< 1 Samueli 8 >
1 Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
And it came to pass, when Samuel was old, that he made his sons judges over Israel.
2 Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
Now the name of his first-born was Joel; and the name of his second, Abijah; they were judges in Beer-sheba.
3 Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
And his sons walked not in his ways, but turned aside after lucre, and took bribes, and perverted justice.
4 Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
Then all the elders of Israel gathered themselves together, and came to Samuel unto Ramah.
5 Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
And they said unto him: 'Behold, thou art old, and thy sons walk not in thy ways; now make us a king to judge us like all the nations.'
6 Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
But the thing displeased Samuel, when they said: 'Give us a king to judge us.' And Samuel prayed unto the LORD.
7 Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
And the LORD said unto Samuel: 'Hearken unto the voice of the people in all that they say unto thee; for they have not rejected thee, but they have rejected Me, that I should not be king over them.
8 Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
According to all the works which they have done since the day that I brought them up out of Egypt even unto this day, in that they have forsaken Me, and served other gods, so do they also unto thee.
9 Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
Now therefore hearken unto their voice; howbeit thou shalt earnestly forewarn them, and shalt declare unto them the manner of the king that shall reign over them.'
10 Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
And Samuel told all the words of the LORD unto the people that asked of him a king.
11 Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
And he said: 'This will be the manner of the king that shall reign over you: he will take your sons, and appoint them unto him, for his chariots, and to be his horsemen; and they shall run before his chariots.
12 Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
And he will appoint them unto him for captains of thousands, and captains of fifties; and to plow his ground, and to reap his harvest, and to make his instruments of war, and the instruments of his chariots.
13 Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
And he will take your daughters to be perfumers, and to be cooks, and to be bakers.
14 Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
And he will take your fields, and your vineyards, and your oliveyards, even the best of them, and give them to his servants.
15 Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
And he will take the tenth of your seed, and of your vineyards, and give to his officers, and to his servants.
16 Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
And he will take your men-servants, and your maid-servants, and your goodliest young men, and your asses, and put them to his work.
17 Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
He will take the tenth of your flocks; and ye shall be his servants.
18 Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
And ye shall cry out in that day because of your king whom ye shall have chosen you; and the LORD will not answer you in that day.'
19 Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
But the people refused to hearken unto the voice of Samuel; and they said: 'Nay; but there shall be a king over us;
20 Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
that we also may be like all the nations; and that our king may judge us, and go out before us, and fight our battles.'
21 Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
And Samuel heard all the words of the people, and he spoke them in the ears of the LORD.
22 Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”
And the LORD said to Samuel: 'Hearken unto their voice, and make them a king.' And Samuel said unto the men of Israel: 'Go ye every man unto his city.'