< 1 Samueli 9 >
1 Panali munthu wina wa fuko la Benjamini, wotchuka, dzina lake Kisi, mwana wa Abieli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya.
I Benjamin var der en Mand ved Navn Kisj, en Søn af Abiel, en Søn af Zeror, en Søn af Bekorat, en Søn af Afia, en Benjaminit, en formuende Mand.
2 Iyeyu anali ndi mwana dzina lake Sauli, mnyamata wa maonekedwe abwino. Pakati pa Aisraeli onse panalibe wofanana naye. Anali wamtali kotero kuti anthu onse ankamulekeza mʼmapewa.
Han havde en Søn ved Navn Saul, statelig og smuk, ingen blandt Israeliterne var smukkere end han; han var et Hoved højere end alt Folket.
3 Tsono abulu a Kisi, abambo ake a Sauli anasowa. Choncho Kisi anati kwa mwana wake Sauli, “Tenga wantchito mmodzi ndipo mupite mukafunefune abuluwo.”
Engang var nogle af Sauls Fader Kisjs Æsler blevet borte, og Kisj sagde da til sin Søn Saul: "Tag en af Karlene med og gå ud og søg efter Æslerne!"
4 Choncho iwo anadutsa dziko la mapiri a Efereimu ndi dera la Salisa, koma sanawapeze. Anadutsa ku Saalimu koma abuluwo sanawapeze. Kenaka anadutsa dziko la Benjamini, koma osawapezabe.
De gik så først gennem Efraims Bjerge og Sjalisja egnen, men fandt dem ikke; derefter gik de gennem Sja'alimegnen, men der var de heller ikke; derpå gik de gennem Benjamins Land, men fandt dem ikke.
5 Atafika ku dera la Zufi, Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Tiye tibwerere, mwina abambo anga angasiye kudandaula za abulu ndipo adzayamba kudandaula za ife.”
Da de kom til Zufegnen, sagde Saul til Karlen, som var med ham: "Kom, lad os vende hjem, for at min Fader ikke skal holde op med at tænke på Æslerne og i Stedet blive urolig for os!"
6 Koma mnyamatayo anayankha kuti, “Taonani, mu mzinda uwo muli munthu wa Mulungu. Anthu amamupatsa ulemu kwambiri, ndipo zonse zimene amanena zimachitika. Tiyeni tipite kumeneko tsopano. Mwina adzatiwuza kumene tiyenera kulowera.”
Men han svarede ham: "Se, i Byen der bor en Guds Mand, en anset Mand; hvad han siger, sker altid. Lad os nu gå derhen, måske kan han give os Besked angående det, vi går om."
7 Sauli anafunsa mnyamata wake kuti, “Tikapita tikamupatsa chiyani munthuyo pakuti chakudya chimene chinali mʼmatumba mwathu chatha? Tilibe mphatso iliyonse yoti timutengere munthu wa Mulungu. Nanga tili ndi chiyani?”
Da sagde Saul til Karlen: "Ja, lad os gå derhen! Men hvad skal vi give Manden? Thi vi har ikke mere Brød i vore Tasker, og nogen Gave har vi ikke at give den Guds Mand. Hvad har vi?"
8 Mnyamatayo anayankha kuti, “Onani, ndili ndi kandalama kakangʼono ka siliva. Ndikamupatsa munthu wa Mulunguyo ndipo akatidziwitsa kumene kuli abuluwo.”
Karlen svarede atter Saul: "Se, jeg har en kvart Sekel Sølv, den kan du give den Guds Mand; så siger han os nok Besked om det, vi går om."
9 (Kale mu Israeli ngati munthu afuna kukapempha nzeru kwa Mulungu ankanena kuti, “Tiyeni tipite kwa mlosi.” Ndiye kuti munthu amene lero akutchedwa mneneri, kale ankatchedwa mlosi).
Fordum sagde man i Israel, når man gik hen for at rådspørge Gud: "Kom, lad os gå til Seeren!" Thi hvad man nu til Dags kalder en Profet, kaldte man fordum en Seer.
10 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Chabwino, tiye tipite.” Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda umene kunali munthu wa Mulunguyo.
Da sagde Saul til Karlen: "Du har Ret! Kom, lad os gå derhen!" Så gik de hen til Byen, hvor den Guds Mand boede.
11 Akukwera phiri kupita ku mzindawo anakumana ndi atsikana akutuluka mu mzindamo kukatunga madzi, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mlosi uja alipo?”
Som de nu gik ad Vejen op til Byen, traf de nogle unge Piger, der gik ud for at øse Vand, og de spurgte dem: "Er Seeren her?"
12 Iwo anayankha, “Inde alipo. Ali kutsogolo kwanuku, fulumirani tsopano, wangobwera kumene mu mzinda wathu uno lero, chifukwa lero anthu akupereka nsembe ku phiri.
De svarede dem: "Ja, han er foran; han kom til Byen lige nu. Folket ofrer nemlig i Dag et Slagtoffer på Offerhøjen.
13 Mukangolowa mu mzindawo mumupeza asanapite ku phiri kukadya. Anthu sangayambe kudya iye asanabwere chifukwa iyeyu ayenera kudalitsa nsembeyo. Kenaka anthu oyitanidwa adzayamba kudya. Pitani tsopano, chifukwa muyenera kumupeza nthawi ino.”
Når I blot går ind i Byen, kan I træffe ham, før han går op på Offerhøjen til Måltidet; thi Folket spiser ikke, før han kommer, da han skal velsigne Slagtofferet; så først spiser de indbudne. Gå nu op til Byen, thi netop nu kan I træffe ham!"
14 Choncho anapita ku mzinda kuja. Akulowa mu mzindamo, anaona Samueli akutuluka mu mzindamo akubwera kumene kunali iwo, koma amapita ku phiri, ku malo wopatulika.
De gik så op til Byen; og som de gik ind igennem Porten, kom Samuel gående imod dem på Vej op til Offerhøjen.
15 Koma chadzulo lake Sauli asanafike, Yehova anali atamuwuza kale Samueli za zimenezi kuti,
HERREN havde Dagen før Sauls Komme åbnet Samuels Øre og sagt:
16 “Mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzakutumizira munthu wochokera ku dziko la Benjamini. Udzamudzoze kuti akhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. Iye adzawapulumutsa mʼdzanja la Afilisti. Ine ndaona kuzunzika kwawo ndipo ndamva kulira kwawo.”
"I Morgen ved denne Tid sender jeg en Mand til dig fra Benjamins Land; ham skal du salve til Fyrste over mit Folk Israel; han skal frelse mit Folk fra Filisternes Hånd; thi jeg har givet Agt på mit Folks Nød, dets Klageråb har nået mig!"
17 Samueli atamuona Sauli, Yehova anamuwuza kuti, “Munthu ndinakuwuza uja ndi uyu. Iyeyu adzalamulira anthu anga.”
Og straks da Samuel fik Øje på Saul, sagde HERREN til ham: "Se, der er den Mand, om hvem jeg sagde til dig: Han skal herske over mit Folk!"
18 Tsono Sauli anayandikira Samueli pa chipata ndipo anamufunsa, “Kodi mungandiwuze kumene kuli nyumba ya mlosi?”
Da trådte Saul hen til Samuel midt i Porten og sagde: "Vær så god at sige mig, hvor Seerens Hus er!"
19 Samueli anayankha, “Ine ndine mlosiyo. Tsogolani kupita ku phiri pakuti lero mudya ndi ine, ndipo mawa mmawa ndidzakuwuzani zonse zimene zili mu mtima mwanu.
Samuel svarede: "Seeren det er mig; gå i Forvejen op på Offerhøjen; du skal spise sammen med mig i Dag; i Morgen skal jeg følge dig på Vej og kundgøre dig alt, hvad der er i dit Hjerte;
20 Musadere nkhawa za abulu anu amene akhala akusowa masiku atatu apitawa, poti apezeka kale. Kodi Aisraeli onse akufunitsitsa ndani? Kodi si ndiwe ndi nyumba yonse ya abambo ako?”
for Æslerne, som for tre Dage siden blev borte for dig, skal du ikke ængste dig; de et fundet. Men til hvem står alt Israels Begær uden til dig og hele dit Fædrenehus?"
21 Sauli anayankha, “Inetu ndine Mbenjamini, fuko lalingʼono la mafuko onse a Israeli, ndipo banja langa ndi lalingʼono pakati pa mabanja a fuko la Benjamini. Nanga nʼchifukwa chiyani mukunena zimenezi kwa ine?”
Da svarede Saul: "Er jeg ikke fra Benjamin, Israels mindste Stamme? Og min Slægt er den ringeste af alle Benjamins Stammes Slægter. Hvor kan du da tale således til mig?"
22 Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wake uja ndi kulowa nawo mʼchipinda chachikulu ndipo anawakhazika kutsogolo kwa anthu oyitanidwa. Onse pamodzi analipo anthu makumi atatu.
Men Samuel tog Saul og hans Karl, førte dem til Gildesalen og gav dem Plads øverst blandt de indbudne der var omtrent tredive Mænd
23 Tsono Samueli anati kwa wophika, “Bwera nayo nyama imene ndinakupatsa, imene ndinakuwuza kuti uyisunge pambali.”
og Samuel sagde til Kokken: "Ræk mig det Stykke, jeg gav dig og sagde, du skulde lægge til Side!"
24 Kotero wophikayo anatenga mwendo wa nyama ndipo anawuyika patsogolo pa Sauli. Samueli anati “Nayi nyama imene ndinakusungira kuti pa nthawi yake udye pamodzi ndi anthu amene ndawayitana.” Ndipo Sauli anadya tsiku limenelo ndi Samueli.
Da tog Kokken Køllen og satte den for Saul. Og Samuel sagde: "Se, Kødet står for dig, spis! Thi til den fastsatte Tid har man ventet dig, for at du kunde spise sammen med de indbudne." Så spiste Saul sammen med Samuel den Dag.
25 Atatsika kuchoka ku phiri kuja, Samueli anamukonzera Sauli malo ogona pa denga la nyumba yake, ndipo Sauli anagona pamenepo.
Derpå steg de ned fra Offerhøjen fil Byen, og der blev redt til Saul på Taget.
26 Tsono mʼbandakucha Samueli anayitana Sauli pa dengapo nati, “Konzeka ndipo ine ndikuperekeza.” Choncho Sauli anadzuka ndipo onse awiri, Samueli ndi Sauli anakalowa mu msewu.
Så lagde han sig til Hvile. Tidligt om Morgenen, da Morgenrøden brød frem, råbte Samuel til Saul oppe på Taget: "Stå op, jeg vil følge dig på Vej!" Da stod Saul op, og han og Samuel gik ud sammen,
27 Atakafika ku mathero a mzindawo, Samueli anati kwa Sauli, “Muwuzeni mnyamata wanu kuti atsogole, koma inuyo muyime pangʼono kuti ndikuwuzeni mawu ochokera kwa Mulungu.”
Men da de på Nedvejen var kommet til Udkanten af Byen, sagde Samuel til Saul: "Sig til Karlen, at han skal gå i Forvejen! Men bliv du stående et Øjeblik, så vil jeg kundgøre dig Guds Ord!"