< 1 Samueli 8 >

1 Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
Quand Samuel fut devenu vieux, il établit ses fils pour juges sur Israël.
2 Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
Son premier-né s'appelait Joël, et le second Abija; et ils jugeaient à Béer-Shéba.
3 Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
Et ses fils ne marchèrent point dans ses voies, mais ils s'en détournèrent pour rechercher le gain; et ils prenaient des présents, et pervertissaient le droit.
4 Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
Alors tous les anciens d'Israël s'assemblèrent, et vinrent vers Samuel à Rama;
5 Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
Et ils lui dirent: Voici, tu es devenu vieux, et tes fils ne marchent point dans tes voies; maintenant, établis sur nous un roi pour nous juger, comme en ont toutes les nations.
6 Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
Et cette parole déplut à Samuel, parce qu'ils avaient dit: Donne-nous un roi pour nous juger; et Samuel pria l'Éternel.
7 Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
Et l'Éternel dit à Samuel: Obéis à la voix du peuple, en tout ce qu'ils te diront; car ce n'est pas toi qu'ils ont rejeté, mais c'est moi qu'ils ont rejeté, afin que je ne règne point sur eux.
8 Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
Conformément à toutes les actions qu'ils ont faites, depuis le jour où je les ai fait monter hors d'Égypte jusqu'à ce jour, et de même qu'ils m'ont abandonné et ont servi d'autres dieux, ils agissent aussi de même à ton égard.
9 Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
Maintenant donc, obéis à leur voix; seulement ne manque point de protester contre eux, et de leur déclarer comment le roi, qui régnera sur eux, les traitera.
10 Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
Alors Samuel dit toutes les paroles de l'Éternel au peuple, qui lui avait demandé un roi.
11 Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
Et il dit: Voici comment vous traitera le roi qui régnera sur vous. Il prendra vos fils, et les mettra sur ses chars et parmi ses cavaliers, et ils courront devant son char;
12 Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
Il les prendra aussi pour en faire ses chefs de milliers, et ses chefs de cinquantaines; pour labourer ses champs, pour récolter sa moisson, et pour faire ses instruments de guerre, et l'attirail de ses chars.
13 Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
Il prendra aussi vos filles, pour en faire des parfumeuses, des cuisinières, et des boulangères;
14 Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
Il prendra aussi vos champs, vos vignes et vos oliviers les meilleurs, et les donnera à ses serviteurs.
15 Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
Il lèvera la dîme de vos grains et de vos vignes, et la donnera à ses eunuques et à ses serviteurs;
16 Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
Il prendra vos serviteurs et vos servantes, et l'élite de vos jeunes gens, et vos ânes, et les emploiera à ses ouvrages;
17 Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
Il dîmera vos troupeaux, et vous serez ses esclaves.
18 Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
Vous crierez, en ce jour-là, à cause de votre roi, que vous vous serez choisi, mais l'Éternel ne vous exaucera point.
19 Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
Mais le peuple refusa d'écouter la voix de Samuel, et ils dirent: Non! mais il y aura un roi sur nous,
20 Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
Et nous serons, nous aussi, comme toutes les nations; et notre roi nous jugera, et sortira devant nous, et conduira nos guerres.
21 Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
Et Samuel entendit toutes les paroles du peuple, et les rapporta aux oreilles de l'Éternel.
22 Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”
Et l'Éternel dit à Samuel: Obéis à leur voix, et établis-leur un roi. Et Samuel dit aux hommes d'Israël: Allez-vous-en chacun en sa ville.

< 1 Samueli 8 >