< 1 Samueli 8 >
1 Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
Şamuel q'əs qıxhamee, dixbışike İzrailis haakimar haa'a.
2 Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
Mang'une ts'erriyne duxayn do Yoel, q'ör'esıng'unud Aviya ıxha. Manbışe Beer-Şevee haakimiyvalla haa'a vuxha.
3 Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
Dixbı dekkıne yəqqı'n avayk'an deş. Manbı haramne pılıqab qihna gyabak'a, ruşvatbı alyaat'a, qotkuda deşin q'aralybı hele ıxha.
4 Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
Gırgın İzrailin ağsaqqalar Ramayeeqa sabı, Şamuelyne k'anyaqa abı,
5 Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
mang'uk'le eyhen: – Ğu q'əs qıxha, yiğın dixbımee yiğne yəqqı'n əlyhəə deş. Həşdeme menne milletbışika nəxürnayiy, şasdar həməxürna sa paççah gixhxhe. Şas xəbvalla hee'ecen.
6 Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
Manbışe: «Şasdar sa paççah gixhxhe, mang'vee şas xəbvalla hee'ecenva» uvhuyng'a, Şamuelis manbışe uvhuyn ıkkiykan deş. Mang'vee Rəbbis düə haa'a.
7 Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
Rəbbee Şamuelik'le eyhen: – Milletın eyhene gırgınçil k'ırı alixhxhe. Manbışe ğu deş, Zı əq'əna qa'a. Manbışis Zı cona Paççah ıxha ıkkan deş.
8 Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
Zı manbı Misirğançe qığav'uyne yiğıle, g'iyniyne yiğılqamee manbışe menne allahaaşis ı'bəədatbı hı'ı. Məxüb manbı Zake əq'əna qeepxha. Zak hı'iyn kar, manbışe həşded vak ha'a.
9 Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
Ğu manbışe eyhençil k'ırı alixhxhıyle qiyğa, ğu manbışilqa yugda hixhar he'e, cos xəbvalla haa'asde paççahee xəbvalla nəxübiy haa'as.
10 Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
Şamuelee cuke paççah heqqane milletılqa, Rəbbee uvhuyn cuvab hixhar ha'an.
11 Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
Mang'vee eyhen: – Şos xəbvalla haa'asde paççahee, xəbvalla inəxüb haa'as: mang'vee vuşun dixbı sav'u, quvkeesınbı. Dəv'əyne daşk'abışiliy balkanaaşil cus g'ullux haa'as alivkas. Manbıb mang'une daşk'abışde ögee g'adaaxvanas.
12 Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
Manbışde sanbışike aazırıng'us, sanbışikeb xhots'aling'us ç'ak'ınbı haa'as. Mansanbıb cun cigabı ezas, şagav sa'as g'axuvles. Avxuynbışisqad silahiy dəv'əyne daşk'abışis kara'alesın karbı ha'as alikkas.
13 Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
Mang'vee vuşun yişba ətirbıyiy otxhuniybı ha'as, gıneybı qecesva vukkees.
14 Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
Mang'vee vuşun inekke yugun çolbıyiy t'ımıllığbı, zeytunun bağbı xılençe g'ayşu, cune insanaaşis heles.
15 Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
Mang'vee vuşde sukukeyiy t'ımılike yits'ıb'esda pay alyapt'ı, məmuraaşisiy cune insanaaşis hevles.
16 Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
Vuşun g'ular – adamer, yadar – vuşun mek'vunbı, vuşun əməlerıd çikana mang'vee cus alyaat'as.
17 Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
Vuşde vəq'əbışda yits'ıb'esda pay mang'vee cus alyapt'as, şunab mang'un nukarar vuxhes.
18 Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
Yiğ qalesın, şu g'əyxı'yne paççahne xıleençe, Allahılqa şucad xıleppı aaqas, Mang'vee şu g'attivxhan hee'ecenva. Rəbbeemee mane gahıl şos cuvab qeles deş.
19 Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
Milletısmee, Şamuelyne cuvabıl k'ırı alixhxhes diykkın, eyhen: – De'eş, şal oğa paççah ıxha şas ıkkan.
20 Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
Havaasre menne milletbışis nəxübiy, şasıb paççahee xəbvalla hee'ecen. Dəv'ə gipxhımeeyib, yişde ögee hooracen.
21 Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
Milletın eyhen gırgın yik'el aqqı, qiyğale man Şamuelee Rəbbis yuşan ha'a.
22 Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”
Rəbbee Şamuelik'le eyhen: – Manbışe eyhençil k'ırı alixhxhı, manbışis sa paççah gixhxhe. Manke Şamuelee İzrailybışik'le «Gırgınbı vuşde şaharbışeeqa savk'leva» eyhe.