< 1 Samueli 8 >

1 Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
Samuel yaşlanınca oğullarını İsrail'e önder atadı.
2 Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
Beer-Şeva'da görev yapan ilk oğlunun adı Yoel, ikinci oğlunun adıysa Aviya'ydı.
3 Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
Ama oğulları onun yolunda yürümediler. Tersine, haksız kazanca yönelip rüşvet alır, yargıda yan tutarlardı.
4 Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
Bu yüzden İsrail'in bütün ileri gelenleri toplanıp Rama'ya, Samuel'in yanına vardılar.
5 Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
Ona, “Bak, sen yaşlandın” dediler, “Oğulların da senin yolunda yürümüyor. Şimdi, öteki uluslarda olduğu gibi, bizi yönetecek bir kral ata.”
6 Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
Ne var ki, “Bizi yönetecek bir kral ata” demeleri Samuel'in hoşuna gitmedi. Samuel RAB'be yakardı.
7 Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
RAB, Samuel'e şu karşılığı verdi: “Halkın sana bütün söylediklerini dinle. Çünkü reddettikleri sen değilsin; kralları olarak beni reddettiler.
8 Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
Onları Mısır'dan çıkardığım günden bu yana bütün yaptıklarının aynısını sana da yapıyorlar. Beni bırakıp başka ilahlara kulluk ettiler.
9 Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
Şimdi onları dinle. Ancak onları açıkça uyar ve kendilerine krallık yapacak kişinin onları nasıl yöneteceğini söyle.”
10 Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
Samuel kendisinden kral isteyen halka RAB'bin bütün söylediklerini bildirdi:
11 Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
“Size krallık yapacak kişinin yönetimi şöyle olacak: Oğullarınızı alıp savaş arabalarında ve atlı birliklerinde görevlendirecek. Onun savaş arabalarının önünde koşacaklar.
12 Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
Bazılarını biner, bazılarını ellişer kişilik birliklere komutan atayacak. Kimisini toprağını sürüp ekinini biçmek, kimisini de silahların ve savaş arabalarının donatımını yapmak için görevlendirecek.
13 Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
Kızlarınızı ıtriyatçı, aşçı, fırıncı olmak üzere alacak.
14 Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
Seçkin tarlalarınızı, bağlarınızı, zeytinliklerinizi alıp hizmetkârlarına verecek.
15 Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
Tahıllarınızın, üzümlerinizin ondalığını alıp saray görevlileriyle öbür hizmetkârlarına dağıtacak.
16 Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
Kadın erkek kölelerinizi, seçkin boğalarınızı, eşeklerinizi alıp kendi işinde çalıştıracak.
17 Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
Sürülerinizin de ondalığını alacak. Sizler ise onun köleleri olacaksınız.
18 Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
Bunlar gerçekleştiğinde, seçtiğiniz kral yüzünden feryat edeceksiniz. Ama RAB o gün size karşılık vermeyecek.”
19 Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
Ne var ki, halk Samuel'in sözünü dinlemek istemedi. “Hayır, bizi yönetecek bir kral olsun” dediler,
20 Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
“Böylece biz de bütün uluslar gibi olacağız. Kralımız bizi yönetecek, önümüzden gidip savaşlarımızı sürdürecek.”
21 Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
Halkın bütün söylediklerini dinleyen Samuel, bunları RAB'be aktardı.
22 Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”
RAB Samuel'e, “Onların sözünü dinle ve başlarına bir kral ata” diye buyurdu. Bunun üzerine Samuel İsrailliler'e, “Herkes kendi kentine dönsün” dedi.

< 1 Samueli 8 >