< 1 Samueli 9 >

1 Panali munthu wina wa fuko la Benjamini, wotchuka, dzina lake Kisi, mwana wa Abieli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya.
Byl pak muž z pokolení Beniamin, jménem Cis, syn Abiele syna Seror, syna Bechorat, syna Afia, syna muže Jemini, muž udatný.
2 Iyeyu anali ndi mwana dzina lake Sauli, mnyamata wa maonekedwe abwino. Pakati pa Aisraeli onse panalibe wofanana naye. Anali wamtali kotero kuti anthu onse ankamulekeza mʼmapewa.
Ten měl syna jménem Saule, mládence krásného, tak že žádného z synů Izraelských nebylo pěknějšího nad něj; od ramene svého vzhůru převyšoval všecken lid.
3 Tsono abulu a Kisi, abambo ake a Sauli anasowa. Choncho Kisi anati kwa mwana wake Sauli, “Tenga wantchito mmodzi ndipo mupite mukafunefune abuluwo.”
Byly se pak ztratily oslice Cis, otce Saulova. I řekl Cis Saulovi synu svému: Vezmi i hned s sebou jednoho z služebníků, a vstana, jdi, hledej oslic.
4 Choncho iwo anadutsa dziko la mapiri a Efereimu ndi dera la Salisa, koma sanawapeze. Anadutsa ku Saalimu koma abuluwo sanawapeze. Kenaka anadutsa dziko la Benjamini, koma osawapezabe.
A tak šel přes horu Efraim, a prošel až do země Salisa, a nic nenalezli; prošli také zemi Sálim, a nic nenalezli. Ještě přešli i zemi Jemini, a nenalezli.
5 Atafika ku dera la Zufi, Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Tiye tibwerere, mwina abambo anga angasiye kudandaula za abulu ndipo adzayamba kudandaula za ife.”
Když pak přišli do země Zuf, řekl Saul služebníku svému, kterýž byl s ním: Poď, a navraťme se, aby otec můj nechaje těch oslic, neměl starosti o nás.
6 Koma mnyamatayo anayankha kuti, “Taonani, mu mzinda uwo muli munthu wa Mulungu. Anthu amamupatsa ulemu kwambiri, ndipo zonse zimene amanena zimachitika. Tiyeni tipite kumeneko tsopano. Mwina adzatiwuza kumene tiyenera kulowera.”
Kterýž řekl jemu: Aj, nyní muž Boží jest v městě tomto, a muž ten jest znamenitý; cožkoli praví, všecko se tak stává. Medle, jděme tam, zdali by oznámil nám cestu naši, kterouž bychom jíti měli.
7 Sauli anafunsa mnyamata wake kuti, “Tikapita tikamupatsa chiyani munthuyo pakuti chakudya chimene chinali mʼmatumba mwathu chatha? Tilibe mphatso iliyonse yoti timutengere munthu wa Mulungu. Nanga tili ndi chiyani?”
Odpověděl Saul služebníku svému: Aj, půjdeme. Co pak přineseme muži tomu? Nebo jsme chléb vytrávili z pytlíků našich, ani daru nemáme, kterýž bychom přinesli muži Božímu. Což máme?
8 Mnyamatayo anayankha kuti, “Onani, ndili ndi kandalama kakangʼono ka siliva. Ndikamupatsa munthu wa Mulunguyo ndipo akatidziwitsa kumene kuli abuluwo.”
I doložil služebník, odpovídaje Saulovi, a řekl: Hle, nalezl jsem u sebe čtvrt lotu stříbra; to dám muži Božímu, aby nám oznámil cestu naši.
9 (Kale mu Israeli ngati munthu afuna kukapempha nzeru kwa Mulungu ankanena kuti, “Tiyeni tipite kwa mlosi.” Ndiye kuti munthu amene lero akutchedwa mneneri, kale ankatchedwa mlosi).
(Za starodávna v Izraeli tak říkával každý, kdož jíti měl raditi se s Bohem: Poďte, a půjdeme až k vidoucímu. Nebo ten, kterýž nyní slove prorok, za starodávna sloul vidoucí.)
10 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Chabwino, tiye tipite.” Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda umene kunali munthu wa Mulunguyo.
Řekl tedy Saul služebníku svému: Dobrá jest řeč tvá, nu, jděmež. I šli do města, v kterémž byl muž Boží.
11 Akukwera phiri kupita ku mzindawo anakumana ndi atsikana akutuluka mu mzindamo kukatunga madzi, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mlosi uja alipo?”
A když vcházeli na horu města, potkali se s děvečkami, vycházejícími vážit vody. I řekli jim: Jest-li zde vidoucí?
12 Iwo anayankha, “Inde alipo. Ali kutsogolo kwanuku, fulumirani tsopano, wangobwera kumene mu mzinda wathu uno lero, chifukwa lero anthu akupereka nsembe ku phiri.
Kteréž odpověděly jim a řekly: Jest. Hle, a on před tebou, pospěš tedy; nebo dnes přišel do města, proto že obětuje dnes lid na té hoře.
13 Mukangolowa mu mzindawo mumupeza asanapite ku phiri kukadya. Anthu sangayambe kudya iye asanabwere chifukwa iyeyu ayenera kudalitsa nsembeyo. Kenaka anthu oyitanidwa adzayamba kudya. Pitani tsopano, chifukwa muyenera kumupeza nthawi ino.”
Hned jakž vejdete do města, tedy naleznete ho, prvé než vstoupí na horu k jídlu. Lid zajisté nebude jísti, dokudž on nepřijde, nebo on požehná obětí, a potom pozvaní jísti budou. A protož jděte, nebo v tuto chvíli naleznete ho.
14 Choncho anapita ku mzinda kuja. Akulowa mu mzindamo, anaona Samueli akutuluka mu mzindamo akubwera kumene kunali iwo, koma amapita ku phiri, ku malo wopatulika.
I šli do města. A když vcházeli do prostřed města, aj, Samuel vycházel proti nim, aby vstoupil na tu horu.
15 Koma chadzulo lake Sauli asanafike, Yehova anali atamuwuza kale Samueli za zimenezi kuti,
Hospodin pak zjevil Samuelovi o jeden den prvé, nežli přišel Saul, řka:
16 “Mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzakutumizira munthu wochokera ku dziko la Benjamini. Udzamudzoze kuti akhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. Iye adzawapulumutsa mʼdzanja la Afilisti. Ine ndaona kuzunzika kwawo ndipo ndamva kulira kwawo.”
V tuto chvíli zítra pošli k tobě muže z země Beniamin, kteréhož pomažeš, aby byl vůdce lidu mého Izraelského, a vysvobodíť lid můj z ruky Filistinských; vzhlédlť jsem zajisté na lid svůj, nebo přišlo volání jeho ke mně.
17 Samueli atamuona Sauli, Yehova anamuwuza kuti, “Munthu ndinakuwuza uja ndi uyu. Iyeyu adzalamulira anthu anga.”
A když Samuel uzřel Saule, řekl jemu Hospodin: Aj, teď ten muž, o kterémž pravil jsem tobě: tenť spravovati bude lid můj.
18 Tsono Sauli anayandikira Samueli pa chipata ndipo anamufunsa, “Kodi mungandiwuze kumene kuli nyumba ya mlosi?”
Tedy přistoupil Saul k Samuelovi v bráně, a řekl: Ukaž mi, prosím, kde jest tuto dům vidoucího?
19 Samueli anayankha, “Ine ndine mlosiyo. Tsogolani kupita ku phiri pakuti lero mudya ndi ine, ndipo mawa mmawa ndidzakuwuzani zonse zimene zili mu mtima mwanu.
I odpověděl Samuel Saulovi: Já jsem vidoucí. Vstupiž přede mnou na horu, a budete dnes jísti se mnou; potom ráno propustím tě, a cožkoli jest v srdci tvém, oznámím tobě.
20 Musadere nkhawa za abulu anu amene akhala akusowa masiku atatu apitawa, poti apezeka kale. Kodi Aisraeli onse akufunitsitsa ndani? Kodi si ndiwe ndi nyumba yonse ya abambo ako?”
O oslice pak, kteréžť se ztratily dnes třetí den, nic se nestarej, nebo nalezeny jsou. Ale na koho žádost všeho Izraele? Zdali ne na tebe a na všecken dům otce tvého?
21 Sauli anayankha, “Inetu ndine Mbenjamini, fuko lalingʼono la mafuko onse a Israeli, ndipo banja langa ndi lalingʼono pakati pa mabanja a fuko la Benjamini. Nanga nʼchifukwa chiyani mukunena zimenezi kwa ine?”
I odpověděl Saul a řekl: Zdaliž já nejsem syn Jemini, z nejmenšího pokolení Izraelského? Ano i čeled má jest nejchaternejší ze všech čeledí pokolení Beniaminova. Pročež jsi tedy ke mně mluvil taková slova?
22 Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wake uja ndi kulowa nawo mʼchipinda chachikulu ndipo anawakhazika kutsogolo kwa anthu oyitanidwa. Onse pamodzi analipo anthu makumi atatu.
A pojav Samuel Saule i služebníka jeho, uvedl je do pokoje, a dal jim místo nejpřednější mezi pozvanými, jichž bylo okolo třidcíti mužů.
23 Tsono Samueli anati kwa wophika, “Bwera nayo nyama imene ndinakupatsa, imene ndinakuwuza kuti uyisunge pambali.”
I řekl Samuel kuchaři: Dej sem ten díl, kterýž jsem dal tobě, o kterémžť jsem řekl: Schovej jej obzvláštně.
24 Kotero wophikayo anatenga mwendo wa nyama ndipo anawuyika patsogolo pa Sauli. Samueli anati “Nayi nyama imene ndinakusungira kuti pa nthawi yake udye pamodzi ndi anthu amene ndawayitana.” Ndipo Sauli anadya tsiku limenelo ndi Samueli.
Když tedy přinesl kuchař plece i s tím, což se ho přídrželo, položil Samuel před Saule, a řekl: Teď, což pozůstalo, vezmi sobě, jez; až k této chvíli zajisté zachováno jest to pro tebe, jakž jsem řekl: Lidu jsem pozval. I jedl Saul s Samuelem v ten den.
25 Atatsika kuchoka ku phiri kuja, Samueli anamukonzera Sauli malo ogona pa denga la nyumba yake, ndipo Sauli anagona pamenepo.
A když sešli s hory do města, mluvil s Saulem na vrchní podlaze.
26 Tsono mʼbandakucha Samueli anayitana Sauli pa dengapo nati, “Konzeka ndipo ine ndikuperekeza.” Choncho Sauli anadzuka ndipo onse awiri, Samueli ndi Sauli anakalowa mu msewu.
Potom vstali velmi ráno. I stalo se, když záře vzcházela, že zavolal Samuel Saule na hůru, řka: Vstaň, a propustím tě. Vstal tedy Saul, a vyšli oba ven, on i Samuel.
27 Atakafika ku mathero a mzindawo, Samueli anati kwa Sauli, “Muwuzeni mnyamata wanu kuti atsogole, koma inuyo muyime pangʼono kuti ndikuwuzeni mawu ochokera kwa Mulungu.”
A když přicházeli na konec města, řekl Samuel Saulovi: Rci služebníku, ať jde napřed, (i šel); ty pak pozastav se málo, ažť oznámím řeč Boží.

< 1 Samueli 9 >