17 Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
Aa le nanoiñe aze t’i Elý ami’ty hoe, akia ampanintsiñañe, i Andrianañahare’ Israele ty hamale soa i nihalalia’oy.
18 Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
Aa le hoe re, Ehe te haharendre-pañisohañe am-pahaoniña’o o anak’ ampata’oo. Le niavotse i rakembay, nikama, vaho tsy nanahelo ka ty lahara’e.
19 Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
Nañampitso iereo te nitroatse naho nitalaho añatrefa’ Iehovà naho nimpoly mb’añ’anjomba’ iareo e Ramà añe; le nifañaoñe amy Khanà vali’e t’i Elkanà vaho nahatiahy aze t’Iehovà.
20 Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
Ie añe, tondroke te niareñe t’i Khanà, le nisamake ana-dahy vaho natao’e Samoele ty añara’e, Amy te nihalalieko amy Iehovà.
21 Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
Nitolom-pionjo hañenga i sorom-boa-taoñey naho hañava-pànta am’ Iehovà t’i Elkaná roandriañe rekets’ o añ’anjomba’eo.
22 Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
Fe tsy nañavelo mb’eo t’i Kaná; hoe re amy vali’ey: Ie otàñe i ajajay, le hendeseko mb’eo, hiatrefa’e am’ Iehovà, vaho ao ty himoneña’e nainai’e.
23 Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
Aa le hoe t’i Elkanà, vali’e ama’e: Ano ze atao’o ho soa; Mahaliñisa ampara’ t’ie notàñe; hajado’ Iehovà abey i tsara’ey. Aa le nandrare tobok’ ao re nampinono i ana’ey, ampara’ te notae’e.
24 Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
Aa ie notàñe i ajajay le nendese’e mindre ama’e nionjoñe mb’eo, reketse ty bania telo ay, naho mahakama efà raike, vaho ty zonjòn-divay, le nendese’e mb’ añ’ anjomba’ Iehovà e Silò ao, mbe nitora’e i ajajay.
25 Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
Ie linenta i baniay le nendeseñe amy Elý mb’eo i ajajay.
26 Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
Le hoe re: O talèkoo, kanao veloñ’ ain-drehe, ry talèko, izaho i ampela nijohañe marine azo etoa, nilolok’ amy Iehovày.
27 Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
Ty ajaja toy i nihalaliekoy; vaho natolo’ Iehovà amako i nihalaliakoy;
28 Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.
aa le ingo fa hahereko am’ Iehovà, kanao velon-dre le a Iehovà. Aa le niambane añatrefa’ Iehovà re.

< 1 Samueli 1 >