< 1 Samueli 9 >
1 Panali munthu wina wa fuko la Benjamini, wotchuka, dzina lake Kisi, mwana wa Abieli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya.
Kwakulomuntu wakoBhenjamini, indoda elesithunzi, ibizo layo lalinguKhishi indodana ka-Abhiyeli, indodana kaZerori, indodana kaBhekhorathi, indodana ka-Afiya owakoBhenjamini.
2 Iyeyu anali ndi mwana dzina lake Sauli, mnyamata wa maonekedwe abwino. Pakati pa Aisraeli onse panalibe wofanana naye. Anali wamtali kotero kuti anthu onse ankamulekeza mʼmapewa.
Wayelendodana ethiwa nguSawuli, ijaha elilesithunzi kungekho ongalinganiswa lalo phakathi kwama-Israyeli, edlula abantu bonke ngobude kusukela emahlombe kusiya ekhanda.
3 Tsono abulu a Kisi, abambo ake a Sauli anasowa. Choncho Kisi anati kwa mwana wake Sauli, “Tenga wantchito mmodzi ndipo mupite mukafunefune abuluwo.”
Ngalesisikhathi obabhemi bakaKhishi uyise kaSawuli balahleka, uKhishi wasesithi kuSawuli indodana yakhe, “Thatha enye yezinceku uhambe layo ukuyadinga obabhemi.”
4 Choncho iwo anadutsa dziko la mapiri a Efereimu ndi dera la Salisa, koma sanawapeze. Anadutsa ku Saalimu koma abuluwo sanawapeze. Kenaka anadutsa dziko la Benjamini, koma osawapezabe.
Ngakho wadabula elizweni lamaqaqa elako-Efrayimi lasemangweni ozungeze iShalisha, kodwa kababatholanga. Baqhubeka baya esifundeni saseShalimi, kodwa obabhemi babengekho. Wadabula phakathi kwelizwe lakoBhenjamini, kodwa kabawatholanga.
5 Atafika ku dera la Zufi, Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Tiye tibwerere, mwina abambo anga angasiye kudandaula za abulu ndipo adzayamba kudandaula za ife.”
Kwathi sebefikile esifundeni saseZufi, uSawuli wathi encekwini eyayilaye, “Woza, kasibuyele, hlezi ubaba ekele ukucabanga ngabobabhemi aqalise ukukhathazeka ngathi.”
6 Koma mnyamatayo anayankha kuti, “Taonani, mu mzinda uwo muli munthu wa Mulungu. Anthu amamupatsa ulemu kwambiri, ndipo zonse zimene amanena zimachitika. Tiyeni tipite kumeneko tsopano. Mwina adzatiwuza kumene tiyenera kulowera.”
Kodwa inceku yaphendula yathi, “Khangela, kulumuzi kulomuntu kaNkulunkulu; uyahlonitshwa kakhulu, njalo konke akutshoyo kuyenzakala. Kasiye khona khathesi nje. Mhlawumbe angasitshela ukuthi siqonde ngaphi.”
7 Sauli anafunsa mnyamata wake kuti, “Tikapita tikamupatsa chiyani munthuyo pakuti chakudya chimene chinali mʼmatumba mwathu chatha? Tilibe mphatso iliyonse yoti timutengere munthu wa Mulungu. Nanga tili ndi chiyani?”
USawuli wasesithi encekwini, “Singaya kuye, sizamnikani umuntu lowo na? Ukudla kakusekho emigodleni yethu. Kasilasipho esingahamba laso emuntwini kaNkulunkulu. Kuyini esilakho na?”
8 Mnyamatayo anayankha kuti, “Onani, ndili ndi kandalama kakangʼono ka siliva. Ndikamupatsa munthu wa Mulunguyo ndipo akatidziwitsa kumene kuli abuluwo.”
Inceku yaphendula njalo yathi, “Khangela, ngilokwesine kweshekeli elesiliva. Ngizakunika umuntu kaNkulunkulu ukuze asitshele ukuthi siqonde ngaphi.”
9 (Kale mu Israeli ngati munthu afuna kukapempha nzeru kwa Mulungu ankanena kuti, “Tiyeni tipite kwa mlosi.” Ndiye kuti munthu amene lero akutchedwa mneneri, kale ankatchedwa mlosi).
(Ngaphambilini ko-Israyeli, lapho umuntu esiyabuza uNkulunkulu, wayesithi, “Woza, kasiye kumboni,” ngoba umphrofethi wakhathesi wayethiwa ngumboni.)
10 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Chabwino, tiye tipite.” Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda umene kunali munthu wa Mulunguyo.
USawuli wasesithi encekwini yakhe, “Kuhle. Woza kasihambe.” Ngakho basuka baya emzini okwakuhlala khona umuntu kaNkulunkulu.
11 Akukwera phiri kupita ku mzindawo anakumana ndi atsikana akutuluka mu mzindamo kukatunga madzi, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mlosi uja alipo?”
Besaqansa uqaqa besiya kulowomuzi bahlangana lamantombazana ayephume ukuyakukha amanzi basebewabuza besithi, “Kulomboni lapha na?”
12 Iwo anayankha, “Inde alipo. Ali kutsogolo kwanuku, fulumirani tsopano, wangobwera kumene mu mzinda wathu uno lero, chifukwa lero anthu akupereka nsembe ku phiri.
Aphendula athi, “Ukhona. Uphambidlana kwenu. Phangisani khathesi; usanda kufika emzini wethu lamhla, ngoba abantu balomhlatshelo endaweni ephakemeyo.
13 Mukangolowa mu mzindawo mumupeza asanapite ku phiri kukadya. Anthu sangayambe kudya iye asanabwere chifukwa iyeyu ayenera kudalitsa nsembeyo. Kenaka anthu oyitanidwa adzayamba kudya. Pitani tsopano, chifukwa muyenera kumupeza nthawi ino.”
Khonokho nje lingena umuzi, lizamfica engakaqanseli phezulu endaweni ephakemeyo ukuyakudla. Abantu kabayikuqalisa ukudla aze afike, ngoba kumele abusise umhlatshelo; emva kwalokho bazakudla-ke labo abanxusiweyo. Hambani-ke, lizamthola khathesi nje.”
14 Choncho anapita ku mzinda kuja. Akulowa mu mzindamo, anaona Samueli akutuluka mu mzindamo akubwera kumene kunali iwo, koma amapita ku phiri, ku malo wopatulika.
Baya kulowomuzi, kwathi lapho bengena kuwo, babona uSamuyeli esiza kubo eqansela endaweni ephakemeyo.
15 Koma chadzulo lake Sauli asanafike, Yehova anali atamuwuza kale Samueli za zimenezi kuti,
Ngosuku uSawuli engakafiki, uThixo wayeveze lokhu kuSamuyeli wathi,
16 “Mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzakutumizira munthu wochokera ku dziko la Benjamini. Udzamudzoze kuti akhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. Iye adzawapulumutsa mʼdzanja la Afilisti. Ine ndaona kuzunzika kwawo ndipo ndamva kulira kwawo.”
“Ngesikhathi esingaba yisonalesi kusasa ngizaletha kuwe umuntu ovela elizweni lakoBhenjamini. Mgcobe ukuba ngumkhokheli wabantu bami u-Israyeli; uzakhulula abantu bami esandleni samaFilistiya. Ngibakhangele abantu bami, ngoba ukukhala kwabo sekufikile kimi.”
17 Samueli atamuona Sauli, Yehova anamuwuza kuti, “Munthu ndinakuwuza uja ndi uyu. Iyeyu adzalamulira anthu anga.”
Kwathi uSamuyeli ebona uSawuli, uThixo wathi kuye, “Lo nguye umuntu engikhulume kuwe ngaye; uzabusa abantu bami.”
18 Tsono Sauli anayandikira Samueli pa chipata ndipo anamufunsa, “Kodi mungandiwuze kumene kuli nyumba ya mlosi?”
USawuli wasondela kuSamuyeli wabuza wathi, “Ake ungitshele ukuthi indlu yomboni ingaphi.”
19 Samueli anayankha, “Ine ndine mlosiyo. Tsogolani kupita ku phiri pakuti lero mudya ndi ine, ndipo mawa mmawa ndidzakuwuzani zonse zimene zili mu mtima mwanu.
USamuyeli waphendula wathi, “Umboni yimi. Hamba phambi kwami uye endaweni ephakemeyo, ngoba lamhla uzakudla lami, ekuseni ngizakuyekela uhambe njalo ngizakutshela konke okusenhliziyweni yakho.
20 Musadere nkhawa za abulu anu amene akhala akusowa masiku atatu apitawa, poti apezeka kale. Kodi Aisraeli onse akufunitsitsa ndani? Kodi si ndiwe ndi nyumba yonse ya abambo ako?”
Obabhemi abalahlekileyo ensukwini ezintathu ezedluleyo, ungakhathazeki ngabo; sebebonakele. Njalo kungubani izifiso zonke zika-Israyeli ezikhangele kuye nxa kungasuwe lendlu yonke kayihlo na?”
21 Sauli anayankha, “Inetu ndine Mbenjamini, fuko lalingʼono la mafuko onse a Israeli, ndipo banja langa ndi lalingʼono pakati pa mabanja a fuko la Benjamini. Nanga nʼchifukwa chiyani mukunena zimenezi kwa ine?”
USawuli waphendula wathi, “Kodwa mina kangisuye yini wakoBhenjamini, isizwana esincinyane kulazo zonke ko-Israyeli, njalo lendlu yakwethu kayincinyane kulazo zonke izindlu zesizwe sakoBhenjamini na?”
22 Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wake uja ndi kulowa nawo mʼchipinda chachikulu ndipo anawakhazika kutsogolo kwa anthu oyitanidwa. Onse pamodzi analipo anthu makumi atatu.
USamuyeli wasengenisa uSawuli lenceku yakhe endlini enkulu wabahlalisa phambi kwalabo ababenxusiwe babengaba ngamatshumi amathathu ubunengi babo.
23 Tsono Samueli anati kwa wophika, “Bwera nayo nyama imene ndinakupatsa, imene ndinakuwuza kuti uyisunge pambali.”
USamuyeli wasesithi kumpheki wakhe, “Letha iqatha lenyama engikuphe lona, leliyana engithe uligcine.”
24 Kotero wophikayo anatenga mwendo wa nyama ndipo anawuyika patsogolo pa Sauli. Samueli anati “Nayi nyama imene ndinakusungira kuti pa nthawi yake udye pamodzi ndi anthu amene ndawayitana.” Ndipo Sauli anadya tsiku limenelo ndi Samueli.
Ngakho umpheki wathatha umlenze lalokho okwakuphezu kwawo, wakubeka phambi kukaSawuli. USamuyeli wasesithi, “Nanku okube kugcinelwe wena. Dlana, ngoba kade kubekelwe wena kulelithuba, kusukela ngesikhathi ngisithi, ‘Ngilabemzini abanxusiweyo.’” USawuli wadla loSamuyeli ngalolosuku.
25 Atatsika kuchoka ku phiri kuja, Samueli anamukonzera Sauli malo ogona pa denga la nyumba yake, ndipo Sauli anagona pamenepo.
Sebehlile endaweni ephakemeyo ukuya emzini, uSamuyeli wakhuluma loSawuli bephezu kophahla lwendlu yakhe.
26 Tsono mʼbandakucha Samueli anayitana Sauli pa dengapo nati, “Konzeka ndipo ine ndikuperekeza.” Choncho Sauli anadzuka ndipo onse awiri, Samueli ndi Sauli anakalowa mu msewu.
Bavuka ngezikhathi zemadabukakusa, uSamuyeli wabiza uSawuli phezu kophahla wathi, “Lunga ngikuqhube ohanjweni lwakho.” USawuli eselungile, yena loSamuyeli baphuma bonke.
27 Atakafika ku mathero a mzindawo, Samueli anati kwa Sauli, “Muwuzeni mnyamata wanu kuti atsogole, koma inuyo muyime pangʼono kuti ndikuwuzeni mawu ochokera kwa Mulungu.”
Ekuhambeni kwabo besehlela emaphethelweni omuzi, uSamuyeli wathi kuSawuli, “Tshela inceku yakho iqhubeke phambi kwethu” lakanye inceku yenza njalo “kodwa wena sala lapha okwesikhatshana ukuze ngikutshele ilizwi elivela kuNkulunkulu.”